Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: An –Naazi’at (Abashikanuza)   Umurongo:

An –Naazi’at (Abashikanuza)

وَٱلنَّٰزِعَٰتِ غَرۡقٗا
Ndikulumbilira (angelo) amene amazula mwamphamvu (mizimu ya osakhulupirira).[379]
[379] (Ndime 1-5) M’Qur’an nthawi zambiri Allah amalumbilira zolengedwa Zake; zamoyo ndi zopanda moyo, zooneka ndi zosaoneka. Cholinga ndikutilimbikitsa kuti tikhale olingalira luso Lake pa chinthu chilichonse chimene wachilumbilira kuti tizindikire ulemelero Wake ndi mphamvu Zake zoposa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلنَّٰشِطَٰتِ نَشۡطٗا
Ndikulumbiliranso (angelo) amene amachotsa moleza (mizimu ya okhulupirira).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلسَّٰبِحَٰتِ سَبۡحٗا
Ndi omwe amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (ponka nayo ku malo ake oyembekezera).
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَٱلسَّٰبِقَٰتِ سَبۡقٗا
Ndi iwo amene akupikisana pokwaniritsa malamulo a Allah.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَٱلۡمُدَبِّرَٰتِ أَمۡرٗا
Ndi iwo (angelo) amene akulongosola malamulo (Ake). (Ndithudi inu anthu mudzauka kwa akufa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَوۡمَ تَرۡجُفُ ٱلرَّاجِفَةُ
Patsiku lomwe (lipenga loyamba lidzaimbidwa), dziko lapansi ndi mapiri ake zidzagwedezeka (ndipo aliyense adzafa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
تَتۡبَعُهَا ٱلرَّادِفَةُ
Ndipo kudzatsatira kuyimba kwa lipenga lachiwiri (kumene kudzaukitsa akufa onse).
Ibisobanuro by'icyarabu:
قُلُوبٞ يَوۡمَئِذٖ وَاجِفَةٌ
Tsiku limenelo mitima idzanjenjemera ndi kuopa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَبۡصَٰرُهَا خَٰشِعَةٞ
Maso a eni mitimayo adzakhala ozyolika (chifukwa chamadandaulo);
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَقُولُونَ أَءِنَّا لَمَرۡدُودُونَ فِي ٱلۡحَافِرَةِ
(Osakhulupirira) akunena: “Kodi nzoona tidzabwezedwa pambuyo pa imfa monga tidalili kale?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَءِذَا كُنَّا عِظَٰمٗا نَّخِرَةٗ
“Pomwe ife titakhala mafupa ofumbwa (tingabwezedwe ndi kuukitsidwa mwa tsopano)?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
قَالُواْ تِلۡكَ إِذٗا كَرَّةٌ خَاسِرَةٞ
Adanena (mokanira ndi mwachipongwe): “Choncho kubwerera kumeneko ngati kudzakhalepodi kudzakhala kotaika (ndi kopanda phindu kwa ife. Pomwe ife sindife oyenera kutaika).”
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَإِنَّمَا هِيَ زَجۡرَةٞ وَٰحِدَةٞ
(Musaganize kubwererako nchinthu chovuta). Ndithundithu Kiyamayo ndi nkuwo umodzi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَإِذَا هُم بِٱلسَّاهِرَةِ
Mwadzidzidzi (zolengedwa zonse) zidzangoona zili pa dziko latsopano (zili zamoyo).
Ibisobanuro by'icyarabu:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ
Kodi yakufika (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Mûsa?[380]
[380] Kuyambira Ayah iyi mpaka Ayah 26 Allah akumtonthoza mneneri Wake pomuuza nkhani ya Mneneri Musa momwe Farawo adamkanira, ndikuti asaganize kuti vutoli lampeza iye yekha koma kuti aneneri enanso akale lidawaonekeranso. Ndiponso m’ma Ayah amenewa muli chenjezo kwa akafiri kuti aope Allah kuti asawalange monga adamulangira Farawo ndi anthu ake amene adali kutsutsana ndi Allah.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِذۡ نَادَىٰهُ رَبُّهُۥ بِٱلۡوَادِ ٱلۡمُقَدَّسِ طُوًى
Pamene Mbuye wake adamuitana pa chigwa choyera (chotchedwa) Tuwaa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ٱذۡهَبۡ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
(Adamuuza kuti) pita kwa Farawo ndithu iye wapyola malire, (mkudzitukumula kwake ndikupondereza anthu).
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَقُلۡ هَل لَّكَ إِلَىٰٓ أَن تَزَكَّىٰ
Choncho ukamuuze kuti: “Kodi ukufuna kudziyeretsa?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَهۡدِيَكَ إِلَىٰ رَبِّكَ فَتَخۡشَىٰ
“Ndikuti ndikuongolere kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَأَرَىٰهُ ٱلۡأٓيَةَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
(Basi Mûsa) adamuonetsa (Farawo) chozizwitsa chachikulu.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَكَذَّبَ وَعَصَىٰ
Koma (Farawo) adatsutsa (Mûsa pazimene adadza nazo zija) ndi kunyoza.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ثُمَّ أَدۡبَرَ يَسۡعَىٰ
Kenaka adabwerera uku akulimbika kutsutsana naye (Allah),
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَحَشَرَ فَنَادَىٰ
Adawasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu;
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَقَالَ أَنَا۠ رَبُّكُمُ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Nanena: “Ine ndine mbuye wanu wapamwambamwamba!”
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَأَخَذَهُ ٱللَّهُ نَكَالَ ٱلۡأٓخِرَةِ وَٱلۡأُولَىٰٓ
Pamenepo Allah adamulanga chifukwa cha mawu ake omaliza ndi oyamba.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَعِبۡرَةٗ لِّمَن يَخۡشَىٰٓ
Ndithu pa zimenezi pali phunziro (lalikulu) kwa yemwe akuopa Allah.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ءَأَنتُمۡ أَشَدُّ خَلۡقًا أَمِ ٱلسَّمَآءُۚ بَنَىٰهَا
Kodi kulengedwa kwanu, (inu osakhulupirira kuti muuke) nkovuta kapena thambo limene adalimanga (posonkhanitsa mbali zake zosiyanasiyana ndikukhala chinthu chimodzi)?[381]
[381] Tanthauzo lake ndikuti: “Kodi chilengedwe chanu nchovuta kwambiri kuposa chilengedwe cha thambo pamene inu mukuganiza kuti Allah sangathe kukudzutsani pambuyo pa imfa?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
رَفَعَ سَمۡكَهَا فَسَوَّىٰهَا
Adatukula nsinkhu wake ndikulikonza bwino (popanda pena pong’ambika kapena posiyana ndi pena).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَغۡطَشَ لَيۡلَهَا وَأَخۡرَجَ ضُحَىٰهَا
Ndipo amauvindikira usiku wake ndi mdima ndipo amatulutsa kuwala wake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ ذَٰلِكَ دَحَىٰهَآ
Ndipo pambuyo pazimenezo, nthaka adaiyala (kuti ikhale yoyenera kuikhala).
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَخۡرَجَ مِنۡهَا مَآءَهَا وَمَرۡعَىٰهَا
Adatulutsa m’menemo madzi ake (potulutsa akasupe) ndikumeretsa msipu wake;
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلۡجِبَالَ أَرۡسَىٰهَا
Ndipo mapiri adawakhazikitsa (ndikuwalimbika);
Ibisobanuro by'icyarabu:
مَتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Adachita zonsezi) chifukwa chokusangalatsani inu ndi ziweto zanu.[382]
[382] Mu Ayah iyi Allah akusonyeza kuti Iye ndi Mwini mphamvu zonse zochitira chinthu chilichonse chachikulu kuposa kuwaukitsa akufa; ndiponso akukumbutsa ufulu Wake waukulu womwe adatichitira potipatsa zinthu zonsezo kuti tithandizike nazo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلطَّآمَّةُ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Choncho likadzafika tsoka lalikulu (tsiku la Qiyâma).
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَوۡمَ يَتَذَكَّرُ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا سَعَىٰ
Tsiku limenelo munthu adzakumbukira zimene adachita, (zabwino ndi zoipa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِمَن يَرَىٰ
Ndipo Moto waukali udzawonetsedwa kwa yense openya.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَأَمَّا مَن طَغَىٰ
Tsono amene adapyola malire (pochita machimo),
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَءَاثَرَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Ndikudzisankhira (yekha) moyo wa pa dziko lapansi,
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَإِنَّ ٱلۡجَحِيمَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Jahannam ndiwo malo ake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَمَّا مَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ وَنَهَى ٱلنَّفۡسَ عَنِ ٱلۡهَوَىٰ
Tsono amene akuopa kuti adzaimilira pamaso pa Mbuye wake, nauletsa mtima wake ku zilakolako zoipa,
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَإِنَّ ٱلۡجَنَّةَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Munda wamtendere ndiwo adzakhale malo ake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلسَّاعَةِ أَيَّانَ مُرۡسَىٰهَا
Akukufunsa (iwe Mtumiki) (s.a.w) za nthawi (ya tsiku lachimaliziro kuti): “Idzakhala liti?”
Ibisobanuro by'icyarabu:
فِيمَ أَنتَ مِن ذِكۡرَىٰهَآ
Uli ndi mphamvu yanji iwe yofotokozera za tsikulo? (Iwe ulibe kuzindikira za nthawiyo kotero kuti ungaitchule kwa iwo).
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِلَىٰ رَبِّكَ مُنتَهَىٰهَآ
Kwa Mbuye wako ndiko kuli mathero ake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّمَآ أَنتَ مُنذِرُ مَن يَخۡشَىٰهَا
Iwe (ntchito yako) ndikuwachenjeza amene akuiopa; (osati kulengeza zanthawi yake).
Ibisobanuro by'icyarabu:
كَأَنَّهُمۡ يَوۡمَ يَرَوۡنَهَا لَمۡ يَلۡبَثُوٓاْ إِلَّا عَشِيَّةً أَوۡ ضُحَىٰهَا
Tsiku limene adzaiona adzakhala ngati sadakhale (pa dziko nthawi yayitali), koma ngati madzulo amodzi kapena masana ake (nthawi ya m’mawa).[383]
[383] Apa tanthauzo lake ndikuti adzaona masiku onse amene adakhala m’dziko ngati lidali ola limodzi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: An –Naazi’at (Abashikanuza)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga