وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی البلد   ئایه‌تی:

سورەتی البلد

لَآ أُقۡسِمُ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndikulumbilira mzinda uwu (wa Makka).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأَنتَ حِلُّۢ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndipo iwe udzatsikira mu mzindawu mwa ufulu (ndi kuuonjezera ulemelero).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَوَالِدٖ وَمَا وَلَدَ
Ndiponso ndikulumbilira chobereka ndi choberekedwa, (kudzera mwa iwo mtundu wa anthu udasungidwa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِي كَبَدٍ
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
[439] Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake, chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe kupilira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda chida. Ndipo pamwamba pa izi, Allah wamukakamiza zinthu zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye achita chikulembedwa. Pa tsiku lachimaliziro adzawerengedwa chilichonse chimene adachichita; chachikulu kapena chaching’ono.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّن يَقۡدِرَ عَلَيۡهِ أَحَدٞ
Kodi (munthu wolengedwa ndi mavutoyu) akuganiza kuti palibe amene angamuthe? [440]
[440] Tanthauzo lake apa nkuti munthu akuganiza kuti palibe aliyense amene angamuweruze pa zolakwa zake.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَقُولُ أَهۡلَكۡتُ مَالٗا لُّبَدًا
Akunena (monyadira kuti): “Ndaononga chuma chambiri (chifukwa choletsa Chisilamu kufala).”[441]
[441] (Ndime 6-7) Mawu awa akunenedwa kwa okanira omwe adali kupereka chuma chawo pomenyana ndi Usilamu kapena kufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Kenako adali kudzitama chifukwa chopereka chuma chambiri pa njirayo. Izi zikumukhudza aliyense amene akufuna kuti Chisilamu chionongeke. Ndipo iwo amaganiza kuti Allah sakudziwa za maganizo awo oipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّمۡ يَرَهُۥٓ أَحَدٌ
Kodi akuganiza kuti palibe akumuona?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَلَمۡ نَجۡعَل لَّهُۥ عَيۡنَيۡنِ
Kodi sitidampangire maso awiri (amene akuyang’anira)?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلِسَانٗا وَشَفَتَيۡنِ
Ndilirime ndi milomo iwiri (zimene akulankhulira)?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَهَدَيۡنَٰهُ ٱلنَّجۡدَيۡنِ
Ndipo tamlongosolera njira ziwiri: (yabwino ndi yoipa, ndipo tampatsa mphamvu yosankhira njira imene akufuna).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَا ٱقۡتَحَمَ ٱلۡعَقَبَةَ
Kodi walikwera phiri lovutalo (lomwe lingakamfikitse ku Jannah)?[442]
[442] Tanthauzo lake ndikuti bwanji munthu sathokoza chifundo chimenechi (chopatsidwa maso ndi pakamwa) pogwiritsa ntchito chuma chake pa zinthu zabwino zimene Allah wazitchula m’ma Ayah akubwerawa? Ndipo tanthauzo la “kukwera phiri lovuta’’ ndiko kupereka chuma panjira ya Allah chimene chili ndinthu chovuta kwa anthu ambiri ndipo chimafanana ndikukwera phiri losongoka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡعَقَبَةُ
Nanga nchiyani chakudziwitsa za kukwera phiri lovutalo?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَكُّ رَقَبَةٍ
(Kutero ndiko) kupereka ufulu kwa kapolo,
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوۡ إِطۡعَٰمٞ فِي يَوۡمٖ ذِي مَسۡغَبَةٖ
Kapena kuwadyetsa (osowa) pa tsiku la njala,
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَتِيمٗا ذَا مَقۡرَبَةٍ
Amasiye achibale,
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوۡ مِسۡكِينٗا ذَا مَتۡرَبَةٖ
Kapena wosauka wa fumbi lokhalokha (chifukwa cha kuvutika kwambiri),
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ثُمَّ كَانَ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡمَرۡحَمَةِ
Komanso nakhala mmodzi mwa okhulupirira ndikumalangizana za kupirira, ndi kumalangizananso za chifundo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Otero ndiwo (anthu abwino) a ku dzanja lamanja.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا هُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Koma amene sanakhulupirire Ayah Zathu, ndi anthu a kudzanja lamanzere (oipa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
عَلَيۡهِمۡ نَارٞ مُّؤۡصَدَةُۢ
Moto wozungulira mbali zonse udzakhala pa iwo (ndikuwatsekera makomo).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی البلد
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن