Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Ash-Shams   Vers:

Ash-Shams

وَٱلشَّمۡسِ وَضُحَىٰهَا
Ndikulumbilira dzuwa ndi dangalira lake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلۡقَمَرِ إِذَا تَلَىٰهَا
Ndi mwezi pamene ukulitsatira (dzuwalo ndikulowa mmalo mwake powalitsa dziko dzuwalo litalowa).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا جَلَّىٰهَا
Ndi usana pamene ukulisonyeza poyera (kuti lisaphimbidwe).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰهَا
Ndi usiku pamene ukuliphimba.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلسَّمَآءِ وَمَا بَنَىٰهَا
Ndi thambo ndi (Mwini mphamvu zonse Wamkulu) Yemwe adalimanga ndi kulitukula (mwaluso).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا طَحَىٰهَا
Ndi nthaka ndi (Mwini mphamvu zonse Wamkulu), Yemwe adaiyala (mbali zonse ndi kuichita kukhala ngati choyala).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَنَفۡسٖ وَمَا سَوَّىٰهَا
Ndi mzimu ndi Yemwe adawulinganiza (powupatsa mphamvu).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَأَلۡهَمَهَا فُجُورَهَا وَتَقۡوَىٰهَا
Ndipo adaudziwitsa zoipa zake ndi zabwino zake; (ndi kuwupatsa ufulu ndi mphamvu zochitira zimene ukufuna).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قَدۡ أَفۡلَحَ مَن زَكَّىٰهَا
Ndithu wapambana amene wauyeretsa.[443]
[443] Kuyeretsa mzimu ndiko kuukongoletsa ndi maphunziro ndi ntchito zabwino. Zimenezi ndizo zimamkwanitsa munthu kuti atchulidwe munthu. Ndipo zimenezi ndizo zingapereke ulemelero kwa munthu pa dziko mpaka pa tsiku lachimaliziro.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَدۡ خَابَ مَن دَسَّىٰهَا
Ndipo ndithu wataika amene wauononga.[444]
[444] Kuwuononga mzimu ndiko kuuchitira mphwayi; kungoulekelera ndikumautsatira pa zimene ufuna mpaka kulowa mu uve ndi m’machimo a umbuli ndipo ndi kuonongeka pa dziko lino mpaka pa tsiku lachimaliziro.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ بِطَغۡوَىٰهَآ
Thamud (Samudu) adakanira (Mneneri wawo) chifukwa cha kulumpha malire kwawo.[445]
[445] (Ndime 11-15) Asamudu atchulidwa m’surat AL-FAJR. Anthu awa adamukana Mtumiki wawo, Mtumiki Swalih (a.s); adamuuza kuti ngati afuna amukhulupirire, atulutse ngamira kuchokera mthanthwe, apo ndipo adzamukhulupilira kuti ndi Mneneri. Swalih adampempha Allah, ndipo lidasweka thanthwe lija ndikutulukamo ngamira monga momwe adafunira anthu aja. Koma sadamukhulupirirebe. Mneneri Swalih (a.s) adawauza kuti: “Chenjerani ndi ngamira ya Allah iyi, musaikhudze ndi choipa chilichonse.” Ndipo adawakakamiza kuti pa tsiku limene ngamira ija ikumwa madzi, iwo asatunge madzi. Ndiponso pa tsiku limene iwo akutunga madzi ngamira siidzamwa madzi. Koma adamkanira. Ndipo m’modzi wa iwo amene adali wamphulupulu adaipha ngamira ija. Allah nthawi yomweyo adawatsitsira chilango chifukwa cha machimo awo, chomwe chidawakwanira onse kuyambira uja wopha ngamira ndi ena onse.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِذِ ٱنۢبَعَثَ أَشۡقَىٰهَا
Pamene woipitsitsa wawo adadzipereka (kupha ngamira yozizwitsa).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَقَالَ لَهُمۡ رَسُولُ ٱللَّهِ نَاقَةَ ٱللَّهِ وَسُقۡيَٰهَا
Pamenepo Mneneri wa Allah (Swaleh) adawauza: “Isiyeni ngamira ya Allah (idye mdziko la Allah). Musailetse kumwa madzi (pa tsiku lake).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَكَذَّبُوهُ فَعَقَرُوهَا فَدَمۡدَمَ عَلَيۡهِمۡ رَبُّهُم بِذَنۢبِهِمۡ فَسَوَّىٰهَا
Koma adamutsutsa ndikuipha; kwa chifukwa chimenecho Mbuye wawo (Allah) adawaononga chifukwa cha tchimo lawo; adangowafafaniza (onse mnthaka).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَا يَخَافُ عُقۡبَٰهَا
Iye saopa zotsatira za chilangochi (chifukwa amenewa ndi malipiro a chilungamo pa zomwe adachita).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Ash-Shams
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen