Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: AL-BALAD   Verset:

AL-BALAD

لَآ أُقۡسِمُ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndikulumbilira mzinda uwu (wa Makka).
Les exégèses en arabe:
وَأَنتَ حِلُّۢ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndipo iwe udzatsikira mu mzindawu mwa ufulu (ndi kuuonjezera ulemelero).
Les exégèses en arabe:
وَوَالِدٖ وَمَا وَلَدَ
Ndiponso ndikulumbilira chobereka ndi choberekedwa, (kudzera mwa iwo mtundu wa anthu udasungidwa).
Les exégèses en arabe:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِي كَبَدٍ
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
[439] Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake, chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe kupilira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda chida. Ndipo pamwamba pa izi, Allah wamukakamiza zinthu zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye achita chikulembedwa. Pa tsiku lachimaliziro adzawerengedwa chilichonse chimene adachichita; chachikulu kapena chaching’ono.
Les exégèses en arabe:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّن يَقۡدِرَ عَلَيۡهِ أَحَدٞ
Kodi (munthu wolengedwa ndi mavutoyu) akuganiza kuti palibe amene angamuthe? [440]
[440] Tanthauzo lake apa nkuti munthu akuganiza kuti palibe aliyense amene angamuweruze pa zolakwa zake.
Les exégèses en arabe:
يَقُولُ أَهۡلَكۡتُ مَالٗا لُّبَدًا
Akunena (monyadira kuti): “Ndaononga chuma chambiri (chifukwa choletsa Chisilamu kufala).”[441]
[441] (Ndime 6-7) Mawu awa akunenedwa kwa okanira omwe adali kupereka chuma chawo pomenyana ndi Usilamu kapena kufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Kenako adali kudzitama chifukwa chopereka chuma chambiri pa njirayo. Izi zikumukhudza aliyense amene akufuna kuti Chisilamu chionongeke. Ndipo iwo amaganiza kuti Allah sakudziwa za maganizo awo oipa.
Les exégèses en arabe:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّمۡ يَرَهُۥٓ أَحَدٌ
Kodi akuganiza kuti palibe akumuona?
Les exégèses en arabe:
أَلَمۡ نَجۡعَل لَّهُۥ عَيۡنَيۡنِ
Kodi sitidampangire maso awiri (amene akuyang’anira)?
Les exégèses en arabe:
وَلِسَانٗا وَشَفَتَيۡنِ
Ndilirime ndi milomo iwiri (zimene akulankhulira)?
Les exégèses en arabe:
وَهَدَيۡنَٰهُ ٱلنَّجۡدَيۡنِ
Ndipo tamlongosolera njira ziwiri: (yabwino ndi yoipa, ndipo tampatsa mphamvu yosankhira njira imene akufuna).
Les exégèses en arabe:
فَلَا ٱقۡتَحَمَ ٱلۡعَقَبَةَ
Kodi walikwera phiri lovutalo (lomwe lingakamfikitse ku Jannah)?[442]
[442] Tanthauzo lake ndikuti bwanji munthu sathokoza chifundo chimenechi (chopatsidwa maso ndi pakamwa) pogwiritsa ntchito chuma chake pa zinthu zabwino zimene Allah wazitchula m’ma Ayah akubwerawa? Ndipo tanthauzo la “kukwera phiri lovuta’’ ndiko kupereka chuma panjira ya Allah chimene chili ndinthu chovuta kwa anthu ambiri ndipo chimafanana ndikukwera phiri losongoka.
Les exégèses en arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡعَقَبَةُ
Nanga nchiyani chakudziwitsa za kukwera phiri lovutalo?
Les exégèses en arabe:
فَكُّ رَقَبَةٍ
(Kutero ndiko) kupereka ufulu kwa kapolo,
Les exégèses en arabe:
أَوۡ إِطۡعَٰمٞ فِي يَوۡمٖ ذِي مَسۡغَبَةٖ
Kapena kuwadyetsa (osowa) pa tsiku la njala,
Les exégèses en arabe:
يَتِيمٗا ذَا مَقۡرَبَةٍ
Amasiye achibale,
Les exégèses en arabe:
أَوۡ مِسۡكِينٗا ذَا مَتۡرَبَةٖ
Kapena wosauka wa fumbi lokhalokha (chifukwa cha kuvutika kwambiri),
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ كَانَ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡمَرۡحَمَةِ
Komanso nakhala mmodzi mwa okhulupirira ndikumalangizana za kupirira, ndi kumalangizananso za chifundo.
Les exégèses en arabe:
أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Otero ndiwo (anthu abwino) a ku dzanja lamanja.
Les exégèses en arabe:
وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا هُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Koma amene sanakhulupirire Ayah Zathu, ndi anthu a kudzanja lamanzere (oipa).
Les exégèses en arabe:
عَلَيۡهِمۡ نَارٞ مُّؤۡصَدَةُۢ
Moto wozungulira mbali zonse udzakhala pa iwo (ndikuwatsekera makomo).
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: AL-BALAD
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture