《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 章: 布柔智   段:

布柔智

وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلۡبُرُوجِ
Ndikulumbilira thambo lomwe liri ndi Buruj (Nyenyezi zikuluzikulu).[411]
[411] Buruj ndi nyenyezi zomwe zimakhala m’magulumagulu ndipo gulu lililonse limatchedwa Buruj. Ndipo Buruj zonse zilipo khumi ndi ziwiri (12). Zisanu ndi imodzi zili kumpoto kwa “Equator”, pomwe zisanu ndi imodzi zili kumwera kwake.
阿拉伯语经注:
وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡمَوۡعُودِ
Ndi tsiku lolonjezedwa (kuwerengedwa ndi kulipidwa),
阿拉伯语经注:
وَشَاهِدٖ وَمَشۡهُودٖ
Ndi woikira umboni, ndi woikiridwa umboni.[412]
[412] “Woikira umboni ndi woikiridwa umboni” angathe kukhala aliyense woikira umboni ndi woikiridwa umboni pa tsiku lachimaliziro, monga aneneri adzaikira umboni anthu pa zabwino kapena zoipa; pa malo pochitira mapemphero padzamuikira umboni wazabwino yemwe adali kupempherapo. Ndipo pamalo pomwe padali kuchitikira zoipa padzawachitira umboni anthu oipa za machimo awo: ngakhale ziwalo ndi khungu nazonso pa tsiku limenelo zidzaikira umboni kwa mwini ziwalozo. Basi munthu akatsimikiza kuchita machimo akumbukire kuti ali nazo mboni zambiri zomwe zikumuona ndipo pa tsiku la chiweruziro zidzaima pa maso pa Allah kupereka umboni wokhudza munthuyo.
阿拉伯语经注:
قُتِلَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡأُخۡدُودِ
Atembeleredwa eni ngalande zamoto (zomwe adali kuwazunzira okhulupirira Allah, achimuna ndi achikazi).[413]
[413] Pamene Ayuda a ku Najrani adalowa m’Chikhristu, (Chisilamu chisadafike ndiponso Chikhristu chisadaonongeke), idamufika nkhaniyi mfumu yawo dzina lake Dhu-Nuwas; adabwera ku Najrani ndi gulu lankhondo lalikulu; adawakakamizira anthu ku Chiyuda koma iwo adakana. Nayamba kuwapha anthu okhulupilirawo powaponya m’ngalande za moto.
阿拉伯语经注:
ٱلنَّارِ ذَاتِ ٱلۡوَقُودِ
(Ngalande) za moto wankhuni (zambiri zomwe adali kuzikoleza ndikuotchera okhulupirira),
阿拉伯语经注:
إِذۡ هُمۡ عَلَيۡهَا قُعُودٞ
Pamene iwo adali chikhalire m’mphepete mwa ngalandezo.
阿拉伯语经注:
وَهُمۡ عَلَىٰ مَا يَفۡعَلُونَ بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ شُهُودٞ
Uku iwo akuyang’ana zomwe amawachitira okhulupirira, (pootchedwa ndi moto).
阿拉伯语经注:
وَمَا نَقَمُواْ مِنۡهُمۡ إِلَّآ أَن يُؤۡمِنُواْ بِٱللَّهِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَمِيدِ
Sadaone choipa chilichonse mwa iwo koma chifukwa choti adakhulupirira Allah mwini mphamvu zonse ndiponso mwini kuyamikidwa,
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِي لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدٌ
Yemwe ufumu wakumwamba ndi pansi ndiWake; ndipo Allah ndi mboni pachilichonse.
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱلَّذِينَ فَتَنُواْ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ ثُمَّ لَمۡ يَتُوبُواْ فَلَهُمۡ عَذَابُ جَهَنَّمَ وَلَهُمۡ عَذَابُ ٱلۡحَرِيقِ
Ndithu amene ayesa mayeso okhulupirira achimuna ndi achikazi (pa chipembedzo chawo ndi mazunzo ndi chilango cha moto), pambuyo pake osalapa (pa zimenezi), adzalandira chilango cha Jahena ndiponso chilango cha moto wopsereza,[414]
[414] Tanthauzo la “kuwazunza” apa ndiko kuwavutitsa ndi kuwathetsa mphamvu kuti asiye chikhulupiliro chawo; asakhulupirire mwa Allah. Mawuwa ngakhale akukhudzana ndi eni ngalande za moto, akukhudzanso akafiri a m’Makka omwe adali kuzunza Asilamu ndi mazunzo osiyanasiyana kuti abwelere kuchipembedzo cha mafano. Ndipo zimenezi zikhudzanso aliyense.
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمۡ جَنَّٰتٞ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡكَبِيرُ
Ndithudi amene akhulupirira ndi kuchita ntchito zabwino, adzakhala ndi Minda yamtendere (momwe) mitsinje ikuyenda pansi pake; kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
阿拉伯语经注:
إِنَّ بَطۡشَ رَبِّكَ لَشَدِيدٌ
Ndithu kulanga kwa Mbuye wako (kwa anthu achinyengo), ndi kwaukali kwambiri.[415]
[415] (Ndime 12-16) Allah pambuyo powatonthoza Asilamu pakuwauza zomwe zidawaonekera abale awo amene adatsogola, tsopanonso akuwatonthoza ndi ufumu Wake wolemekezeka kuti adziwe kuti awo akafiri omwe akudziona kuti ali ndi mphamvu zolangira anzawo, Iye sangamuthe. Akafuna adzawalanga ndi chilango cha dziko lapansi ndi cha tsiku lachimaliziro, kapena chimodzi mwa zilangozi; pakuti Iye Ngokhululuka kwambiri ndiponso Ngwachikondi zedi, awatembenula mitima yawo kuti achikhulupirire chimene adachikana. Chifukwa cha mphamvu Zake zoposa, Allah, adachita zonsezi ziwiri. Patapita zaka zochepa adawapatsa mphamvu omwe adali opanda mphamvu, kenaka adayamba kuwalanga osakhulupilira aja chilango cha padziko, monga Abu Jahl ndi anzake omwe adali kumutsutsa kwambiri Mtumiki (s.a.w) pamodzi ndi omutsatira ake. Ndipo ena adawatembenula mitima yawo nkulowa mchipembedzo cha Chisilamu; adaima ndikuchiteteza Chisilamu popereka nsembe ya mizimu yawo ndi chuma chawo.
阿拉伯语经注:
إِنَّهُۥ هُوَ يُبۡدِئُ وَيُعِيدُ
Iye, (Mmodzi yekha) ndi amene adayambitsa zolengedwa ndiponso ndi Yemwe adzazibweze (pambuyo poonongeka);
阿拉伯语经注:
وَهُوَ ٱلۡغَفُورُ ٱلۡوَدُودُ
Iye, ndi Wokhululuka (kwa amene walapa kwa Iye), ndiponso Wokonda kwambiri (amene akumkonda ndi kumumvera),
阿拉伯语经注:
ذُو ٱلۡعَرۡشِ ٱلۡمَجِيدُ
Mwini Arsh (Mpando wachifumu), (ndiponso) Wolemekezeka (mmene alili ndi mbiri Zake),
阿拉伯语经注:
فَعَّالٞ لِّمَا يُرِيدُ
Wochita zimene wafuna, (ndipo chimene wafuna sichikanika).
阿拉伯语经注:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡجُنُودِ
Kodi yakufika nkhani ya magulu a nkhondo,
阿拉伯语经注:
فِرۡعَوۡنَ وَثَمُودَ
Firiaun (Farawo) ndi Samudu, (ndi chilango chimene chidawapeza chifukwa chakulimbikira kwawo pa zinthu zopanda pake)?
阿拉伯语经注:
بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فِي تَكۡذِيبٖ
Koma amene sadakhulupirire ali mkati motsutsa basi.
阿拉伯语经注:
وَٱللَّهُ مِن وَرَآئِهِم مُّحِيطُۢ
Koma Allah awazinga mbali zonse.
阿拉伯语经注:
بَلۡ هُوَ قُرۡءَانٞ مَّجِيدٞ
Koma iyi ndi Qur’an yolemekezeka.
阿拉伯语经注:
فِي لَوۡحٖ مَّحۡفُوظِۭ
Yomwe idachokera mu ubawo (chisileti chachikulu) wotetezedwa (ndi manja alionse, osintha kanthu kapena kuonjezerapo).
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 布柔智
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭