আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আশ্ব-শ্বামচ   আয়াত:

ছুৰা আশ্ব-শ্বামচ

وَٱلشَّمۡسِ وَضُحَىٰهَا
Ndikulumbilira dzuwa ndi dangalira lake.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلۡقَمَرِ إِذَا تَلَىٰهَا
Ndi mwezi pamene ukulitsatira (dzuwalo ndikulowa mmalo mwake powalitsa dziko dzuwalo litalowa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا جَلَّىٰهَا
Ndi usana pamene ukulisonyeza poyera (kuti lisaphimbidwe).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰهَا
Ndi usiku pamene ukuliphimba.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلسَّمَآءِ وَمَا بَنَىٰهَا
Ndi thambo ndi (Mwini mphamvu zonse Wamkulu) Yemwe adalimanga ndi kulitukula (mwaluso).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا طَحَىٰهَا
Ndi nthaka ndi (Mwini mphamvu zonse Wamkulu), Yemwe adaiyala (mbali zonse ndi kuichita kukhala ngati choyala).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَنَفۡسٖ وَمَا سَوَّىٰهَا
Ndi mzimu ndi Yemwe adawulinganiza (powupatsa mphamvu).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَأَلۡهَمَهَا فُجُورَهَا وَتَقۡوَىٰهَا
Ndipo adaudziwitsa zoipa zake ndi zabwino zake; (ndi kuwupatsa ufulu ndi mphamvu zochitira zimene ukufuna).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
قَدۡ أَفۡلَحَ مَن زَكَّىٰهَا
Ndithu wapambana amene wauyeretsa.[443]
[443] Kuyeretsa mzimu ndiko kuukongoletsa ndi maphunziro ndi ntchito zabwino. Zimenezi ndizo zimamkwanitsa munthu kuti atchulidwe munthu. Ndipo zimenezi ndizo zingapereke ulemelero kwa munthu pa dziko mpaka pa tsiku lachimaliziro.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَقَدۡ خَابَ مَن دَسَّىٰهَا
Ndipo ndithu wataika amene wauononga.[444]
[444] Kuwuononga mzimu ndiko kuuchitira mphwayi; kungoulekelera ndikumautsatira pa zimene ufuna mpaka kulowa mu uve ndi m’machimo a umbuli ndipo ndi kuonongeka pa dziko lino mpaka pa tsiku lachimaliziro.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ بِطَغۡوَىٰهَآ
Thamud (Samudu) adakanira (Mneneri wawo) chifukwa cha kulumpha malire kwawo.[445]
[445] (Ndime 11-15) Asamudu atchulidwa m’surat AL-FAJR. Anthu awa adamukana Mtumiki wawo, Mtumiki Swalih (a.s); adamuuza kuti ngati afuna amukhulupirire, atulutse ngamira kuchokera mthanthwe, apo ndipo adzamukhulupilira kuti ndi Mneneri. Swalih adampempha Allah, ndipo lidasweka thanthwe lija ndikutulukamo ngamira monga momwe adafunira anthu aja. Koma sadamukhulupirirebe. Mneneri Swalih (a.s) adawauza kuti: “Chenjerani ndi ngamira ya Allah iyi, musaikhudze ndi choipa chilichonse.” Ndipo adawakakamiza kuti pa tsiku limene ngamira ija ikumwa madzi, iwo asatunge madzi. Ndiponso pa tsiku limene iwo akutunga madzi ngamira siidzamwa madzi. Koma adamkanira. Ndipo m’modzi wa iwo amene adali wamphulupulu adaipha ngamira ija. Allah nthawi yomweyo adawatsitsira chilango chifukwa cha machimo awo, chomwe chidawakwanira onse kuyambira uja wopha ngamira ndi ena onse.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِذِ ٱنۢبَعَثَ أَشۡقَىٰهَا
Pamene woipitsitsa wawo adadzipereka (kupha ngamira yozizwitsa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَقَالَ لَهُمۡ رَسُولُ ٱللَّهِ نَاقَةَ ٱللَّهِ وَسُقۡيَٰهَا
Pamenepo Mneneri wa Allah (Swaleh) adawauza: “Isiyeni ngamira ya Allah (idye mdziko la Allah). Musailetse kumwa madzi (pa tsiku lake).”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَكَذَّبُوهُ فَعَقَرُوهَا فَدَمۡدَمَ عَلَيۡهِمۡ رَبُّهُم بِذَنۢبِهِمۡ فَسَوَّىٰهَا
Koma adamutsutsa ndikuipha; kwa chifukwa chimenecho Mbuye wawo (Allah) adawaononga chifukwa cha tchimo lawo; adangowafafaniza (onse mnthaka).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَلَا يَخَافُ عُقۡبَٰهَا
Iye saopa zotsatira za chilangochi (chifukwa amenewa ndi malipiro a chilungamo pa zomwe adachita).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আশ্ব-শ্বামচ
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

চেৱা ভাষাত কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ- অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা। ২০২০ চন।

বন্ধ