Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Burūj   Ayah:

Al-Burūj

وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلۡبُرُوجِ
Ndikulumbilira thambo lomwe liri ndi Buruj (Nyenyezi zikuluzikulu).[411]
[411] Buruj ndi nyenyezi zomwe zimakhala m’magulumagulu ndipo gulu lililonse limatchedwa Buruj. Ndipo Buruj zonse zilipo khumi ndi ziwiri (12). Zisanu ndi imodzi zili kumpoto kwa “Equator”, pomwe zisanu ndi imodzi zili kumwera kwake.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡمَوۡعُودِ
Ndi tsiku lolonjezedwa (kuwerengedwa ndi kulipidwa),
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَشَاهِدٖ وَمَشۡهُودٖ
Ndi woikira umboni, ndi woikiridwa umboni.[412]
[412] “Woikira umboni ndi woikiridwa umboni” angathe kukhala aliyense woikira umboni ndi woikiridwa umboni pa tsiku lachimaliziro, monga aneneri adzaikira umboni anthu pa zabwino kapena zoipa; pa malo pochitira mapemphero padzamuikira umboni wazabwino yemwe adali kupempherapo. Ndipo pamalo pomwe padali kuchitikira zoipa padzawachitira umboni anthu oipa za machimo awo: ngakhale ziwalo ndi khungu nazonso pa tsiku limenelo zidzaikira umboni kwa mwini ziwalozo. Basi munthu akatsimikiza kuchita machimo akumbukire kuti ali nazo mboni zambiri zomwe zikumuona ndipo pa tsiku la chiweruziro zidzaima pa maso pa Allah kupereka umboni wokhudza munthuyo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُتِلَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡأُخۡدُودِ
Atembeleredwa eni ngalande zamoto (zomwe adali kuwazunzira okhulupirira Allah, achimuna ndi achikazi).[413]
[413] Pamene Ayuda a ku Najrani adalowa m’Chikhristu, (Chisilamu chisadafike ndiponso Chikhristu chisadaonongeke), idamufika nkhaniyi mfumu yawo dzina lake Dhu-Nuwas; adabwera ku Najrani ndi gulu lankhondo lalikulu; adawakakamizira anthu ku Chiyuda koma iwo adakana. Nayamba kuwapha anthu okhulupilirawo powaponya m’ngalande za moto.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلنَّارِ ذَاتِ ٱلۡوَقُودِ
(Ngalande) za moto wankhuni (zambiri zomwe adali kuzikoleza ndikuotchera okhulupirira),
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِذۡ هُمۡ عَلَيۡهَا قُعُودٞ
Pamene iwo adali chikhalire m’mphepete mwa ngalandezo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَهُمۡ عَلَىٰ مَا يَفۡعَلُونَ بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ شُهُودٞ
Uku iwo akuyang’ana zomwe amawachitira okhulupirira, (pootchedwa ndi moto).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا نَقَمُواْ مِنۡهُمۡ إِلَّآ أَن يُؤۡمِنُواْ بِٱللَّهِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَمِيدِ
Sadaone choipa chilichonse mwa iwo koma chifukwa choti adakhulupirira Allah mwini mphamvu zonse ndiponso mwini kuyamikidwa,
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلَّذِي لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدٌ
Yemwe ufumu wakumwamba ndi pansi ndiWake; ndipo Allah ndi mboni pachilichonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ فَتَنُواْ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ ثُمَّ لَمۡ يَتُوبُواْ فَلَهُمۡ عَذَابُ جَهَنَّمَ وَلَهُمۡ عَذَابُ ٱلۡحَرِيقِ
Ndithu amene ayesa mayeso okhulupirira achimuna ndi achikazi (pa chipembedzo chawo ndi mazunzo ndi chilango cha moto), pambuyo pake osalapa (pa zimenezi), adzalandira chilango cha Jahena ndiponso chilango cha moto wopsereza,[414]
[414] Tanthauzo la “kuwazunza” apa ndiko kuwavutitsa ndi kuwathetsa mphamvu kuti asiye chikhulupiliro chawo; asakhulupirire mwa Allah. Mawuwa ngakhale akukhudzana ndi eni ngalande za moto, akukhudzanso akafiri a m’Makka omwe adali kuzunza Asilamu ndi mazunzo osiyanasiyana kuti abwelere kuchipembedzo cha mafano. Ndipo zimenezi zikhudzanso aliyense.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمۡ جَنَّٰتٞ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡكَبِيرُ
Ndithudi amene akhulupirira ndi kuchita ntchito zabwino, adzakhala ndi Minda yamtendere (momwe) mitsinje ikuyenda pansi pake; kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ بَطۡشَ رَبِّكَ لَشَدِيدٌ
Ndithu kulanga kwa Mbuye wako (kwa anthu achinyengo), ndi kwaukali kwambiri.[415]
[415] (Ndime 12-16) Allah pambuyo powatonthoza Asilamu pakuwauza zomwe zidawaonekera abale awo amene adatsogola, tsopanonso akuwatonthoza ndi ufumu Wake wolemekezeka kuti adziwe kuti awo akafiri omwe akudziona kuti ali ndi mphamvu zolangira anzawo, Iye sangamuthe. Akafuna adzawalanga ndi chilango cha dziko lapansi ndi cha tsiku lachimaliziro, kapena chimodzi mwa zilangozi; pakuti Iye Ngokhululuka kwambiri ndiponso Ngwachikondi zedi, awatembenula mitima yawo kuti achikhulupirire chimene adachikana. Chifukwa cha mphamvu Zake zoposa, Allah, adachita zonsezi ziwiri. Patapita zaka zochepa adawapatsa mphamvu omwe adali opanda mphamvu, kenaka adayamba kuwalanga osakhulupilira aja chilango cha padziko, monga Abu Jahl ndi anzake omwe adali kumutsutsa kwambiri Mtumiki (s.a.w) pamodzi ndi omutsatira ake. Ndipo ena adawatembenula mitima yawo nkulowa mchipembedzo cha Chisilamu; adaima ndikuchiteteza Chisilamu popereka nsembe ya mizimu yawo ndi chuma chawo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّهُۥ هُوَ يُبۡدِئُ وَيُعِيدُ
Iye, (Mmodzi yekha) ndi amene adayambitsa zolengedwa ndiponso ndi Yemwe adzazibweze (pambuyo poonongeka);
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَهُوَ ٱلۡغَفُورُ ٱلۡوَدُودُ
Iye, ndi Wokhululuka (kwa amene walapa kwa Iye), ndiponso Wokonda kwambiri (amene akumkonda ndi kumumvera),
Ang mga Tafsir na Arabe:
ذُو ٱلۡعَرۡشِ ٱلۡمَجِيدُ
Mwini Arsh (Mpando wachifumu), (ndiponso) Wolemekezeka (mmene alili ndi mbiri Zake),
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَعَّالٞ لِّمَا يُرِيدُ
Wochita zimene wafuna, (ndipo chimene wafuna sichikanika).
Ang mga Tafsir na Arabe:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡجُنُودِ
Kodi yakufika nkhani ya magulu a nkhondo,
Ang mga Tafsir na Arabe:
فِرۡعَوۡنَ وَثَمُودَ
Firiaun (Farawo) ndi Samudu, (ndi chilango chimene chidawapeza chifukwa chakulimbikira kwawo pa zinthu zopanda pake)?
Ang mga Tafsir na Arabe:
بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فِي تَكۡذِيبٖ
Koma amene sadakhulupirire ali mkati motsutsa basi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱللَّهُ مِن وَرَآئِهِم مُّحِيطُۢ
Koma Allah awazinga mbali zonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
بَلۡ هُوَ قُرۡءَانٞ مَّجِيدٞ
Koma iyi ndi Qur’an yolemekezeka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فِي لَوۡحٖ مَّحۡفُوظِۭ
Yomwe idachokera mu ubawo (chisileti chachikulu) wotetezedwa (ndi manja alionse, osintha kanthu kapena kuonjezerapo).
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Burūj
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara