Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 拉尔德   段:
۞ أَفَمَن يَعۡلَمُ أَنَّمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَ ٱلۡحَقُّ كَمَنۡ هُوَ أَعۡمَىٰٓۚ إِنَّمَا يَتَذَكَّرُ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Kodi amene akudziwa kuti zimene zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako nzoona, angafanane ndi yemwe ali wakhungu? Ndithudi eni nzeru ndi okhawo olingalira.
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِينَ يُوفُونَ بِعَهۡدِ ٱللَّهِ وَلَا يَنقُضُونَ ٱلۡمِيثَٰقَ
(Iwowo ndi) omwe akukwaniritsa lonjezo la Allah, ndipo saswa lonjezo lomangika (pakati pawo ndi anzawo).
阿拉伯语经注:
وَٱلَّذِينَ يَصِلُونَ مَآ أَمَرَ ٱللَّهُ بِهِۦٓ أَن يُوصَلَ وَيَخۡشَوۡنَ رَبَّهُمۡ وَيَخَافُونَ سُوٓءَ ٱلۡحِسَابِ
Ndiponso omwe akulumikiza zomwe Allah walamula kuti zilumikizidwe (monga chibale), pamodzi ndi kuopa Mbuye wawo ndi kuopanso chiwerengero choipa (chomwe chidzawapeza oipa tsiku lachimaliziro tero amayesetsa kuwapatuka machitidwe oipa).
阿拉伯语经注:
وَٱلَّذِينَ صَبَرُواْ ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِمۡ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَأَنفَقُواْ مِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ سِرّٗا وَعَلَانِيَةٗ وَيَدۡرَءُونَ بِٱلۡحَسَنَةِ ٱلسَّيِّئَةَ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ عُقۡبَى ٱلدَّارِ
Ndi omwenso amapirira chifukwa chofuna chiyanjo cha Mbuye wawo ndi kupemphera Swala ndi kupereka mu zomwe tawapatsa, mobisa ndi moonekera, ndi kuchotsa choipa ndi chabwino (pochita chabwino pa choipacho); iwo ndi omwe adzapeza malipiro (abwino) a ku Nyumba ya tsiku la chimaliziro.[241]
[241] Kunena koti: “Kupereka mobisa ndi moonekera.” kukusonyeza kuti sadaka zomwe munthu akupereka asazifunire nthawi yake yeniyeni yoperekera. Koma nthawi iliyonse. Ngati nkofunika kupereka mobisa kuopera kuti omwe akupatsidwawo asanyozeke kumaso kwa anthu, apereke mobisa. Ndipo ngati nkofunika kupereka moonetsera, ncholinga choti anthu ena atsanzire, monga kusonkhetsa kwa poyera, apereke moonekera. Tsono kunena kwakuti: “Kuchotsa choipa ndi chabwino,” kukutanthauza kuti anthu amenewa akawachitira zoipa ena, iwo sabwezera zoipazo. Koma amapitiriza kuchitira anthu oipawo zabwino.
阿拉伯语经注:
جَنَّٰتُ عَدۡنٖ يَدۡخُلُونَهَا وَمَن صَلَحَ مِنۡ ءَابَآئِهِمۡ وَأَزۡوَٰجِهِمۡ وَذُرِّيَّٰتِهِمۡۖ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ يَدۡخُلُونَ عَلَيۡهِم مِّن كُلِّ بَابٖ
Minda yamuyaya adzailowa iwo (pamodzi) ndi amene adachita zabwino mwa makolo awo, akazi awo ndi ana awo; ndipo angelo azikalowa kwa iwo khomo lililonse.
阿拉伯语经注:
سَلَٰمٌ عَلَيۡكُم بِمَا صَبَرۡتُمۡۚ فَنِعۡمَ عُقۡبَى ٱلدَّارِ
(Uku akunena): “Salaamun Alayikumu (Mtendere uli pa inu) chifukwa chakupirira kwanu (pochita zabwino ndi kusiya zoipa ndi kukhala mwaubwino ndi anzanu)! Taona kukhala bwino zotsatira za Nyumba ya tsiku la chimaliziro.”
阿拉伯语经注:
وَٱلَّذِينَ يَنقُضُونَ عَهۡدَ ٱللَّهِ مِنۢ بَعۡدِ مِيثَٰقِهِۦ وَيَقۡطَعُونَ مَآ أَمَرَ ٱللَّهُ بِهِۦٓ أَن يُوصَلَ وَيُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمُ ٱللَّعۡنَةُ وَلَهُمۡ سُوٓءُ ٱلدَّارِ
Koma amene akuswa lonjezo la Allah (ndi malonjezo a anthu anzawo) pambuyo polimanga motsimikiza, ndi kumadula chimene Allah walamula kuti chilumikizidwe, ndi kumaononga padziko, iwowo ndiwo adzapeza tembelero; ndiponso adzapeza Nyumba yoipa.
阿拉伯语经注:
ٱللَّهُ يَبۡسُطُ ٱلرِّزۡقَ لِمَن يَشَآءُ وَيَقۡدِرُۚ وَفَرِحُواْ بِٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَمَا ٱلۡحَيَوٰةُ ٱلدُّنۡيَا فِي ٱلۡأٓخِرَةِ إِلَّا مَتَٰعٞ
Allah amamtambasulira rizq amene wamfuna, ndipo amamfumbatiranso (kumchepetsera arnene wamfuna). Ndipo akusangalalira moyo wa pa dziko lapansi, suli kanthu moyo wapadziko poyerekeza ndi moyo wa pambuyo pa imfa, koma ndi chisangalalo chochepa basi.
阿拉伯语经注:
وَيَقُولُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَوۡلَآ أُنزِلَ عَلَيۡهِ ءَايَةٞ مِّن رَّبِّهِۦۚ قُلۡ إِنَّ ٱللَّهَ يُضِلُّ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِيٓ إِلَيۡهِ مَنۡ أَنَابَ
Ndipo amene sadakhulupirire akunena: “Bwanji sichidatsitsidwe kwa iye chozizwitsa kuchokera kwa Mbuye wake?”‘ Nena: “Ndithu Allah amalekelera kusokera amene wamfuna (chifukwa chosafuna kutembenukira kwa Iye Allah); ndipo amamuongolera amene akutembenukira kwa Iye.”
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَتَطۡمَئِنُّ قُلُوبُهُم بِذِكۡرِ ٱللَّهِۗ أَلَا بِذِكۡرِ ٱللَّهِ تَطۡمَئِنُّ ٱلۡقُلُوبُ
(Awa ndi) amene akhulupirira, ndipo mitima yawo ikukhazikika pokumbukira Allah. Dziwani, pokumbukira Allah mitima imakhazikika (imatonthola).
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 拉尔德
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭