വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ പരിഭാഷ * - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക


പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: സൂറത്തുൽ ബലദ്   ആയത്ത്:

സൂറത്തുൽ ബലദ്

لَآ أُقۡسِمُ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndikulumbilira mzinda uwu (wa Makka).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَأَنتَ حِلُّۢ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndipo iwe udzatsikira mu mzindawu mwa ufulu (ndi kuuonjezera ulemelero).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَوَالِدٖ وَمَا وَلَدَ
Ndiponso ndikulumbilira chobereka ndi choberekedwa, (kudzera mwa iwo mtundu wa anthu udasungidwa).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِي كَبَدٍ
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
[439] Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake, chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe kupilira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda chida. Ndipo pamwamba pa izi, Allah wamukakamiza zinthu zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye achita chikulembedwa. Pa tsiku lachimaliziro adzawerengedwa chilichonse chimene adachichita; chachikulu kapena chaching’ono.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّن يَقۡدِرَ عَلَيۡهِ أَحَدٞ
Kodi (munthu wolengedwa ndi mavutoyu) akuganiza kuti palibe amene angamuthe? [440]
[440] Tanthauzo lake apa nkuti munthu akuganiza kuti palibe aliyense amene angamuweruze pa zolakwa zake.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
يَقُولُ أَهۡلَكۡتُ مَالٗا لُّبَدًا
Akunena (monyadira kuti): “Ndaononga chuma chambiri (chifukwa choletsa Chisilamu kufala).”[441]
[441] (Ndime 6-7) Mawu awa akunenedwa kwa okanira omwe adali kupereka chuma chawo pomenyana ndi Usilamu kapena kufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Kenako adali kudzitama chifukwa chopereka chuma chambiri pa njirayo. Izi zikumukhudza aliyense amene akufuna kuti Chisilamu chionongeke. Ndipo iwo amaganiza kuti Allah sakudziwa za maganizo awo oipa.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّمۡ يَرَهُۥٓ أَحَدٌ
Kodi akuganiza kuti palibe akumuona?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَلَمۡ نَجۡعَل لَّهُۥ عَيۡنَيۡنِ
Kodi sitidampangire maso awiri (amene akuyang’anira)?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَلِسَانٗا وَشَفَتَيۡنِ
Ndilirime ndi milomo iwiri (zimene akulankhulira)?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَهَدَيۡنَٰهُ ٱلنَّجۡدَيۡنِ
Ndipo tamlongosolera njira ziwiri: (yabwino ndi yoipa, ndipo tampatsa mphamvu yosankhira njira imene akufuna).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
فَلَا ٱقۡتَحَمَ ٱلۡعَقَبَةَ
Kodi walikwera phiri lovutalo (lomwe lingakamfikitse ku Jannah)?[442]
[442] Tanthauzo lake ndikuti bwanji munthu sathokoza chifundo chimenechi (chopatsidwa maso ndi pakamwa) pogwiritsa ntchito chuma chake pa zinthu zabwino zimene Allah wazitchula m’ma Ayah akubwerawa? Ndipo tanthauzo la “kukwera phiri lovuta’’ ndiko kupereka chuma panjira ya Allah chimene chili ndinthu chovuta kwa anthu ambiri ndipo chimafanana ndikukwera phiri losongoka.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡعَقَبَةُ
Nanga nchiyani chakudziwitsa za kukwera phiri lovutalo?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
فَكُّ رَقَبَةٍ
(Kutero ndiko) kupereka ufulu kwa kapolo,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَوۡ إِطۡعَٰمٞ فِي يَوۡمٖ ذِي مَسۡغَبَةٖ
Kapena kuwadyetsa (osowa) pa tsiku la njala,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
يَتِيمٗا ذَا مَقۡرَبَةٍ
Amasiye achibale,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَوۡ مِسۡكِينٗا ذَا مَتۡرَبَةٖ
Kapena wosauka wa fumbi lokhalokha (chifukwa cha kuvutika kwambiri),
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
ثُمَّ كَانَ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡمَرۡحَمَةِ
Komanso nakhala mmodzi mwa okhulupirira ndikumalangizana za kupirira, ndi kumalangizananso za chifundo.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Otero ndiwo (anthu abwino) a ku dzanja lamanja.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا هُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Koma amene sanakhulupirire Ayah Zathu, ndi anthu a kudzanja lamanzere (oipa).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
عَلَيۡهِمۡ نَارٞ مُّؤۡصَدَةُۢ
Moto wozungulira mbali zonse udzakhala pa iwo (ndikuwatsekera makomo).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
 
പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: സൂറത്തുൽ ബലദ്
സൂറത്തുകളുടെ സൂചിക പേജ് നമ്പർ
 
വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ പരിഭാഷ - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക

പരിശുദ്ധ ഖുർആൻ ആശയ വിവർത്തനം ചെവ്വ ഭാഷയിൽ, പരിഭാഷ: ഖാലിദ് ഇബ്റാഹീം പെറ്റാല, 2020 പതിപ്പ്

അടക്കുക