Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Сура: Мурсалот сураси   Оят:

Мурсалот сураси

وَٱلۡمُرۡسَلَٰتِ عُرۡفٗا
Ndikulumbilira mphepo yomwe ikuomba motsatizana.
Арабча тафсирлар:
فَٱلۡعَٰصِفَٰتِ عَصۡفٗا
Ndi mphepo yamkuntho ikamakuntha.
Арабча тафсирлар:
وَٱلنَّٰشِرَٰتِ نَشۡرٗا
Ndi mphepo yobalalitsa mitambo ndi mvula.
Арабча тафсирлар:
فَٱلۡفَٰرِقَٰتِ فَرۡقٗا
Ndi ma Ayah osiyanitsa pakati pachoona ndi chonama;
Арабча тафсирлар:
فَٱلۡمُلۡقِيَٰتِ ذِكۡرًا
Ndi angelo opereka chivumbulutso kwa aneneri.
Арабча тафсирлар:
عُذۡرًا أَوۡ نُذۡرًا
Kuti chichotse madandaulo kapena chikhale chenjezo;
Арабча тафсирлар:
إِنَّمَا تُوعَدُونَ لَوَٰقِعٞ
Ndithu zimene mukulonjezedwa (kuti chimaliziro chidzakhalapo) zidzachitikadi (popanda chipeneko),
Арабча тафсирлар:
فَإِذَا ٱلنُّجُومُ طُمِسَتۡ
Pamene nyenyezi zidzafafanizidwa (kuwala kwake ndi kuchotsedwa m’malo mwake).
Арабча тафсирлар:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ فُرِجَتۡ
Ndiponso pamene thambo lidzang‘ambidwa.
Арабча тафсирлар:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ نُسِفَتۡ
Ndi pamenenso mapiri adzachotsedwa m’malo mwake ndi kuperedwa (kukhala fumbi).
Арабча тафсирлар:
وَإِذَا ٱلرُّسُلُ أُقِّتَتۡ
Ndi pamene atumiki adzasonkhanitsidwa pa nthawi yake, (kuti apereke umboni ku mibadwo yawo).
Арабча тафсирлар:
لِأَيِّ يَوۡمٍ أُجِّلَتۡ
Kodi nditsiku lanji azichedwetsera (zinthu zikuluzikulu kuti zidzachitike)?
Арабча тафсирлар:
لِيَوۡمِ ٱلۡفَصۡلِ
Nditsiku loweruza (pakati pa zolengedwa).
Арабча тафсирлар:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِ
Nchiyani chingakudziwitse za tsiku la chiweruzirolo?
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Арабча тафсирлар:
أَلَمۡ نُهۡلِكِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Kodi sitidawaononge (anthu) akale (chifukwa cha machimo awo, monga anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu)?
Арабча тафсирлар:
ثُمَّ نُتۡبِعُهُمُ ٱلۡأٓخِرِينَ
Kenako titsatiza ena (okana Allah m’kuonongekako monga tidawachitira oyamba),
Арабча тафсирлар:
كَذَٰلِكَ نَفۡعَلُ بِٱلۡمُجۡرِمِينَ
Chomwecho tiwachitiranso ochimwa.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Арабча тафсирлар:
أَلَمۡ نَخۡلُقكُّم مِّن مَّآءٖ مَّهِينٖ
Kodi sitidakulengeni kuchokera ku madzi onyozeka, (madzi ambewu ya munthu)?
Арабча тафсирлар:
فَجَعَلۡنَٰهُ فِي قَرَارٖ مَّكِينٍ
Kenako tidawaika pamalo okhazikika (kuti chilengedwe chake chikwanire pamenepo),
Арабча тафсирлар:
إِلَىٰ قَدَرٖ مَّعۡلُومٖ
Mpaka nyengo yodziwika (imene tidaipima kuti mwana abadwe).
Арабча тафсирлар:
فَقَدَرۡنَا فَنِعۡمَ ٱلۡقَٰدِرُونَ
Tidaipima nyengoyo; taonani kupima bwino Ife opima!
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Арабча тафсирлар:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ كِفَاتًا
Kodi sitidaichite nthaka kukhala yofungatira,
Арабча тафсирлар:
أَحۡيَآءٗ وَأَمۡوَٰتٗا
Amoyo ndi akufa?
Арабча тафсирлар:
وَجَعَلۡنَا فِيهَا رَوَٰسِيَ شَٰمِخَٰتٖ وَأَسۡقَيۡنَٰكُم مَّآءٗ فُرَاتٗا
Ndipo tidaika m’menemo mapiri ataliatali (olimbitsa nthaka), ndipo takumwetsani madzi okoma.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Арабча тафсирлар:
ٱنطَلِقُوٓاْ إِلَىٰ مَا كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
(Kudzanenedwa kwa okana tsiku la chimaliziro:) Pitani kuzimene mudali kuzitsutsa zija.
Арабча тафсирлар:
ٱنطَلِقُوٓاْ إِلَىٰ ظِلّٖ ذِي ثَلَٰثِ شُعَبٖ
Pitani kumthunzi (wautsi wa ku Moto) wa nthambi zitatu,
Арабча тафсирлар:
لَّا ظَلِيلٖ وَلَا يُغۡنِي مِنَ ٱللَّهَبِ
Simthunzi (wamtendere) ndiponso siwotchinjiriza ku malawi a Moto.”
Арабча тафсирлар:
إِنَّهَا تَرۡمِي بِشَرَرٖ كَٱلۡقَصۡرِ
Ndithu motowo umaponya mphalikira (mbaliwali) zazikulu ngati nyumba,
Арабча тафсирлар:
كَأَنَّهُۥ جِمَٰلَتٞ صُفۡرٞ
Zonga ngati ngamira zachikasu.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (zimenezi).
Арабча тафсирлар:
هَٰذَا يَوۡمُ لَا يَنطِقُونَ
Ili ndi tsiku lomwe sadzayankhula.
Арабча тафсирлар:
وَلَا يُؤۡذَنُ لَهُمۡ فَيَعۡتَذِرُونَ
Ndipo sadzapatsidwa chilolezo (choyankhulira) kuti apereke madandaulo awo.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (za tsiku limenelo).
Арабча тафсирлар:
هَٰذَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِۖ جَمَعۡنَٰكُمۡ وَٱلۡأَوَّلِينَ
(Adzauzidwa kuti): Ili ndi tsiku loweruza (pakati pa abwino ndi oipa takusonkhanitsani inu (otsutsa Muhammad {s.a.w}), ndi akale (otsutsa aneneri akale).
Арабча тафсирлар:
فَإِن كَانَ لَكُمۡ كَيۡدٞ فَكِيدُونِ
Ngati muli ndi ndale (yodzipulumutsira ku chilango Changa) ndichiteni ndaleyo!
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo la Allah).
Арабча тафсирлар:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي ظِلَٰلٖ وَعُيُونٖ
Ndithu oopa (Allah tsiku limenelo) adzakhala mu mthunzi ndi mitsinje,
Арабча тафсирлар:
وَفَوَٰكِهَ مِمَّا يَشۡتَهُونَ
Ndipo adzakhala ndi zipatso zomwe azidzazifuna.
Арабча тафсирлар:
كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ هَنِيٓـَٔۢا بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
(Kudzanenedwa kwa iwo): “Idyani, imwani mokondwa chifukwa cha zabwino zomwe mudali kuchita (mu moyo wa dziko lapansi).
Арабча тафсирлар:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umo ndi mmene Ife timawalipirira ochita zabwino.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (mtendere wa Allah)
Арабча тафсирлар:
كُلُواْ وَتَمَتَّعُواْ قَلِيلًا إِنَّكُم مُّجۡرِمُونَ
Idyani, sangalalani pang’ono m’kanthawi kochepa; ndithu inu ndinu ochimwa (chifukwa chakumphatikiza Allah ndi zolengedwa).
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (mtendere wa Allah).
Арабча тафсирлар:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱرۡكَعُواْ لَا يَرۡكَعُونَ
Ndipo kukanenedwa kwa iwo: “Weramani, (pembedzani Allah).” sawerengera.
Арабча тафсирлар:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (malamulo a Allah).
Арабча тафсирлар:
فَبِأَيِّ حَدِيثِۭ بَعۡدَهُۥ يُؤۡمِنُونَ
Kodi ndi nkhani iti imene adzaikhulupirira pambuyo pa Iyi (Qur’an)?
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Сура: Мурсалот сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш