Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 拉尔德   段:
لَهُۥ دَعۡوَةُ ٱلۡحَقِّۚ وَٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ مِن دُونِهِۦ لَا يَسۡتَجِيبُونَ لَهُم بِشَيۡءٍ إِلَّا كَبَٰسِطِ كَفَّيۡهِ إِلَى ٱلۡمَآءِ لِيَبۡلُغَ فَاهُ وَمَا هُوَ بِبَٰلِغِهِۦۚ وَمَا دُعَآءُ ٱلۡكَٰفِرِينَ إِلَّا فِي ضَلَٰلٖ
Kwa Iye ndiko kuli (kuvomera) pempho lachoonadi. Ndipo aja amene akupempha mafano kusiya Iye (Allah), sawayankha pa chilichonse koma (chikhalidwe chawo) chili ngati yemwe akutambasulira madzi manja ake awiri kuti afike m’kamwa mwake; koma sangafike. Ndipo mapemphero a osakhulupirira sali kanthu koma ndi otaika basi (opita pachabe).
阿拉伯语经注:
وَلِلَّهِۤ يَسۡجُدُۤ مَن فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ طَوۡعٗا وَكَرۡهٗا وَظِلَٰلُهُم بِٱلۡغُدُوِّ وَٱلۡأٓصَالِ۩
Ndipo amene ali kumwamba ndi pansi amamgwadira Allah mwachifuniro ndi mopanda chifuniro; ndiponso zithunzi zawo (zimamgwadira) m’mawa ndi madzulo.
阿拉伯语经注:
قُلۡ مَن رَّبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ قُلِ ٱللَّهُۚ قُلۡ أَفَٱتَّخَذۡتُم مِّن دُونِهِۦٓ أَوۡلِيَآءَ لَا يَمۡلِكُونَ لِأَنفُسِهِمۡ نَفۡعٗا وَلَا ضَرّٗاۚ قُلۡ هَلۡ يَسۡتَوِي ٱلۡأَعۡمَىٰ وَٱلۡبَصِيرُ أَمۡ هَلۡ تَسۡتَوِي ٱلظُّلُمَٰتُ وَٱلنُّورُۗ أَمۡ جَعَلُواْ لِلَّهِ شُرَكَآءَ خَلَقُواْ كَخَلۡقِهِۦ فَتَشَٰبَهَ ٱلۡخَلۡقُ عَلَيۡهِمۡۚ قُلِ ٱللَّهُ خَٰلِقُ كُلِّ شَيۡءٖ وَهُوَ ٱلۡوَٰحِدُ ٱلۡقَهَّٰرُ
Nena: “Ndani Mbuye wa thambo ndi nthaka?” Nena: “Ndi Allah.” Nena: “Mukudzipangira milungu ina kusiya Iye, (milungu) yomwe siingadzibweretsere zabwino kapena kudzichotsera sautso?” Nena: “Kodi angakhale ofanana wakhungu ndi wopenya? Kodi kapena ungafanane mdima ndi kuunika?” Kapena ampangira anzake Allah omwe adalenga zofanana ndi zomwe Allah adalenga kotero kuti zolengedwa (zambali ziwirizo) zikufanana kwa iwo? Nena: “Allah ndiye Mlengi wa chilichonse. Ndipo Iye ndi Mmodzi Wayekha, Wopambana (ndipo chimene Iye wafuna ndi chimene chimachitika)”
阿拉伯语经注:
أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَسَالَتۡ أَوۡدِيَةُۢ بِقَدَرِهَا فَٱحۡتَمَلَ ٱلسَّيۡلُ زَبَدٗا رَّابِيٗاۖ وَمِمَّا يُوقِدُونَ عَلَيۡهِ فِي ٱلنَّارِ ٱبۡتِغَآءَ حِلۡيَةٍ أَوۡ مَتَٰعٖ زَبَدٞ مِّثۡلُهُۥۚ كَذَٰلِكَ يَضۡرِبُ ٱللَّهُ ٱلۡحَقَّ وَٱلۡبَٰطِلَۚ فَأَمَّا ٱلزَّبَدُ فَيَذۡهَبُ جُفَآءٗۖ وَأَمَّا مَا يَنفَعُ ٱلنَّاسَ فَيَمۡكُثُ فِي ٱلۡأَرۡضِۚ كَذَٰلِكَ يَضۡرِبُ ٱللَّهُ ٱلۡأَمۡثَالَ
Adatsitsa madzi, kuchokera ku mitambo, ndipo zigwa zidayendetsa madzi mwa mlingo wake. Ndipo msefukiro wamadzi udatenga thovu lomwe limayandama pamwamba pa madzi. Ndiponso zomwe amazisungunula pa moto chifukwa chofuna zodzikongoletseranazo kapena ziwiya (monga zagolide ndi siliva), mumakhalanso thovu chimodzimodzi. Umo ndi momwe Allah akuperekera fanizo lachoonadi ndi fanizo lachonama. Tsono thovu, limangopita monga zitakataka chabe; koma zimene zimathandiza anthu, zimakhazikika m’nthaka. Umo ndi m’mene Allah akuperekera mafanizo.[240]
[240] Nthawi zambiri zinthu zachabe zimagundika kwambiri, koma sizikhalira kuzimilira. Choncho.nkofunika kwa anthu kuchenjera ndi zinthu zotere. Asazikhulupirire chifukwa choona kuti zagundika, koma azipenyetsetse bwino, mofatsa kuti kuona kwake kwa zinthu kutsimikizike kwa iye.
阿拉伯语经注:
لِلَّذِينَ ٱسۡتَجَابُواْ لِرَبِّهِمُ ٱلۡحُسۡنَىٰۚ وَٱلَّذِينَ لَمۡ يَسۡتَجِيبُواْ لَهُۥ لَوۡ أَنَّ لَهُم مَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا وَمِثۡلَهُۥ مَعَهُۥ لَٱفۡتَدَوۡاْ بِهِۦٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ سُوٓءُ ٱلۡحِسَابِ وَمَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمِهَادُ
Amene adavomera Mbuye wawo, adzapeza zabwino. Koma amene sadamuvomere, ngakhale akadakhala nazo zonse za m’dziko ndi zina zonga izo pamodzi, ndikuzipereka kuti adziombolere (sizikadavomerezedwa). Ndipo iwo adzakhala ndi chiwerengero choipa. Ndipo malo awo ndi ku Jahannam, taonani kuipa kwa malo okakhazikikamo!
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 拉尔德
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭