แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: ‘Abasa   อายะฮ์:

‘Abasa

عَبَسَ وَتَوَلَّىٰٓ
Adachita tsinya (Mneneri) ndi kuyang’ana kumbali.[384]
[384] Tsiku lina Mneneri (s.a.w) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza. Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum. Sadadziwe kuti Mneneri (s.a.w) ali wotanganidwa. Adamukuwira: “E Iwe Mneneri wa Allah! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Allah.” Ndipo ankangomubwerezera-bwerezera mawu amenewa. Mneneri (s.a.w) pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, adamchitira tsinya wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; sadamumvere. Basi pamenepa Allah akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَن جَآءَهُ ٱلۡأَعۡمَىٰ
Chifukwa chakuti adamdzera wakhungu (kudzamfunsa zokhudzana ndi chipembedzo chake pamene iye adali kuyankhula ndi atsogoleri Achiquraishi).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّهُۥ يَزَّكَّىٰٓ
Nanga chingakudziwitse nchiyani kuti mwina iye angadziyeretse (pomvera ulaliki wako watsopano)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَوۡ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ ٱلذِّكۡرَىٰٓ
Kapena akumbukira, ndipo kukumbukirako kumthandiza?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَمَّا مَنِ ٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma amene wadzikwaniritsa (ndi chuma chake ndi mphamvu zake),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَأَنتَ لَهُۥ تَصَدَّىٰ
Ameneyo ndi yemwe ukumchitira chidwi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا عَلَيۡكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ
Palibe chilichonse pa iwe ngati sadziyeretsa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَمَّا مَن جَآءَكَ يَسۡعَىٰ
Koma amene wakudzera uku akuthamanga (kufuna maphunziro ndi chiongoko),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَهُوَ يَخۡشَىٰ
Ndipo iye akuopa (Allah mu mtima mwake).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَأَنتَ عَنۡهُ تَلَهَّىٰ
Za iye, iwe sukusamala, (ukuyikira chidwi kwa wina).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّآ إِنَّهَا تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithudi iyi (Qur’an) ndi chikumbutso (chenjezo).[385]
[385] (Ndime 11-16) Apa Allah akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur’an ndi ulaliki chabe, amene afuna kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake. Ndiponso adamufotokozera kuti Qur’an idachokera m’mabuku olemekezeka; idachokera ku “Lauhil-Mahfudh” mabuku omwe ali m’manja mwa Angelo olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Basi, amene wafuna alangizika (ndi Qur’an, ndipo amene sakufuna msiye).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فِي صُحُفٖ مُّكَرَّمَةٖ
(Malangizowa akuchokera) mmakalata olemekezeka (kwa Allah);
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَّرۡفُوعَةٖ مُّطَهَّرَةِۭ
Apamwamba ndiponso oyeretsedwa (kumbiri iliyonse yopunguka);
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
بِأَيۡدِي سَفَرَةٖ
Omwe ali m’manja mwa Alembi (Angelo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كِرَامِۭ بَرَرَةٖ
Olemekezeka, omvera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قُتِلَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَآ أَكۡفَرَهُۥ
Waonongeka (watembeleredwa) munthu. Nkotani kusayamika kwake kotereku.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مِنۡ أَيِّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥ
Kuchokera mchinthu chanji chimene iye adamulenga.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مِن نُّطۡفَةٍ خَلَقَهُۥ فَقَدَّرَهُۥ
Kuchokera ku dontho lamadzi (onyozeka) adamulenga, namkonzeratu mkalengedwe kosiyanasiyana.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ ٱلسَّبِيلَ يَسَّرَهُۥ
Kenako adamfewetsera njira (yotulukira m’mimba mwa mai ake).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ أَمَاتَهُۥ فَأَقۡبَرَهُۥ
Ndipo amamchititsa kuti amwalire namukumbula m’manda,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ إِذَا شَآءَ أَنشَرَهُۥ
Kenako akadzafuna adzamuukitsa (pambuyo pa imfa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّا لَمَّا يَقۡضِ مَآ أَمَرَهُۥ
Ayi ndithu (munthu) sanakwaniritsebe zimene adamulamula Mbuye wake (Allah chingakhale wakhala nthawi yaitali pa dziko lapansi).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ إِلَىٰ طَعَامِهِۦٓ
Alingalire munthu (mmene chilili) chakudya chake;[386]
[386] Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang’ane chakudya chimene akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Allah.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَنَّا صَبَبۡنَا ٱلۡمَآءَ صَبّٗا
Ndithu Ife timagwetsa mvula yambiri (kuchokera ku mitambo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ شَقَقۡنَا ٱلۡأَرۡضَ شَقّٗا
Kenako timaing’amba nthaka kuti mmera utuluke;
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا حَبّٗا
Ndipo timameretsa m’menemo njere (ya chakudya cha anthu ndi zina zimene amasunga mnkhokwe),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَعِنَبٗا وَقَضۡبٗا
Ndi mphesa ndi msipu.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَزَيۡتُونٗا وَنَخۡلٗا
Ndi mzitona (wabwino) ndi (zipatso za) kanjedza,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَحَدَآئِقَ غُلۡبٗا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَفَٰكِهَةٗ وَأَبّٗا
Ndi zipatso (zodyedwa ndi anthu) ndi msipu (wodyedwa ndi nyama);
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَّتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Tazimeretsa zimenezo kuti) zikondweretse inu ndi ziweto zanu.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلصَّآخَّةُ
Choncho likadzafika lipenga logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa makosi).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
يَوۡمَ يَفِرُّ ٱلۡمَرۡءُ مِنۡ أَخِيهِ
Patsikuli munthu adzathawa m’bale wake,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأُمِّهِۦ وَأَبِيهِ
Mayi wake ndi bambo wake,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَبَنِيهِ
Mkazi wake ndi ana ake.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لِكُلِّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ يَوۡمَئِذٖ شَأۡنٞ يُغۡنِيهِ
Munthu aliyense mwa iwo, tsiku limenelo adzakhala ndi zakezake zotangwanika nazo. (Sadzalabadira za anzake).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ مُّسۡفِرَةٞ
Tsiku limenelo nkhope zina zidzakhala zowala;[387]
[387] (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri: amene adakhulupilira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma Ayah 40 ndi 42.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ضَاحِكَةٞ مُّسۡتَبۡشِرَةٞ
Zosekelera ndi zachimwemwe (chifukwa cha nkhani yabwino ya ku Munda wamtendere.)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ عَلَيۡهَا غَبَرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zokutidwa ndi fumbi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
تَرۡهَقُهَا قَتَرَةٌ
Mdima udzazikuta.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَفَرَةُ ٱلۡفَجَرَةُ
Iwo ndi anthu osakhulupirira oipa (olakwira Allah).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: ‘Abasa
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด