আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আত-তীন   আয়াত:

ছুৰা আত-তীন

وَٱلتِّينِ وَٱلزَّيۡتُونِ
Ndikulumbilira mitengo ya Mkuyu ndi Zitona (pansi pa mitengo imeneyi Ibrahim ndi Nuh (Nowa) adapeza uneneri),
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَطُورِ سِينِينَ
Ndi phiri la Sinai (pamene Allah adamulankhulira Mûsa),
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ ٱلۡأَمِينِ
Ndiponso mzinda uwu (wolemekezeka) wamtendere; (Makka, womwe adapatsiridwa uneneri Muhammad) (s.a.w).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِيٓ أَحۡسَنِ تَقۡوِيمٖ
Palibe chikaiko, tamulenga munthu mkalengedwe kabwino, kolingana (ndipo ali ndi mbiri zabwino).[457]
[457] M’gulu la nyama palibe yopambana kuposa munthu mkalengedwe ndi pa nzeru.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ رَدَدۡنَٰهُ أَسۡفَلَ سَٰفِلِينَ
Pambuyo pake tamubwezera pansi kumposa wa pansi.[458]
[458] Munthu ali ndi makhalidwe awiri: Ngati agwiritsa ntchito nzeru zake amaongoka ndipo amaiposa nyama ili yonse. Koma ngati sagwiritsa ntchito nzeru zake amasokera ndi kukhala wapansi kuposa nyama zonse.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ فَلَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونٖ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, adzakhala nawo iwo malipiro osatha.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَمَا يُكَذِّبُكَ بَعۡدُ بِٱلدِّينِ
Tsono nchiyani chakuchititsa kuti ukanire kuuka ndi malipiro pambuyo (poona mphamvu zathu pa chilichonse)?[459]
[459] (Ndime 7-8) Allah akuuza munthu kuti: Pambuyo podziwa kuti Allah ndi Yemwe adapanga zimenezo, ndi chiyani nanga chikumukaikitsa za tsiku la chiweruziro?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَلَيۡسَ ٱللَّهُ بِأَحۡكَمِ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Kodi Allah si Muweruzi wa nzeru kuposa aweruzi onse?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আত-তীন
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

চেৱা ভাষাত কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ- অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা। ২০২০ চন।

বন্ধ