Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu En Naziat   Ajeti:

Suretu En Naziat

وَٱلنَّٰزِعَٰتِ غَرۡقٗا
Ndikulumbilira (angelo) amene amazula mwamphamvu (mizimu ya osakhulupirira).[379]
[379] (Ndime 1-5) M’Qur’an nthawi zambiri Allah amalumbilira zolengedwa Zake; zamoyo ndi zopanda moyo, zooneka ndi zosaoneka. Cholinga ndikutilimbikitsa kuti tikhale olingalira luso Lake pa chinthu chilichonse chimene wachilumbilira kuti tizindikire ulemelero Wake ndi mphamvu Zake zoposa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلنَّٰشِطَٰتِ نَشۡطٗا
Ndikulumbiliranso (angelo) amene amachotsa moleza (mizimu ya okhulupirira).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلسَّٰبِحَٰتِ سَبۡحٗا
Ndi omwe amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (ponka nayo ku malo ake oyembekezera).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَٱلسَّٰبِقَٰتِ سَبۡقٗا
Ndi iwo amene akupikisana pokwaniritsa malamulo a Allah.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَٱلۡمُدَبِّرَٰتِ أَمۡرٗا
Ndi iwo (angelo) amene akulongosola malamulo (Ake). (Ndithudi inu anthu mudzauka kwa akufa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَوۡمَ تَرۡجُفُ ٱلرَّاجِفَةُ
Patsiku lomwe (lipenga loyamba lidzaimbidwa), dziko lapansi ndi mapiri ake zidzagwedezeka (ndipo aliyense adzafa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
تَتۡبَعُهَا ٱلرَّادِفَةُ
Ndipo kudzatsatira kuyimba kwa lipenga lachiwiri (kumene kudzaukitsa akufa onse).
Tefsiret në gjuhën arabe:
قُلُوبٞ يَوۡمَئِذٖ وَاجِفَةٌ
Tsiku limenelo mitima idzanjenjemera ndi kuopa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَبۡصَٰرُهَا خَٰشِعَةٞ
Maso a eni mitimayo adzakhala ozyolika (chifukwa chamadandaulo);
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَقُولُونَ أَءِنَّا لَمَرۡدُودُونَ فِي ٱلۡحَافِرَةِ
(Osakhulupirira) akunena: “Kodi nzoona tidzabwezedwa pambuyo pa imfa monga tidalili kale?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَءِذَا كُنَّا عِظَٰمٗا نَّخِرَةٗ
“Pomwe ife titakhala mafupa ofumbwa (tingabwezedwe ndi kuukitsidwa mwa tsopano)?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالُواْ تِلۡكَ إِذٗا كَرَّةٌ خَاسِرَةٞ
Adanena (mokanira ndi mwachipongwe): “Choncho kubwerera kumeneko ngati kudzakhalepodi kudzakhala kotaika (ndi kopanda phindu kwa ife. Pomwe ife sindife oyenera kutaika).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِنَّمَا هِيَ زَجۡرَةٞ وَٰحِدَةٞ
(Musaganize kubwererako nchinthu chovuta). Ndithundithu Kiyamayo ndi nkuwo umodzi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِذَا هُم بِٱلسَّاهِرَةِ
Mwadzidzidzi (zolengedwa zonse) zidzangoona zili pa dziko latsopano (zili zamoyo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ
Kodi yakufika (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Mûsa?[380]
[380] Kuyambira Ayah iyi mpaka Ayah 26 Allah akumtonthoza mneneri Wake pomuuza nkhani ya Mneneri Musa momwe Farawo adamkanira, ndikuti asaganize kuti vutoli lampeza iye yekha koma kuti aneneri enanso akale lidawaonekeranso. Ndiponso m’ma Ayah amenewa muli chenjezo kwa akafiri kuti aope Allah kuti asawalange monga adamulangira Farawo ndi anthu ake amene adali kutsutsana ndi Allah.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِذۡ نَادَىٰهُ رَبُّهُۥ بِٱلۡوَادِ ٱلۡمُقَدَّسِ طُوًى
Pamene Mbuye wake adamuitana pa chigwa choyera (chotchedwa) Tuwaa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ٱذۡهَبۡ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
(Adamuuza kuti) pita kwa Farawo ndithu iye wapyola malire, (mkudzitukumula kwake ndikupondereza anthu).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَقُلۡ هَل لَّكَ إِلَىٰٓ أَن تَزَكَّىٰ
Choncho ukamuuze kuti: “Kodi ukufuna kudziyeretsa?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأَهۡدِيَكَ إِلَىٰ رَبِّكَ فَتَخۡشَىٰ
“Ndikuti ndikuongolere kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَرَىٰهُ ٱلۡأٓيَةَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
(Basi Mûsa) adamuonetsa (Farawo) chozizwitsa chachikulu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَكَذَّبَ وَعَصَىٰ
Koma (Farawo) adatsutsa (Mûsa pazimene adadza nazo zija) ndi kunyoza.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ أَدۡبَرَ يَسۡعَىٰ
Kenaka adabwerera uku akulimbika kutsutsana naye (Allah),
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَحَشَرَ فَنَادَىٰ
Adawasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu;
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَقَالَ أَنَا۠ رَبُّكُمُ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Nanena: “Ine ndine mbuye wanu wapamwambamwamba!”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَخَذَهُ ٱللَّهُ نَكَالَ ٱلۡأٓخِرَةِ وَٱلۡأُولَىٰٓ
Pamenepo Allah adamulanga chifukwa cha mawu ake omaliza ndi oyamba.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَعِبۡرَةٗ لِّمَن يَخۡشَىٰٓ
Ndithu pa zimenezi pali phunziro (lalikulu) kwa yemwe akuopa Allah.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ءَأَنتُمۡ أَشَدُّ خَلۡقًا أَمِ ٱلسَّمَآءُۚ بَنَىٰهَا
Kodi kulengedwa kwanu, (inu osakhulupirira kuti muuke) nkovuta kapena thambo limene adalimanga (posonkhanitsa mbali zake zosiyanasiyana ndikukhala chinthu chimodzi)?[381]
[381] Tanthauzo lake ndikuti: “Kodi chilengedwe chanu nchovuta kwambiri kuposa chilengedwe cha thambo pamene inu mukuganiza kuti Allah sangathe kukudzutsani pambuyo pa imfa?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
رَفَعَ سَمۡكَهَا فَسَوَّىٰهَا
Adatukula nsinkhu wake ndikulikonza bwino (popanda pena pong’ambika kapena posiyana ndi pena).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأَغۡطَشَ لَيۡلَهَا وَأَخۡرَجَ ضُحَىٰهَا
Ndipo amauvindikira usiku wake ndi mdima ndipo amatulutsa kuwala wake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ ذَٰلِكَ دَحَىٰهَآ
Ndipo pambuyo pazimenezo, nthaka adaiyala (kuti ikhale yoyenera kuikhala).
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَخۡرَجَ مِنۡهَا مَآءَهَا وَمَرۡعَىٰهَا
Adatulutsa m’menemo madzi ake (potulutsa akasupe) ndikumeretsa msipu wake;
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلۡجِبَالَ أَرۡسَىٰهَا
Ndipo mapiri adawakhazikitsa (ndikuwalimbika);
Tefsiret në gjuhën arabe:
مَتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Adachita zonsezi) chifukwa chokusangalatsani inu ndi ziweto zanu.[382]
[382] Mu Ayah iyi Allah akusonyeza kuti Iye ndi Mwini mphamvu zonse zochitira chinthu chilichonse chachikulu kuposa kuwaukitsa akufa; ndiponso akukumbutsa ufulu Wake waukulu womwe adatichitira potipatsa zinthu zonsezo kuti tithandizike nazo.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلطَّآمَّةُ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Choncho likadzafika tsoka lalikulu (tsiku la Qiyâma).
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَوۡمَ يَتَذَكَّرُ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا سَعَىٰ
Tsiku limenelo munthu adzakumbukira zimene adachita, (zabwino ndi zoipa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِمَن يَرَىٰ
Ndipo Moto waukali udzawonetsedwa kwa yense openya.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَمَّا مَن طَغَىٰ
Tsono amene adapyola malire (pochita machimo),
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَءَاثَرَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Ndikudzisankhira (yekha) moyo wa pa dziko lapansi,
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِنَّ ٱلۡجَحِيمَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Jahannam ndiwo malo ake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأَمَّا مَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ وَنَهَى ٱلنَّفۡسَ عَنِ ٱلۡهَوَىٰ
Tsono amene akuopa kuti adzaimilira pamaso pa Mbuye wake, nauletsa mtima wake ku zilakolako zoipa,
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِنَّ ٱلۡجَنَّةَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Munda wamtendere ndiwo adzakhale malo ake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلسَّاعَةِ أَيَّانَ مُرۡسَىٰهَا
Akukufunsa (iwe Mtumiki) (s.a.w) za nthawi (ya tsiku lachimaliziro kuti): “Idzakhala liti?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فِيمَ أَنتَ مِن ذِكۡرَىٰهَآ
Uli ndi mphamvu yanji iwe yofotokozera za tsikulo? (Iwe ulibe kuzindikira za nthawiyo kotero kuti ungaitchule kwa iwo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِلَىٰ رَبِّكَ مُنتَهَىٰهَآ
Kwa Mbuye wako ndiko kuli mathero ake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّمَآ أَنتَ مُنذِرُ مَن يَخۡشَىٰهَا
Iwe (ntchito yako) ndikuwachenjeza amene akuiopa; (osati kulengeza zanthawi yake).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَأَنَّهُمۡ يَوۡمَ يَرَوۡنَهَا لَمۡ يَلۡبَثُوٓاْ إِلَّا عَشِيَّةً أَوۡ ضُحَىٰهَا
Tsiku limene adzaiona adzakhala ngati sadakhale (pa dziko nthawi yayitali), koma ngati madzulo amodzi kapena masana ake (nthawi ya m’mawa).[383]
[383] Apa tanthauzo lake ndikuti adzaona masiku onse amene adakhala m’dziko ngati lidali ola limodzi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu En Naziat
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll