Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Abese   Ajeti:

Suretu Abese

عَبَسَ وَتَوَلَّىٰٓ
Adachita tsinya (Mneneri) ndi kuyang’ana kumbali.[384]
[384] Tsiku lina Mneneri (s.a.w) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza. Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum. Sadadziwe kuti Mneneri (s.a.w) ali wotanganidwa. Adamukuwira: “E Iwe Mneneri wa Allah! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Allah.” Ndipo ankangomubwerezera-bwerezera mawu amenewa. Mneneri (s.a.w) pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, adamchitira tsinya wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; sadamumvere. Basi pamenepa Allah akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَن جَآءَهُ ٱلۡأَعۡمَىٰ
Chifukwa chakuti adamdzera wakhungu (kudzamfunsa zokhudzana ndi chipembedzo chake pamene iye adali kuyankhula ndi atsogoleri Achiquraishi).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّهُۥ يَزَّكَّىٰٓ
Nanga chingakudziwitse nchiyani kuti mwina iye angadziyeretse (pomvera ulaliki wako watsopano)?
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَوۡ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ ٱلذِّكۡرَىٰٓ
Kapena akumbukira, ndipo kukumbukirako kumthandiza?
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَمَّا مَنِ ٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma amene wadzikwaniritsa (ndi chuma chake ndi mphamvu zake),
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَنتَ لَهُۥ تَصَدَّىٰ
Ameneyo ndi yemwe ukumchitira chidwi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا عَلَيۡكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ
Palibe chilichonse pa iwe ngati sadziyeretsa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأَمَّا مَن جَآءَكَ يَسۡعَىٰ
Koma amene wakudzera uku akuthamanga (kufuna maphunziro ndi chiongoko),
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَهُوَ يَخۡشَىٰ
Ndipo iye akuopa (Allah mu mtima mwake).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَنتَ عَنۡهُ تَلَهَّىٰ
Za iye, iwe sukusamala, (ukuyikira chidwi kwa wina).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآ إِنَّهَا تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithudi iyi (Qur’an) ndi chikumbutso (chenjezo).[385]
[385] (Ndime 11-16) Apa Allah akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur’an ndi ulaliki chabe, amene afuna kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake. Ndiponso adamufotokozera kuti Qur’an idachokera m’mabuku olemekezeka; idachokera ku “Lauhil-Mahfudh” mabuku omwe ali m’manja mwa Angelo olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Basi, amene wafuna alangizika (ndi Qur’an, ndipo amene sakufuna msiye).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فِي صُحُفٖ مُّكَرَّمَةٖ
(Malangizowa akuchokera) mmakalata olemekezeka (kwa Allah);
Tefsiret në gjuhën arabe:
مَّرۡفُوعَةٖ مُّطَهَّرَةِۭ
Apamwamba ndiponso oyeretsedwa (kumbiri iliyonse yopunguka);
Tefsiret në gjuhën arabe:
بِأَيۡدِي سَفَرَةٖ
Omwe ali m’manja mwa Alembi (Angelo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كِرَامِۭ بَرَرَةٖ
Olemekezeka, omvera.
Tefsiret në gjuhën arabe:
قُتِلَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَآ أَكۡفَرَهُۥ
Waonongeka (watembeleredwa) munthu. Nkotani kusayamika kwake kotereku.
Tefsiret në gjuhën arabe:
مِنۡ أَيِّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥ
Kuchokera mchinthu chanji chimene iye adamulenga.
Tefsiret në gjuhën arabe:
مِن نُّطۡفَةٍ خَلَقَهُۥ فَقَدَّرَهُۥ
Kuchokera ku dontho lamadzi (onyozeka) adamulenga, namkonzeratu mkalengedwe kosiyanasiyana.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ ٱلسَّبِيلَ يَسَّرَهُۥ
Kenako adamfewetsera njira (yotulukira m’mimba mwa mai ake).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ أَمَاتَهُۥ فَأَقۡبَرَهُۥ
Ndipo amamchititsa kuti amwalire namukumbula m’manda,
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ إِذَا شَآءَ أَنشَرَهُۥ
Kenako akadzafuna adzamuukitsa (pambuyo pa imfa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّا لَمَّا يَقۡضِ مَآ أَمَرَهُۥ
Ayi ndithu (munthu) sanakwaniritsebe zimene adamulamula Mbuye wake (Allah chingakhale wakhala nthawi yaitali pa dziko lapansi).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ إِلَىٰ طَعَامِهِۦٓ
Alingalire munthu (mmene chilili) chakudya chake;[386]
[386] Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang’ane chakudya chimene akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Allah.
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَنَّا صَبَبۡنَا ٱلۡمَآءَ صَبّٗا
Ndithu Ife timagwetsa mvula yambiri (kuchokera ku mitambo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ شَقَقۡنَا ٱلۡأَرۡضَ شَقّٗا
Kenako timaing’amba nthaka kuti mmera utuluke;
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا حَبّٗا
Ndipo timameretsa m’menemo njere (ya chakudya cha anthu ndi zina zimene amasunga mnkhokwe),
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَعِنَبٗا وَقَضۡبٗا
Ndi mphesa ndi msipu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَزَيۡتُونٗا وَنَخۡلٗا
Ndi mzitona (wabwino) ndi (zipatso za) kanjedza,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَحَدَآئِقَ غُلۡبٗا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَفَٰكِهَةٗ وَأَبّٗا
Ndi zipatso (zodyedwa ndi anthu) ndi msipu (wodyedwa ndi nyama);
Tefsiret në gjuhën arabe:
مَّتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Tazimeretsa zimenezo kuti) zikondweretse inu ndi ziweto zanu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلصَّآخَّةُ
Choncho likadzafika lipenga logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa makosi).
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَوۡمَ يَفِرُّ ٱلۡمَرۡءُ مِنۡ أَخِيهِ
Patsikuli munthu adzathawa m’bale wake,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَأُمِّهِۦ وَأَبِيهِ
Mayi wake ndi bambo wake,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَبَنِيهِ
Mkazi wake ndi ana ake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
لِكُلِّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ يَوۡمَئِذٖ شَأۡنٞ يُغۡنِيهِ
Munthu aliyense mwa iwo, tsiku limenelo adzakhala ndi zakezake zotangwanika nazo. (Sadzalabadira za anzake).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ مُّسۡفِرَةٞ
Tsiku limenelo nkhope zina zidzakhala zowala;[387]
[387] (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri: amene adakhulupilira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma Ayah 40 ndi 42.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ضَاحِكَةٞ مُّسۡتَبۡشِرَةٞ
Zosekelera ndi zachimwemwe (chifukwa cha nkhani yabwino ya ku Munda wamtendere.)
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ عَلَيۡهَا غَبَرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zokutidwa ndi fumbi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
تَرۡهَقُهَا قَتَرَةٌ
Mdima udzazikuta.
Tefsiret në gjuhën arabe:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَفَرَةُ ٱلۡفَجَرَةُ
Iwo ndi anthu osakhulupirira oipa (olakwira Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Abese
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll