Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Et Tarik   Ajeti:

Suretu Et Tarik

وَٱلسَّمَآءِ وَٱلطَّارِقِ
Ndikulumbilira ku mwamba ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلطَّارِقُ
Chitakudziwitse nchiyani za Nyenyezi yodza usikuyo?
Tefsiret në gjuhën arabe:
ٱلنَّجۡمُ ٱلثَّاقِبُ
Imeneyo ndi nyenyezi yowala kwambiri (mu mdima).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِن كُلُّ نَفۡسٖ لَّمَّا عَلَيۡهَا حَافِظٞ
Ndithudi palibe mzimu uliwonse koma uli ndi msungi wake (amene akuuyang’anira ndikulemba zonse zochita zake).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ مِمَّ خُلِقَ
Aganizire munthu, kodi adalengedwa kuchokera kuchiyani?
Tefsiret në gjuhën arabe:
خُلِقَ مِن مَّآءٖ دَافِقٖ
Adalengedwa kuchokera ku madzi ofwamphuka.
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَخۡرُجُ مِنۢ بَيۡنِ ٱلصُّلۡبِ وَٱلتَّرَآئِبِ
Amatuluka kuchokera pakati pa mafupa a msana (wa mwamuna) ndi chifuwa (cha mkazi).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّهُۥ عَلَىٰ رَجۡعِهِۦ لَقَادِرٞ
Ndithu Iye ndiwakutha, kumbwezeranso (ku moyo pa mbuyo pa imfa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَوۡمَ تُبۡلَى ٱلسَّرَآئِرُ
Tsiku limene zobisika zonse zidzaonekera poyera.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَا لَهُۥ مِن قُوَّةٖ وَلَا نَاصِرٖ
Munthu sadzakhala ndi mphamvu (tsiku limenelo zodzitetezera iye mwini) ndiponso sadzakhala ndi mtetezi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلرَّجۡعِ
Ndikulumbiliranso mitambo yobweretsabweretsa mvula.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلۡأَرۡضِ ذَاتِ ٱلصَّدۡعِ
Ndi nthaka imene imang’ambika (potulutsa m’mera),
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلٞ فَصۡلٞ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndi mawu olekanitsa (Haqq ndi Bâtwil - choona ndi chonama).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا هُوَ بِٱلۡهَزۡلِ
Imeneyi sinkhambakamwa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّهُمۡ يَكِيدُونَ كَيۡدٗا
Ndithudi iwo akukonza chiwembu.[416]
[416] (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupilira) akuchita ndale kuti azimitse dangalira la Qur’an ndikuyesetsa kuti awabweze amene adakhulupilira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Naye Allah akuwachitira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amazikonza.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأَكِيدُ كَيۡدٗا
Nanenso ndikuwakonzera chiwembu (champhamvu kwambiri chimene sangathe kuchipewa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَهِّلِ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَمۡهِلۡهُمۡ رُوَيۡدَۢا
Basi, apatse nthawi osakhulupirira apatse nthawi pang’ono, (aona posachedwa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Et Tarik
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll