แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: At-Tāriq   อายะฮ์:

At-Tāriq

وَٱلسَّمَآءِ وَٱلطَّارِقِ
Ndikulumbilira ku mwamba ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلطَّارِقُ
Chitakudziwitse nchiyani za Nyenyezi yodza usikuyo?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ٱلنَّجۡمُ ٱلثَّاقِبُ
Imeneyo ndi nyenyezi yowala kwambiri (mu mdima).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِن كُلُّ نَفۡسٖ لَّمَّا عَلَيۡهَا حَافِظٞ
Ndithudi palibe mzimu uliwonse koma uli ndi msungi wake (amene akuuyang’anira ndikulemba zonse zochita zake).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ مِمَّ خُلِقَ
Aganizire munthu, kodi adalengedwa kuchokera kuchiyani?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
خُلِقَ مِن مَّآءٖ دَافِقٖ
Adalengedwa kuchokera ku madzi ofwamphuka.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
يَخۡرُجُ مِنۢ بَيۡنِ ٱلصُّلۡبِ وَٱلتَّرَآئِبِ
Amatuluka kuchokera pakati pa mafupa a msana (wa mwamuna) ndi chifuwa (cha mkazi).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّهُۥ عَلَىٰ رَجۡعِهِۦ لَقَادِرٞ
Ndithu Iye ndiwakutha, kumbwezeranso (ku moyo pa mbuyo pa imfa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
يَوۡمَ تُبۡلَى ٱلسَّرَآئِرُ
Tsiku limene zobisika zonse zidzaonekera poyera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَا لَهُۥ مِن قُوَّةٖ وَلَا نَاصِرٖ
Munthu sadzakhala ndi mphamvu (tsiku limenelo zodzitetezera iye mwini) ndiponso sadzakhala ndi mtetezi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلرَّجۡعِ
Ndikulumbiliranso mitambo yobweretsabweretsa mvula.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلۡأَرۡضِ ذَاتِ ٱلصَّدۡعِ
Ndi nthaka imene imang’ambika (potulutsa m’mera),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلٞ فَصۡلٞ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndi mawu olekanitsa (Haqq ndi Bâtwil - choona ndi chonama).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا هُوَ بِٱلۡهَزۡلِ
Imeneyi sinkhambakamwa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّهُمۡ يَكِيدُونَ كَيۡدٗا
Ndithudi iwo akukonza chiwembu.[416]
[416] (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupilira) akuchita ndale kuti azimitse dangalira la Qur’an ndikuyesetsa kuti awabweze amene adakhulupilira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Naye Allah akuwachitira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amazikonza.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَكِيدُ كَيۡدٗا
Nanenso ndikuwakonzera chiwembu (champhamvu kwambiri chimene sangathe kuchipewa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَهِّلِ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَمۡهِلۡهُمۡ رُوَيۡدَۢا
Basi, apatse nthawi osakhulupirira apatse nthawi pang’ono, (aona posachedwa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: At-Tāriq
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด