Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat A-Naas (De Mensheid)   Vers:

Soerat A-Naas (De Mensheid)

قُلۡ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلنَّاسِ
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye (Mleri) wa anthu (Yemwe akulinganiza zinthu zawo).[503]
[503] Allah pokhala Mlengi wa anthu ndi amenenso amawalera kuyambira pamene ali m’mimba mpaka kumapeto a moyo wawo pano pa dziko. Kuwaleraku kuli muuzimu, mthupi, mu mpweya, ndi pa chilichonse chofunika pa moyo wawo. Kuonjezera pa zimenezi adawapatsa nzeru ndi kuwasonyeza njira zabwino za dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuzitsata njirazo. Adawasonyezanso njira zoipa za dziko lino lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuti azipewe njira zoipazo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
مَلِكِ ٱلنَّاسِ
Mfumu ya anthu ( Imene iri ndi mphamvu yochita chirichonse pa iwo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِلَٰهِ ٱلنَّاسِ
Wopembedzedwa wa anthu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
مِن شَرِّ ٱلۡوَسۡوَاسِ ٱلۡخَنَّاسِ
Kuzoipa za mnong’onezi (yemwe amathira unong’onezi wake m’mitimaya anthu) yemwenso amabisala (posiya unong’onezi wake ngati mwini mtimawo atankumbukira Allah).[504]
[504] Mnong’onezi wa zoipa amene amabisala ndiye Satana, yemwe ntchito yake ndi kunong’oneza zoipa m’mitima ya anthu pofuna kuwasokeretsa ndi kuwaiwalitsa Allah. Koma akakumana ndi munthu wa chikhulupiliro cha mphamvu kapena yemwe amatamanda kwambiri Mbuye wake Allah, Satanayo amalephera ndipo amathawa; kubwerera m’mbuyo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
ٱلَّذِي يُوَسۡوِسُ فِي صُدُورِ ٱلنَّاسِ
Yemwe amanong’oneza mzifuwa za anthu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
مِنَ ٱلۡجِنَّةِ وَٱلنَّاسِ
Wochokera m’ziwanda ndi mwa anthu.”[505]
[505] Mchiyankhulo cha Chiarabu aliyense woipitsitsa amatchedwa “shaitan” satana, munthu kapena chiwanda. Satana wa muwanthu ndiwoipitsitsa kwambiri kwa anthu kuposa wa m’ziwanda.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat A-Naas (De Mensheid)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit