《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 章: 塔勒格   段:

塔勒格

وَٱلسَّمَآءِ وَٱلطَّارِقِ
Ndikulumbilira ku mwamba ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلطَّارِقُ
Chitakudziwitse nchiyani za Nyenyezi yodza usikuyo?
阿拉伯语经注:
ٱلنَّجۡمُ ٱلثَّاقِبُ
Imeneyo ndi nyenyezi yowala kwambiri (mu mdima).
阿拉伯语经注:
إِن كُلُّ نَفۡسٖ لَّمَّا عَلَيۡهَا حَافِظٞ
Ndithudi palibe mzimu uliwonse koma uli ndi msungi wake (amene akuuyang’anira ndikulemba zonse zochita zake).
阿拉伯语经注:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ مِمَّ خُلِقَ
Aganizire munthu, kodi adalengedwa kuchokera kuchiyani?
阿拉伯语经注:
خُلِقَ مِن مَّآءٖ دَافِقٖ
Adalengedwa kuchokera ku madzi ofwamphuka.
阿拉伯语经注:
يَخۡرُجُ مِنۢ بَيۡنِ ٱلصُّلۡبِ وَٱلتَّرَآئِبِ
Amatuluka kuchokera pakati pa mafupa a msana (wa mwamuna) ndi chifuwa (cha mkazi).
阿拉伯语经注:
إِنَّهُۥ عَلَىٰ رَجۡعِهِۦ لَقَادِرٞ
Ndithu Iye ndiwakutha, kumbwezeranso (ku moyo pa mbuyo pa imfa).
阿拉伯语经注:
يَوۡمَ تُبۡلَى ٱلسَّرَآئِرُ
Tsiku limene zobisika zonse zidzaonekera poyera.
阿拉伯语经注:
فَمَا لَهُۥ مِن قُوَّةٖ وَلَا نَاصِرٖ
Munthu sadzakhala ndi mphamvu (tsiku limenelo zodzitetezera iye mwini) ndiponso sadzakhala ndi mtetezi.
阿拉伯语经注:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلرَّجۡعِ
Ndikulumbiliranso mitambo yobweretsabweretsa mvula.
阿拉伯语经注:
وَٱلۡأَرۡضِ ذَاتِ ٱلصَّدۡعِ
Ndi nthaka imene imang’ambika (potulutsa m’mera),
阿拉伯语经注:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلٞ فَصۡلٞ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndi mawu olekanitsa (Haqq ndi Bâtwil - choona ndi chonama).
阿拉伯语经注:
وَمَا هُوَ بِٱلۡهَزۡلِ
Imeneyi sinkhambakamwa.
阿拉伯语经注:
إِنَّهُمۡ يَكِيدُونَ كَيۡدٗا
Ndithudi iwo akukonza chiwembu.[416]
[416] (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupilira) akuchita ndale kuti azimitse dangalira la Qur’an ndikuyesetsa kuti awabweze amene adakhulupilira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Naye Allah akuwachitira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amazikonza.
阿拉伯语经注:
وَأَكِيدُ كَيۡدٗا
Nanenso ndikuwakonzera chiwembu (champhamvu kwambiri chimene sangathe kuchipewa).
阿拉伯语经注:
فَمَهِّلِ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَمۡهِلۡهُمۡ رُوَيۡدَۢا
Basi, apatse nthawi osakhulupirira apatse nthawi pang’ono, (aona posachedwa).
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 塔勒格
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭