《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (6) 章: 艾尔拉
سَنُقۡرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
[419] Mneneri Muhammad (s.a.w) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka atatu m’Swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa Qur’an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa kuti angaiwale. Choncho, apa Allah akumuletsa kuti asadzivutitse kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa lonjezo Lake. Mtumiki (s.a.w) adali kumtsikira ma surah aataliatali ndipo amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba. Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (6) 章: 艾尔拉
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭