Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-'Ala   Câu:

Chương Al-'Ala

سَبِّحِ ٱسۡمَ رَبِّكَ ٱلۡأَعۡلَى
Lemekeza dzina la Mbuye wako Wapamwambamwamba (ndikuliyeretsa ku zinthu zosayenera).[417]
[417] Tanthauzo lakulemekeza dzina la Allah ndiko kukhulupilira kuti iye ndiwopatulika ku mbiri zilizonse zoipa zosamuyenera, monga kumufanizira ndizolengedwa; monga kuti anabereka kapena adaberekedwa, kapena kuti ali ndi mkazi kapenanso kuti alipo omwe amathandizana naye pa Umulungu Wake.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِي خَلَقَ فَسَوَّىٰ
Amene adalenga (chilichonse) ndikuchikonza bwinobwino (mkalengedwe kolingana).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلَّذِي قَدَّرَ فَهَدَىٰ
Amene adalamuliratu (chilichonse zochita zake) ndi kuchiongolera.[418]
[418] Allah pambuyo polenga zolengedwa Zake sadangozileka kuti zisadziwe chochita, koma cholengedwa chilichonse adachilamuliratu kuti chichite zoyenera nacho, ndipo pambuyo pake adachiongolera pa chinthu chimenecho; chidadziwa, ndipo chidachita. Munthu adamusonyeza zomwe zili ndi mazunzo mkati mwake kuti adzitalikitse nazo ndiponso adamusonyeza zabwino kuti azichite.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلَّذِيٓ أَخۡرَجَ ٱلۡمَرۡعَىٰ
Ndi Yemwenso akumeretsa msipu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَجَعَلَهُۥ غُثَآءً أَحۡوَىٰ
Ndipo nausandutsa kukhala wouma ndi wodera.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
سَنُقۡرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
[419] Mneneri Muhammad (s.a.w) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka atatu m’Swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa Qur’an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa kuti angaiwale. Choncho, apa Allah akumuletsa kuti asadzivutitse kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa lonjezo Lake. Mtumiki (s.a.w) adali kumtsikira ma surah aataliatali ndipo amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba. Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِلَّا مَا شَآءَ ٱللَّهُۚ إِنَّهُۥ يَعۡلَمُ ٱلۡجَهۡرَ وَمَا يَخۡفَىٰ
Kupatula chimene wafuna Allah (kuti uchiiwale); ndithu Iye amadziwa zoonekera ndi zimene zimabisika.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَنُيَسِّرُكَ لِلۡيُسۡرَىٰ
Ndipo tikufewetsera (njira yochitira zinthu) zabwino.[420]
[420] Tanthauzo la ‘kufewetsa’ ndiko kuti Shariya ya Chisilamu (malamulo) siili yovuta kuyikwaniritsa monga momwe adalili malamulo a zipembedzo zoyamba. Ndipo ndi malamulo othandiza anthu onse, nthawi zonse ndi pamalo paliponse.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَذَكِّرۡ إِن نَّفَعَتِ ٱلذِّكۡرَىٰ
Choncho akumbutse (wanthu powalalikira) ngati kukumbutsa kuthandiza.[421]
[421] Tanthauzo la apa sikuti Mtumiki (s.a.w) alalikire pokhapokha waona kuti ulalikiwo uthandiza ayi, koma alalikire ndithu kaya kulalikirako kuthandiza kapena ayi, monga momwe zalongosolera Ayah zotsatirazi. Kuyankhula kotere, Arabu amakutcha “iktifa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
سَيَذَّكَّرُ مَن يَخۡشَىٰ
(Palibe chikaiko ulalikiwo) aukumbukira (ndikuthandizidwa nawo) amene akuopa Allah.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَيَتَجَنَّبُهَا ٱلۡأَشۡقَى
Ndipo wamavuto ambiri, (wamakani ndi wokanira), adzitalikitsa ndi ulalikiwo.[422]
[422] “Wamavuto ambiri” apa, ndiko kuzunzika ndi matsoka. Allah akumutcha kafiri kuti “Wamavuto ambiri” chifukwa chakuti ali ndi mavuto padziko lino lapansi mpaka pa tsiku lachimaliziro. Mazunzo a tsiku lachimaliziro monga momwe tidziwira ndi chilango cha Moto chomwe chikumuyembekeza. Tsono “chilango cha padziko lapansi” ndiko kuti alibe chinthu chomutonthoza likampeza tsoka kapena vuto lililonse. Msilamu likampeza vuto amadzitonthoza ndi chikhulupiliro chake chakuti moyo wa munthu suwonjezeka ndiponso suchepa, ndikuti munthu amamwalira akamaliza moyo wake. Koma kafiri saganiza choncho; amangokukuta zala ndi kuwatukwana ma dokotala kuti sadziwa kanthu akadachita mwakutimwakuti munthuyo sakadafa. Msilamu kukampeza kusauka amadzitonthoza ndi kupilira pamodzi ndi chikhulupiliro choti “chilichonse chimachitika mchifuniro cha Allah.” Ndipo amakhala woyembekezera kuti lero kapena mawa, Allah amupatsa chisomo Chake. Koma anthu opanda chikhulupiliro amangoona kuti aponderezedwa; amayesetsa kufunafuna chuma mnjira zosayenera, ndipo akalephera amadzudzula uyu kapena kumenyana ndi uyu, ndipo amangodziona ngati wonyozeka kwambiri pa maso pa munthu wolemera.
Kotero kuti atauzidwa kuti amulambire wolemera uja kuti amupatse ndalama akhoza kuchita zotero. Ndipo tsiku lililonse njiru imamuondetsa; mwina amangodzipha monga momwe tionera masiku ano. Palibe mazunzo aakulu kuposa amenewa. Ngati muyang’ana ma Ayah 16 ndi 17 muona kuti akuthilira umboni pa zimene talongosolazi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِي يَصۡلَى ٱلنَّارَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Amene adzalowa ku moto waukulu (umene wakonzedwa kuti udzakhale malipiro ake).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ لَا يَمُوتُ فِيهَا وَلَا يَحۡيَىٰ
Ndipo sakafa m’menemo (ndikupumula kumazunzo), ndiponso sakakhala ndi moyo (wamtendere).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَدۡ أَفۡلَحَ مَن تَزَكَّىٰ
Ndithu wapambana amene wadziyeretsa (ku machimo),[423]
[423] Tanthauzo lake ndikuti amene wadziyeretsa posiya kumuphatikiza Allah ndi zolengedwa ndi kumchimwira ndi machimo onse. Machimo amaletsa ulaliki wabwino kulowa mu mtima wa munthu. (yang’anani ndemanga ya 14 mu surat ya Al-Mutaffifin).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَذَكَرَ ٱسۡمَ رَبِّهِۦ فَصَلَّىٰ
Ndikukumbukira dzina la Mbuye wake (ndi mtima wake, ndi lirime lake) uku akumapemphera.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
بَلۡ تُؤۡثِرُونَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Koma inu mukukonda kwambiri moyo wa dziko lapansi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ وَأَبۡقَىٰٓ
Pamene moyo wa tsiku lachimaliziro ndiwabwino kwambiri ndiponso wamuyaya.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ هَٰذَا لَفِي ٱلصُّحُفِ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu izi (mukuuzidwa m’Qur’an) zilipo m’mabuku oyamba, akale,[424]
[424] Mawu akuti “wapambana amene wadziyeretsa ndi kumkumbukira Mbuye wake ndi kumapemphera,” ndiponso kuti: “ tsiku lachimaliziro ndilabwino kuposa dziko lapansi” mawuwa adanenedwanso m’mabuku oyamba; sikuti Qur’an ndiyo yayamba kunena zimenezi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
صُحُفِ إِبۡرَٰهِيمَ وَمُوسَىٰ
Mabuku a Ibrahim ndi Mûsa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-'Ala
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại