Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura An-Naazi'aat   Versículo:

Sura An-Naazi'aat

وَٱلنَّٰزِعَٰتِ غَرۡقٗا
Ndikulumbilira (angelo) amene amazula mwamphamvu (mizimu ya osakhulupirira).[379]
[379] (Ndime 1-5) M’Qur’an nthawi zambiri Allah amalumbilira zolengedwa Zake; zamoyo ndi zopanda moyo, zooneka ndi zosaoneka. Cholinga ndikutilimbikitsa kuti tikhale olingalira luso Lake pa chinthu chilichonse chimene wachilumbilira kuti tizindikire ulemelero Wake ndi mphamvu Zake zoposa.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلنَّٰشِطَٰتِ نَشۡطٗا
Ndikulumbiliranso (angelo) amene amachotsa moleza (mizimu ya okhulupirira).
Las Exégesis Árabes:
وَٱلسَّٰبِحَٰتِ سَبۡحٗا
Ndi omwe amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (ponka nayo ku malo ake oyembekezera).
Las Exégesis Árabes:
فَٱلسَّٰبِقَٰتِ سَبۡقٗا
Ndi iwo amene akupikisana pokwaniritsa malamulo a Allah.
Las Exégesis Árabes:
فَٱلۡمُدَبِّرَٰتِ أَمۡرٗا
Ndi iwo (angelo) amene akulongosola malamulo (Ake). (Ndithudi inu anthu mudzauka kwa akufa).
Las Exégesis Árabes:
يَوۡمَ تَرۡجُفُ ٱلرَّاجِفَةُ
Patsiku lomwe (lipenga loyamba lidzaimbidwa), dziko lapansi ndi mapiri ake zidzagwedezeka (ndipo aliyense adzafa).
Las Exégesis Árabes:
تَتۡبَعُهَا ٱلرَّادِفَةُ
Ndipo kudzatsatira kuyimba kwa lipenga lachiwiri (kumene kudzaukitsa akufa onse).
Las Exégesis Árabes:
قُلُوبٞ يَوۡمَئِذٖ وَاجِفَةٌ
Tsiku limenelo mitima idzanjenjemera ndi kuopa.
Las Exégesis Árabes:
أَبۡصَٰرُهَا خَٰشِعَةٞ
Maso a eni mitimayo adzakhala ozyolika (chifukwa chamadandaulo);
Las Exégesis Árabes:
يَقُولُونَ أَءِنَّا لَمَرۡدُودُونَ فِي ٱلۡحَافِرَةِ
(Osakhulupirira) akunena: “Kodi nzoona tidzabwezedwa pambuyo pa imfa monga tidalili kale?”
Las Exégesis Árabes:
أَءِذَا كُنَّا عِظَٰمٗا نَّخِرَةٗ
“Pomwe ife titakhala mafupa ofumbwa (tingabwezedwe ndi kuukitsidwa mwa tsopano)?”
Las Exégesis Árabes:
قَالُواْ تِلۡكَ إِذٗا كَرَّةٌ خَاسِرَةٞ
Adanena (mokanira ndi mwachipongwe): “Choncho kubwerera kumeneko ngati kudzakhalepodi kudzakhala kotaika (ndi kopanda phindu kwa ife. Pomwe ife sindife oyenera kutaika).”
Las Exégesis Árabes:
فَإِنَّمَا هِيَ زَجۡرَةٞ وَٰحِدَةٞ
(Musaganize kubwererako nchinthu chovuta). Ndithundithu Kiyamayo ndi nkuwo umodzi.
Las Exégesis Árabes:
فَإِذَا هُم بِٱلسَّاهِرَةِ
Mwadzidzidzi (zolengedwa zonse) zidzangoona zili pa dziko latsopano (zili zamoyo).
Las Exégesis Árabes:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ
Kodi yakufika (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Mûsa?[380]
[380] Kuyambira Ayah iyi mpaka Ayah 26 Allah akumtonthoza mneneri Wake pomuuza nkhani ya Mneneri Musa momwe Farawo adamkanira, ndikuti asaganize kuti vutoli lampeza iye yekha koma kuti aneneri enanso akale lidawaonekeranso. Ndiponso m’ma Ayah amenewa muli chenjezo kwa akafiri kuti aope Allah kuti asawalange monga adamulangira Farawo ndi anthu ake amene adali kutsutsana ndi Allah.
Las Exégesis Árabes:
إِذۡ نَادَىٰهُ رَبُّهُۥ بِٱلۡوَادِ ٱلۡمُقَدَّسِ طُوًى
Pamene Mbuye wake adamuitana pa chigwa choyera (chotchedwa) Tuwaa.
Las Exégesis Árabes:
ٱذۡهَبۡ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
(Adamuuza kuti) pita kwa Farawo ndithu iye wapyola malire, (mkudzitukumula kwake ndikupondereza anthu).
Las Exégesis Árabes:
فَقُلۡ هَل لَّكَ إِلَىٰٓ أَن تَزَكَّىٰ
Choncho ukamuuze kuti: “Kodi ukufuna kudziyeretsa?”
Las Exégesis Árabes:
وَأَهۡدِيَكَ إِلَىٰ رَبِّكَ فَتَخۡشَىٰ
“Ndikuti ndikuongolere kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?”
Las Exégesis Árabes:
فَأَرَىٰهُ ٱلۡأٓيَةَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
(Basi Mûsa) adamuonetsa (Farawo) chozizwitsa chachikulu.
Las Exégesis Árabes:
فَكَذَّبَ وَعَصَىٰ
Koma (Farawo) adatsutsa (Mûsa pazimene adadza nazo zija) ndi kunyoza.
Las Exégesis Árabes:
ثُمَّ أَدۡبَرَ يَسۡعَىٰ
Kenaka adabwerera uku akulimbika kutsutsana naye (Allah),
Las Exégesis Árabes:
فَحَشَرَ فَنَادَىٰ
Adawasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu;
Las Exégesis Árabes:
فَقَالَ أَنَا۠ رَبُّكُمُ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Nanena: “Ine ndine mbuye wanu wapamwambamwamba!”
Las Exégesis Árabes:
فَأَخَذَهُ ٱللَّهُ نَكَالَ ٱلۡأٓخِرَةِ وَٱلۡأُولَىٰٓ
Pamenepo Allah adamulanga chifukwa cha mawu ake omaliza ndi oyamba.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَعِبۡرَةٗ لِّمَن يَخۡشَىٰٓ
Ndithu pa zimenezi pali phunziro (lalikulu) kwa yemwe akuopa Allah.
Las Exégesis Árabes:
ءَأَنتُمۡ أَشَدُّ خَلۡقًا أَمِ ٱلسَّمَآءُۚ بَنَىٰهَا
Kodi kulengedwa kwanu, (inu osakhulupirira kuti muuke) nkovuta kapena thambo limene adalimanga (posonkhanitsa mbali zake zosiyanasiyana ndikukhala chinthu chimodzi)?[381]
[381] Tanthauzo lake ndikuti: “Kodi chilengedwe chanu nchovuta kwambiri kuposa chilengedwe cha thambo pamene inu mukuganiza kuti Allah sangathe kukudzutsani pambuyo pa imfa?”
Las Exégesis Árabes:
رَفَعَ سَمۡكَهَا فَسَوَّىٰهَا
Adatukula nsinkhu wake ndikulikonza bwino (popanda pena pong’ambika kapena posiyana ndi pena).
Las Exégesis Árabes:
وَأَغۡطَشَ لَيۡلَهَا وَأَخۡرَجَ ضُحَىٰهَا
Ndipo amauvindikira usiku wake ndi mdima ndipo amatulutsa kuwala wake.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ ذَٰلِكَ دَحَىٰهَآ
Ndipo pambuyo pazimenezo, nthaka adaiyala (kuti ikhale yoyenera kuikhala).
Las Exégesis Árabes:
أَخۡرَجَ مِنۡهَا مَآءَهَا وَمَرۡعَىٰهَا
Adatulutsa m’menemo madzi ake (potulutsa akasupe) ndikumeretsa msipu wake;
Las Exégesis Árabes:
وَٱلۡجِبَالَ أَرۡسَىٰهَا
Ndipo mapiri adawakhazikitsa (ndikuwalimbika);
Las Exégesis Árabes:
مَتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Adachita zonsezi) chifukwa chokusangalatsani inu ndi ziweto zanu.[382]
[382] Mu Ayah iyi Allah akusonyeza kuti Iye ndi Mwini mphamvu zonse zochitira chinthu chilichonse chachikulu kuposa kuwaukitsa akufa; ndiponso akukumbutsa ufulu Wake waukulu womwe adatichitira potipatsa zinthu zonsezo kuti tithandizike nazo.
Las Exégesis Árabes:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلطَّآمَّةُ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Choncho likadzafika tsoka lalikulu (tsiku la Qiyâma).
Las Exégesis Árabes:
يَوۡمَ يَتَذَكَّرُ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا سَعَىٰ
Tsiku limenelo munthu adzakumbukira zimene adachita, (zabwino ndi zoipa).
Las Exégesis Árabes:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِمَن يَرَىٰ
Ndipo Moto waukali udzawonetsedwa kwa yense openya.
Las Exégesis Árabes:
فَأَمَّا مَن طَغَىٰ
Tsono amene adapyola malire (pochita machimo),
Las Exégesis Árabes:
وَءَاثَرَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Ndikudzisankhira (yekha) moyo wa pa dziko lapansi,
Las Exégesis Árabes:
فَإِنَّ ٱلۡجَحِيمَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Jahannam ndiwo malo ake.
Las Exégesis Árabes:
وَأَمَّا مَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ وَنَهَى ٱلنَّفۡسَ عَنِ ٱلۡهَوَىٰ
Tsono amene akuopa kuti adzaimilira pamaso pa Mbuye wake, nauletsa mtima wake ku zilakolako zoipa,
Las Exégesis Árabes:
فَإِنَّ ٱلۡجَنَّةَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Munda wamtendere ndiwo adzakhale malo ake.
Las Exégesis Árabes:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلسَّاعَةِ أَيَّانَ مُرۡسَىٰهَا
Akukufunsa (iwe Mtumiki) (s.a.w) za nthawi (ya tsiku lachimaliziro kuti): “Idzakhala liti?”
Las Exégesis Árabes:
فِيمَ أَنتَ مِن ذِكۡرَىٰهَآ
Uli ndi mphamvu yanji iwe yofotokozera za tsikulo? (Iwe ulibe kuzindikira za nthawiyo kotero kuti ungaitchule kwa iwo).
Las Exégesis Árabes:
إِلَىٰ رَبِّكَ مُنتَهَىٰهَآ
Kwa Mbuye wako ndiko kuli mathero ake.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّمَآ أَنتَ مُنذِرُ مَن يَخۡشَىٰهَا
Iwe (ntchito yako) ndikuwachenjeza amene akuiopa; (osati kulengeza zanthawi yake).
Las Exégesis Árabes:
كَأَنَّهُمۡ يَوۡمَ يَرَوۡنَهَا لَمۡ يَلۡبَثُوٓاْ إِلَّا عَشِيَّةً أَوۡ ضُحَىٰهَا
Tsiku limene adzaiona adzakhala ngati sadakhale (pa dziko nthawi yayitali), koma ngati madzulo amodzi kapena masana ake (nthawi ya m’mawa).[383]
[383] Apa tanthauzo lake ndikuti adzaona masiku onse amene adakhala m’dziko ngati lidali ola limodzi.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura An-Naazi'aat
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar