ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ * - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ


ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅಬಸ್   ಶ್ಲೋಕ:

ಸೂರ ಅಬಸ್

عَبَسَ وَتَوَلَّىٰٓ
Adachita tsinya (Mneneri) ndi kuyang’ana kumbali.[384]
[384] Tsiku lina Mneneri (s.a.w) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza. Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum. Sadadziwe kuti Mneneri (s.a.w) ali wotanganidwa. Adamukuwira: “E Iwe Mneneri wa Allah! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Allah.” Ndipo ankangomubwerezera-bwerezera mawu amenewa. Mneneri (s.a.w) pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, adamchitira tsinya wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; sadamumvere. Basi pamenepa Allah akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
أَن جَآءَهُ ٱلۡأَعۡمَىٰ
Chifukwa chakuti adamdzera wakhungu (kudzamfunsa zokhudzana ndi chipembedzo chake pamene iye adali kuyankhula ndi atsogoleri Achiquraishi).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّهُۥ يَزَّكَّىٰٓ
Nanga chingakudziwitse nchiyani kuti mwina iye angadziyeretse (pomvera ulaliki wako watsopano)?
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
أَوۡ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ ٱلذِّكۡرَىٰٓ
Kapena akumbukira, ndipo kukumbukirako kumthandiza?
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
أَمَّا مَنِ ٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma amene wadzikwaniritsa (ndi chuma chake ndi mphamvu zake),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَأَنتَ لَهُۥ تَصَدَّىٰ
Ameneyo ndi yemwe ukumchitira chidwi.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا عَلَيۡكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ
Palibe chilichonse pa iwe ngati sadziyeretsa.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَأَمَّا مَن جَآءَكَ يَسۡعَىٰ
Koma amene wakudzera uku akuthamanga (kufuna maphunziro ndi chiongoko),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَهُوَ يَخۡشَىٰ
Ndipo iye akuopa (Allah mu mtima mwake).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَأَنتَ عَنۡهُ تَلَهَّىٰ
Za iye, iwe sukusamala, (ukuyikira chidwi kwa wina).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
كَلَّآ إِنَّهَا تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithudi iyi (Qur’an) ndi chikumbutso (chenjezo).[385]
[385] (Ndime 11-16) Apa Allah akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur’an ndi ulaliki chabe, amene afuna kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake. Ndiponso adamufotokozera kuti Qur’an idachokera m’mabuku olemekezeka; idachokera ku “Lauhil-Mahfudh” mabuku omwe ali m’manja mwa Angelo olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Basi, amene wafuna alangizika (ndi Qur’an, ndipo amene sakufuna msiye).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فِي صُحُفٖ مُّكَرَّمَةٖ
(Malangizowa akuchokera) mmakalata olemekezeka (kwa Allah);
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
مَّرۡفُوعَةٖ مُّطَهَّرَةِۭ
Apamwamba ndiponso oyeretsedwa (kumbiri iliyonse yopunguka);
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
بِأَيۡدِي سَفَرَةٖ
Omwe ali m’manja mwa Alembi (Angelo).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
كِرَامِۭ بَرَرَةٖ
Olemekezeka, omvera.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
قُتِلَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَآ أَكۡفَرَهُۥ
Waonongeka (watembeleredwa) munthu. Nkotani kusayamika kwake kotereku.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
مِنۡ أَيِّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥ
Kuchokera mchinthu chanji chimene iye adamulenga.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
مِن نُّطۡفَةٍ خَلَقَهُۥ فَقَدَّرَهُۥ
Kuchokera ku dontho lamadzi (onyozeka) adamulenga, namkonzeratu mkalengedwe kosiyanasiyana.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ثُمَّ ٱلسَّبِيلَ يَسَّرَهُۥ
Kenako adamfewetsera njira (yotulukira m’mimba mwa mai ake).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ثُمَّ أَمَاتَهُۥ فَأَقۡبَرَهُۥ
Ndipo amamchititsa kuti amwalire namukumbula m’manda,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ثُمَّ إِذَا شَآءَ أَنشَرَهُۥ
Kenako akadzafuna adzamuukitsa (pambuyo pa imfa).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
كَلَّا لَمَّا يَقۡضِ مَآ أَمَرَهُۥ
Ayi ndithu (munthu) sanakwaniritsebe zimene adamulamula Mbuye wake (Allah chingakhale wakhala nthawi yaitali pa dziko lapansi).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ إِلَىٰ طَعَامِهِۦٓ
Alingalire munthu (mmene chilili) chakudya chake;[386]
[386] Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang’ane chakudya chimene akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Allah.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
أَنَّا صَبَبۡنَا ٱلۡمَآءَ صَبّٗا
Ndithu Ife timagwetsa mvula yambiri (kuchokera ku mitambo).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ثُمَّ شَقَقۡنَا ٱلۡأَرۡضَ شَقّٗا
Kenako timaing’amba nthaka kuti mmera utuluke;
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا حَبّٗا
Ndipo timameretsa m’menemo njere (ya chakudya cha anthu ndi zina zimene amasunga mnkhokwe),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَعِنَبٗا وَقَضۡبٗا
Ndi mphesa ndi msipu.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَزَيۡتُونٗا وَنَخۡلٗا
Ndi mzitona (wabwino) ndi (zipatso za) kanjedza,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَحَدَآئِقَ غُلۡبٗا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَفَٰكِهَةٗ وَأَبّٗا
Ndi zipatso (zodyedwa ndi anthu) ndi msipu (wodyedwa ndi nyama);
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
مَّتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Tazimeretsa zimenezo kuti) zikondweretse inu ndi ziweto zanu.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلصَّآخَّةُ
Choncho likadzafika lipenga logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa makosi).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
يَوۡمَ يَفِرُّ ٱلۡمَرۡءُ مِنۡ أَخِيهِ
Patsikuli munthu adzathawa m’bale wake,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَأُمِّهِۦ وَأَبِيهِ
Mayi wake ndi bambo wake,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَبَنِيهِ
Mkazi wake ndi ana ake.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
لِكُلِّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ يَوۡمَئِذٖ شَأۡنٞ يُغۡنِيهِ
Munthu aliyense mwa iwo, tsiku limenelo adzakhala ndi zakezake zotangwanika nazo. (Sadzalabadira za anzake).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ مُّسۡفِرَةٞ
Tsiku limenelo nkhope zina zidzakhala zowala;[387]
[387] (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri: amene adakhulupilira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma Ayah 40 ndi 42.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ضَاحِكَةٞ مُّسۡتَبۡشِرَةٞ
Zosekelera ndi zachimwemwe (chifukwa cha nkhani yabwino ya ku Munda wamtendere.)
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ عَلَيۡهَا غَبَرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zokutidwa ndi fumbi.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
تَرۡهَقُهَا قَتَرَةٌ
Mdima udzazikuta.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَفَرَةُ ٱلۡفَجَرَةُ
Iwo ndi anthu osakhulupirira oipa (olakwira Allah).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
 
ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅಬಸ್
ಅಧ್ಯಾಯಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ ಪುಟ ಸಂಖ್ಯೆ
 
ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ

ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಚೇವಾ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಖಾಲಿದ್ ಇಬ್ರಾಹೀಂ ಬೀತಾಲಾ - ಮುದ್ರಣ: 2020

ಮುಚ್ಚಿ