ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ * - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ


ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅತ್ತಕ್ವೀರ್   ಶ್ಲೋಕ:

ಸೂರ ಅತ್ತಕ್ವೀರ್

إِذَا ٱلشَّمۡسُ كُوِّرَتۡ
Pamene dzuwa lidzakulungidwe (ndikuchotsedwa kuwala kwake),[388]
[388] Surah zambiri zimene zidavumbulutsidwa ku Makka zimanena zododometsa za tsiku lachimaliziro.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلنُّجُومُ ٱنكَدَرَتۡ
Ndi pamene nyenyezi zidzathothoke (ndi kuchoka dangalira lake),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ سُيِّرَتۡ
Ndi pamene mapiri adzayendetsedwe (kuchoka mmalo mwake),[389]
[389] Tsiku limenelo mapiri adzakhala osalimba ngati thonje limene likungouluka ndi mphepo.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡعِشَارُ عُطِّلَتۡ
Ndi pamene ngamira zabere lamiyezi khumi zidzasiidwe (zopanda oziyang’anira),[390]
[390] Ngamira za bere ndi chuma cha mtengo wapatali kwa Aarabu. Akuuzidwa apa kuti tsiku limenelo adzazisiya osazilabadira konse.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡوُحُوشُ حُشِرَتۡ
Ndi pamene nyama za mtchire zidzasonkhanitsidwe pamodzi (kuchokera mmalo osiyanasiyana chifukwa chakuopsa kwakukulu kwa tsikulo),[391]
[391] Mwa zina zododometsa pa tsiku limenelo ndi nyama za mtchire kusonkhanitsidwa pamodzi popanda kumenyana kapena kudyana.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡبِحَارُ سُجِّرَتۡ
Ndi pamene nyanja zidzayatsidwe moto,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلنُّفُوسُ زُوِّجَتۡ
Ndi pamene mizimu idzalumikizidwe (ndi matupi ake),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡمَوۡءُۥدَةُ سُئِلَتۡ
Ndi pamene mwana wamkazi yemwe adaikidwa m’manda wamoyo adzafunsidwe,[392]
[392] (Ndime 8-9) Ma Ayah awiriwa akufotokoza momwe Aarabu adalili Usilamu usadabwere. Munthu ankati akapatsidwa mphatso ya mwana wa mkazi adali kukhumudwa ndi kudandaula kwambiri. Ankanena kuti asungwana ngopanda phindu ndipo kuti kudali kuononga zinthu pakumulera, kumudyetsa, ndi kumuveka. Ndipo akadzakhala wachiwerewere adzakhala manyazi aakulu kwa makolo ake. Pamene chidadza chisilamu chidathetsa mkhalidwewu. Ndipo apa Allah akutisonyeza kuti patsiku limenelo, la chiweruziro, mwana uja adaikidwa wa moyo, adzafunsidwa kuti adaphedwa ndi tchimo lanji. Iye adzayankha kuti sadachite tchimo lililonse koma adaphedwa mopanda chilungamo.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
بِأَيِّ ذَنۢبٖ قُتِلَتۡ
Ndi tchimo lanji adaphedwera?
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلصُّحُفُ نُشِرَتۡ
Ndi pamene makalata (momwe mudalembedwa zochita za aliyense) adzatambasulidwe ndi kugawidwa (kuti awerengedwe),[393]
[393] Awa ndi makalata achiwerengero momwe mwalembedwa zabwino za munthu ndi zoipa zake. Tsiku limenelo munthu aliyense adzapatsidwa yake kalata kuti aone iye mwini zoipa ndi zabwino zake.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ كُشِطَتۡ
Ndi pamene thambo lidzayalulidwe (kuchoka mmalo mwake),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡجَحِيمُ سُعِّرَتۡ
Ndi pamene Jahena idzasonkhezeredwe mwamphamvu,[394]
[394] (Ndime12-13) Tsiku limenelo Jannah idzayandikitsidwa kwa ochita zabwino ndiponso Moto udzayandikitsidwa kwa ochita zoipa kuti aone kumalo kwake.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَإِذَا ٱلۡجَنَّةُ أُزۡلِفَتۡ
Ndi pamene Jannah idzayandikitsidwe,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
عَلِمَتۡ نَفۡسٞ مَّآ أَحۡضَرَتۡ
(Zikadzachitika zimenezi) mzimu uliwonse udzadziwa zimene wabweretsa (zabwino ndi zoipa).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِٱلۡخُنَّسِ
Ndikulumbilira nyenyezi zimene zimabwerera masana ndi kutulukanso usiku.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ٱلۡجَوَارِ ٱلۡكُنَّسِ
Zomwe zimayenda kenako nkubisika,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا عَسۡعَسَ
Ndi usiku pamene ukulowa.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَا تَنَفَّسَ
Ndi m’mawa kukamacha;
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلُ رَسُولٖ كَرِيمٖ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi liwu la mthenga wa Allah (Jibril) wolemekezeka,[395]
[395] (Ndime 19-20) Mthenga wolemekezeka womveredwa uko kumwamba ndi Jibril (Gabriele) yemwe ndi wamkulu wa angelo onse. Iye ndiyemwe adali kubweretsa Qur’an mwa lamulo la Allah kwa Mneneri Wake Muhammad (s.a.w). Ndipo ulemelero wa Qur’an ndi ulemelero wa Mneneri (s.a.w) chifukwa choti munthu wolemekezeka amamutumizira mthenga wolemekezekanso. Ndipo uthenga wabwino umapatsidwa kwa Mneneri wabwino woposa onse.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
ذِي قُوَّةٍ عِندَ ذِي ٱلۡعَرۡشِ مَكِينٖ
Mwini mphamvu ndi mwini ulemelero kwa Mwini Arsh (Mpando wa chifumu),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
مُّطَاعٖ ثَمَّ أَمِينٖ
Womveredwa kumeneko ndiponso wokhulupirika (pachivumbulutso).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا صَاحِبُكُم بِمَجۡنُونٖ
Ndipo m’bale wanuyu siwamisala ayi.[396]
[396] (Ndime 22-25) Anthu okanira pamene adasowa chonena kwa mneneri (s.a.w) adali kunena nkhani zabodza kuti Mtumiki (s.a.w) wapenga ndikuti zomwe akuyankhula sadapatsidwe ndi Jibril.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَلَقَدۡ رَءَاهُ بِٱلۡأُفُقِ ٱلۡمُبِينِ
Ndithu ndikulumbira kuti (iye Mtumiki) (s.a.w) adamuona (Jibril) mchizimezime (chakum’mawa) chooneka bwino.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا هُوَ عَلَى ٱلۡغَيۡبِ بِضَنِينٖ
Ndipo sali iye (Mtumiki) waumbombo ndi chivumbulutso (koma amafikitsa zonse ndi kuziphunzitsa kwa anthu).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا هُوَ بِقَوۡلِ شَيۡطَٰنٖ رَّجِيمٖ
(Chivumbulutso chomwe chavumbulutsidwachi kwa iye) si mawu a satana wothamangitsidwa (mchifundo cha Allah);
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَأَيۡنَ تَذۡهَبُونَ
Nanga mukupita kuti?
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
إِنۡ هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
(Qur’ani) iyi sichina koma ndi chikumbutso cha zolengedwa zonse.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَسۡتَقِيمَ
Kwa yemwe mwa inu akufuna kuyenda mu njira yoongoka.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَا تَشَآءُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُ رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo simungafune chinthu mwa inu nokha pokhapokha atafuna Allah Mbuye wa zolengedwa zonse.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
 
ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅತ್ತಕ್ವೀರ್
ಅಧ್ಯಾಯಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ ಪುಟ ಸಂಖ್ಯೆ
 
ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ

ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಚೇವಾ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಖಾಲಿದ್ ಇಬ್ರಾಹೀಂ ಬೀತಾಲಾ - ಮುದ್ರಣ: 2020

ಮುಚ್ಚಿ