Ndipo akukufulumizitsa kuti ubweretse choipa (chomwe ndi chilango chawo) m’malo mwa chabwino; ndithu chikhalirecho zilango zambiri zidapita kale (zomwe akadayenera kuchenjera nazo)! Koma Mbuye wako ndi mwini chikhululuko kwa anthu pa uchimo wawo. Ndipo ndithu Mbuye wako Ngolanga mwaukali.[238]
[238] China chodabwitsa cha anthu osakhulupilira mwa Allah ndiko kupempha chilango kuti chiwadzere m’malo mopempha zabwino. Iwo ankanena monga momwe zilili m’ndime ya 32 m’Sûrat Anfal kuti: “Ngati izi zimene wadza nazo Muhammad (s.a.w) nzoona zochokera kwa inu (Allah), choncho timenyeni ndi chimvula chamiyala yochokera ku mitambo; kapena chilango china chilichonse chopweteka. Koma ife sitimutsatirabe.” Umo ndi momwe idalimbira mitima ya osakhulupilira.
Ndipo osakhulupirira akunena: “Bwanji sichidatsitsidwe kwa iye chozizwitsa chochokera kwa Mbuye wake?” Ndithu iwe ndiwe mchenjezi, ndipo mtundu uliwonse wa anthu uli ndi muongoli (wakewake yemwe ali ndi njira zakezake zoongolera anthuwo, osati kutsata njira za muongoli wina).
Allah akudziwa chilichonse chimene mkazi asenza (m’mimba mwake) ndi zimene mimba zikupungula ndi zimene zikuonjezera. Chinthu chilichonse kwa Iye chili ndi mlingo (wake).
Ndi chimodzimodzi (kwa Iye Allah) amene akubisa liwu lake mwa inu ndi amene akulikweza ndi yemwe akudzibisa usiku ndi yemwe akuyenda usana, (onse akuwadziwa).
Ndipo mphezi imalemekeza Allah ndi kumthokoza, naonso angelo (amamlemekeza) momuopa. Ndipo Allah, amatumiza kumenya kwa mphezi ndi kummenya nako amene wamfuna. Ndipo iwo (okanira) akutsutsana pa za Allah (kuti alipo kapena palibe pomwe Iye alipo). Ndipo Iye Ngolanga mwaukali.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
搜索结果:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".