Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Simoore: Simoore yimooɓe   Aaya:

Simoore yimooɓe

طسٓمٓ
Tâ-Sîn-Mîm.
Faccirooji aarabeeji:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Izi ndi Ayah (ndime) za buku (la Qur’an) lofotokoza chilichonse (chofunika m’chipembedzo).
Faccirooji aarabeeji:
لَعَلَّكَ بَٰخِعٞ نَّفۡسَكَ أَلَّا يَكُونُواْ مُؤۡمِنِينَ
Mwina iwe (Mtumiki Muhammad {s.a.w}) udziononga wekha (ndi madandaulo) chifukwa chakuti (iwo) sadakhale okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
إِن نَّشَأۡ نُنَزِّلۡ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ ءَايَةٗ فَظَلَّتۡ أَعۡنَٰقُهُمۡ لَهَا خَٰضِعِينَ
Tikadafuna, tikadawatsitsira chizizwa kuchokera kumwamba; kotero kuti makosi awo akadadzichepetsa ndi chizizwacho, (sakadatha kucheukira kwina koma sitifuna kukakamiza anthu kuti akhale Asilamu).[295]
[295] Mtumiki Muhammad (s.a.w) adali kuwawidwa mtima kwambiri poona kuti anthu sakuvomereza uthenga wachoonadi umene iye adadza nawo, ndipo adali kuwamvera chisoni kwambiri. Choncho Allah adamtonthoza pomuuza kuti: “Usadziphe wekha chifukwa chokhala ndi maganizo owamvera chisoni.” Allah akadafuna kuwaongola mowakakamiza akadatha kutero; koma sadafune.
Faccirooji aarabeeji:
وَمَا يَأۡتِيهِم مِّن ذِكۡرٖ مِّنَ ٱلرَّحۡمَٰنِ مُحۡدَثٍ إِلَّا كَانُواْ عَنۡهُ مُعۡرِضِينَ
Ndipo palibe pamene chikuwadzera chivumbulutso chatsopano chochokera kwa (Allah) Wachifundo chambiri koma amazipatula ku icho (chivumbulutso).
Faccirooji aarabeeji:
فَقَدۡ كَذَّبُواْ فَسَيَأۡتِيهِمۡ أَنۢبَٰٓؤُاْ مَا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndithu atsutsa; choncho posachedwapa ziwadzera nkhani zomwe adali kuzichitira chipongwe.
Faccirooji aarabeeji:
أَوَلَمۡ يَرَوۡاْ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَمۡ أَنۢبَتۡنَا فِيهَا مِن كُلِّ زَوۡجٖ كَرِيمٍ
Kodi sadaone nthaka? Ndimmera ungati taumeretsa m’menemo kuchokera mu mtundu ulionse, wokongola?
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezo muli zizindikiro (zosonyeza mphamvu za Allah). Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِذۡ نَادَىٰ رَبُّكَ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱئۡتِ ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo (akumbutse) pamene Mbuye wako adaitana (m’neneri) Mûsa; adamuuza: “Pita kwa anthu ochita zoipa.”
Faccirooji aarabeeji:
قَوۡمَ فِرۡعَوۡنَۚ أَلَا يَتَّقُونَ
Anthu a Farawo; (auze): “Kodi sawopa (Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبِّ إِنِّيٓ أَخَافُ أَن يُكَذِّبُونِ
(Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ine ndikuopa kuti anganditsutse.
Faccirooji aarabeeji:
وَيَضِيقُ صَدۡرِي وَلَا يَنطَلِقُ لِسَانِي فَأَرۡسِلۡ إِلَىٰ هَٰرُونَ
Ndipo chingabanike chifuwa changa (ndi maganizo, chifukwa chakunditsutsa kwawo); ndiponso lirime langa siliyankhula momveka bwino. Choncho tumizaninso uthengawu kwa Harun (kuti tikhale awiri ndipo azikandithangata pantchito yangayi).
Faccirooji aarabeeji:
وَلَهُمۡ عَلَيَّ ذَنۢبٞ فَأَخَافُ أَن يَقۡتُلُونِ
Ndipo iwowo ndili nawo mlandu ndipo ndikuopa kuti angandiphe (pobwezera chimene ndidawalakwira powaphera munthu wawo).
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ كَلَّاۖ فَٱذۡهَبَا بِـَٔايَٰتِنَآۖ إِنَّا مَعَكُم مُّسۡتَمِعُونَ
(Allah) adati: “Iyayi! Pitani pamodzi ndi zozizwa Zathu; ndithu Ife tikakhala nanu limodzi (pokuthangatani) uku tikumvetsera (zimene azikanena).”
Faccirooji aarabeeji:
فَأۡتِيَا فِرۡعَوۡنَ فَقُولَآ إِنَّا رَسُولُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Choncho mpitireni Farawo, ndipo kamuuzeni kuti: “Ife ndi atumiki a Mbuye wa zolengedwa zonse.”
Faccirooji aarabeeji:
أَنۡ أَرۡسِلۡ مَعَنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“(Tatumidwa) kuti uwapereke kwa ife ana a Israyeli (kuti tinke nawo ku Sham).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ أَلَمۡ نُرَبِّكَ فِينَا وَلِيدٗا وَلَبِثۡتَ فِينَا مِنۡ عُمُرِكَ سِنِينَ
(Farawo) adati (kwa Mûsa): “Kodi sitidakulere kwathu uli mwana, ndi kukhala nafe pa moyo wako zaka zambiri?”
Faccirooji aarabeeji:
وَفَعَلۡتَ فَعۡلَتَكَ ٱلَّتِي فَعَلۡتَ وَأَنتَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
“Ndipo udachita chochita chako chimene udachichita, ndipo iwe ndiwe mmodzi wa osathokoza!”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ فَعَلۡتُهَآ إِذٗا وَأَنَا۠ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
(Mûsa) adati: “Ndidachita zimenezo pomwe ine ndidali mmodzi wa osazindikira zinthu.”
Faccirooji aarabeeji:
فَفَرَرۡتُ مِنكُمۡ لَمَّا خِفۡتُكُمۡ فَوَهَبَ لِي رَبِّي حُكۡمٗا وَجَعَلَنِي مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
“Choncho ndidakuthawani pomwe ndidakuopani; tsono Mbuye wanga wandipatsa nzeru zoweruzira (zinthu), ndi kundisankha kukhala mmodzi wa atumiki.”
Faccirooji aarabeeji:
وَتِلۡكَ نِعۡمَةٞ تَمُنُّهَا عَلَيَّ أَنۡ عَبَّدتَّ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“Ndipo kodi umenewu ndimtendere wonditonzera pomwe mudawaika muukapolo ana a Israyeli!”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ وَمَا رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Farawo adati: “Kodi ndani Mbuye wa zolengedwayo?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُم مُّوقِنِينَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wa thambo ndi nthaka ndi zapakati pake, ngati muli ndi chitsimikizo. (Amachita chilichonse m’menemo mmene wafunira; kupereka moyo ndi imfa).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ لِمَنۡ حَوۡلَهُۥٓ أَلَا تَسۡتَمِعُونَ
(Farawo) adauza omwe adali m’mphepete mwake (mwachipongwe): “Kodi simukumva (mawu achibwanawa)?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبُّكُمۡ وَرَبُّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Mûsa adapitiriza kunena) adati: “Allah ndi Mbuye wanu komanso Mbuye wamakolo anu oyamba.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ إِنَّ رَسُولَكُمُ ٱلَّذِيٓ أُرۡسِلَ إِلَيۡكُمۡ لَمَجۡنُونٞ
(Farawo) adati (kwa anthu ake pofuna kuwakwiitsa): “Ndithu Mtumiki wanu amene watumidwa kwa inu, ngwamisala.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wakuvuma ndi kuzambwe, ndi zomwe ziri pakati pake ngati mumazindikira (zinthu, muzindikira izi).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ لَئِنِ ٱتَّخَذۡتَ إِلَٰهًا غَيۡرِي لَأَجۡعَلَنَّكَ مِنَ ٱلۡمَسۡجُونِينَ
(Farawo) adati: “Ngati udzipangira mulungu wina kusiya ine, ndikuchita kukhala mmodzi wa omangidwa kundende.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ أَوَلَوۡ جِئۡتُكَ بِشَيۡءٖ مُّبِينٖ
(Mûsa) adati: “Kodi ngakhale nditakubweretsera chinthu choonekera poyera (chosonyeza kuti zimene ndikunenazi ndizoona ndatumidwa ndi Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ فَأۡتِ بِهِۦٓ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Farawo) adati: “Chibweretse, ngati uli mwa onena zoona.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَلۡقَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ ثُعۡبَانٞ مُّبِينٞ
Ndipo (Mûsa) adaponya (pansi) ndodo yake, mwadzidzidzi idasanduka njoka yopenyeka.
Faccirooji aarabeeji:
وَنَزَعَ يَدَهُۥ فَإِذَا هِيَ بَيۡضَآءُ لِلنَّٰظِرِينَ
Ndipo adatulutsa dzanja lake; pompo lidali loyera (kwambiri) kwa (onse) openya.
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ لِلۡمَلَإِ حَوۡلَهُۥٓ إِنَّ هَٰذَا لَسَٰحِرٌ عَلِيمٞ
(Farawo) adauza akuluakulu omwe adali m’mphepete mwake: “Ndithu uyu ndi wamatsenga wodziwa kwambiri.”
Faccirooji aarabeeji:
يُرِيدُ أَن يُخۡرِجَكُم مِّنۡ أَرۡضِكُم بِسِحۡرِهِۦ فَمَاذَا تَأۡمُرُونَ
“Akufuna kukutulutsani m’dziko lanu ndi matsenga ake; kodi nanga mukuti chiyani?”[296]
[296] Farawo adasimidwa, adatha nzeru zedi ndi mawu amene adali kutuluka m’kamwa mwa Musa kotero kuti adangoti kakasi, kusowa chonena, nayamba kuwafunsa nzeru ndi malangizo anthu ake pomwe iye ankadzitcha kuti ndi mulungu wodziwa zonse, wamphamvu zoposa.
Faccirooji aarabeeji:
قَالُوٓاْ أَرۡجِهۡ وَأَخَاهُ وَٱبۡعَثۡ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
(Anthu) adati (kwa Farawo): “Mpatse nthawi ndi m’bale wakeyo, ndipo tumiza (amithenga) m’mizinda yonse osonkhanitsa anthu.”
Faccirooji aarabeeji:
يَأۡتُوكَ بِكُلِّ سَحَّارٍ عَلِيمٖ
“Ndipo akubweretsera amatsenga onse odziwa kwabasi (kotero kuti adzampambana Mûsa).”
Faccirooji aarabeeji:
فَجُمِعَ ٱلسَّحَرَةُ لِمِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Choncho amatsenga adasonkhanitsidwa mu nthawi ya tsiku lodziwika.
Faccirooji aarabeeji:
وَقِيلَ لِلنَّاسِ هَلۡ أَنتُم مُّجۡتَمِعُونَ
Ndipo anthu adauzidwa: “Kodi inu musonkhana? (Choncho, sonkhanani).”
Faccirooji aarabeeji:
لَعَلَّنَا نَتَّبِعُ ٱلسَّحَرَةَ إِن كَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
“Mwina tingawatsatire amatsenga ngati iwo ndiamene apambane.”
Faccirooji aarabeeji:
فَلَمَّا جَآءَ ٱلسَّحَرَةُ قَالُواْ لِفِرۡعَوۡنَ أَئِنَّ لَنَا لَأَجۡرًا إِن كُنَّا نَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo pamene amatsenga adadza, adati kwa Farawo: “Kodi tidzakhala ndi mphoto ngati ife ndife tipambane?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ نَعَمۡ وَإِنَّكُمۡ إِذٗا لَّمِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
(Farawo) adati: “Inde, (ndipo kuonjezera apo) ndithu inu mudzakhala mwa amene amakhala pafupi (ndi ine, monga nduna zanga).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ لَهُم مُّوسَىٰٓ أَلۡقُواْ مَآ أَنتُم مُّلۡقُونَ
Mûsa adati kwa iwo: “Ponyani zimene mufuna kuponya (zosonyeza kuya kwa matsenga anu).”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَلۡقَوۡاْ حِبَالَهُمۡ وَعِصِيَّهُمۡ وَقَالُواْ بِعِزَّةِ فِرۡعَوۡنَ إِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Choncho adaponya zingwe zawo ndi ndodo zawo, ndipo adati: “Kupyolera mu mphamvu za Farawo, ndithu ife ndife opambana.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَلۡقَىٰ مُوسَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ تَلۡقَفُ مَا يَأۡفِكُونَ
Kenako Mûsa adaponya ndodo yake; mwadzidzidzi iyo idameza zabodza zomwe iwo adakonza.
Faccirooji aarabeeji:
فَأُلۡقِيَ ٱلسَّحَرَةُ سَٰجِدِينَ
Pamenepo amatsenga adadzigwetsa pansi molambira.
Faccirooji aarabeeji:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Tamkhulupirira Mbuye wa zolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa ndi Harun.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ ءَامَنتُمۡ لَهُۥ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّهُۥ لَكَبِيرُكُمُ ٱلَّذِي عَلَّمَكُمُ ٱلسِّحۡرَ فَلَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَۚ لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ وَلَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Farawo) adati: “Ha! Mwamkhulupirira chotani ndisanakulolezeni? Ndithu iyeyu ndimkulu wanu amene adakuphunzitsani matsenga. Choncho posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni) ndithu ndidula manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa (podula mkono wakumanja ndi mwendo wakumanzere; kapena kudula mkono wakumanzere ndi mwendo wakumanja), ndipo kenako ndikupachikani nonsenu.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ لَا ضَيۡرَۖ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Amatsenga) adati: “Palibe vuto, ndithu ife (tonse) tibwerera kwa Mbuye wathu.”
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّا نَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لَنَا رَبُّنَا خَطَٰيَٰنَآ أَن كُنَّآ أَوَّلَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndithu ife tikuyembekezera kuti Mbuye wathu atikhululukire zolakwa zathu; pokhala oyamba mwa okhulupirira.”
Faccirooji aarabeeji:
۞ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنۡ أَسۡرِ بِعِبَادِيٓ إِنَّكُم مُّتَّبَعُونَ
Ndipo tidamvumbulutsira Mûsa (kuti): “Pita ndi anthu anga m’nthawi yausiku (musamuke m’dziko la Iguputo); ndithu inu mutsatidwa.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَرۡسَلَ فِرۡعَوۡنُ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
Choncho Farawo adatuma (owatuma) kuti asonkhanitse anthu m’mizinda (kuti aletse ana a Israyeli kutuluka).
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَشِرۡذِمَةٞ قَلِيلُونَ
(Adawauza otumidwa aja kuti auze anthu kuti): “Ndithu awa (ana a Israyeli) ndikagulu kochepa.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّهُمۡ لَنَا لَغَآئِظُونَ
Ndipo ndithu iwo akutikwiitsa.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّا لَجَمِيعٌ حَٰذِرُونَ
Koma ndithu ife tonse (ndife ochuluka komabe ngakhale zili choncho) tikuwaopa.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَخۡرَجۡنَٰهُم مِّن جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Choncho tidawatulutsa m’minda ndi mwa akasupe.
Faccirooji aarabeeji:
وَكُنُوزٖ وَمَقَامٖ كَرِيمٖ
Ndi m’nkhokwe za chuma ndi m’malo okongola.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَٰلِكَۖ وَأَوۡرَثۡنَٰهَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Momwemo ndi mmene tidawachitira ndipo tidawalowetsera chokolo zinthu zawo zonse kwa ana a Israyeli.
Faccirooji aarabeeji:
فَأَتۡبَعُوهُم مُّشۡرِقِينَ
Choncho (anthu a Farawo ndi iye mwini) adawatsatira (ana a Israyeli) dzuwa litatuluka.
Faccirooji aarabeeji:
فَلَمَّا تَرَٰٓءَا ٱلۡجَمۡعَانِ قَالَ أَصۡحَٰبُ مُوسَىٰٓ إِنَّا لَمُدۡرَكُونَ
Ndipo pamene magulu awiri adaonana (anthu a Farawo ndi anthu a Mûsa), anthu a Mûsa adati: “Ndithu ife tigwidwa.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ كَلَّآۖ إِنَّ مَعِيَ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
(Mûsa) adati: “Iyayi! Ndithu Mbuye wanga ali nane pamodzi. Andiongolera (kuti ife tonse tipulumuke).”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡبَحۡرَۖ فَٱنفَلَقَ فَكَانَ كُلُّ فِرۡقٖ كَٱلطَّوۡدِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidam’vumbulutsira mawu Mûsa (akuti): “Menya nyanja ndi ndodo yako.” Ndipo idagawikana, mbali iliyonse idali ngati phiri lalikulu.
Faccirooji aarabeeji:
وَأَزۡلَفۡنَا ثَمَّ ٱلۡأٓخَرِينَ
Ndipo tidawayandikitsa pamenepo anthu enawo, (Farawo ndi anthu ake nalowa pa njira yomweyo pambuyo pa Mûsa ndi anthu ake).
Faccirooji aarabeeji:
وَأَنجَيۡنَا مُوسَىٰ وَمَن مَّعَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidapulumutsa Mûsa ndi onse amene adali nawo (mpaka adaoloka nyanjayo, madzi ali chiimire mbali iyi ndi iyi).
Faccirooji aarabeeji:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo, (Farawo ndi anthu ake).
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro. Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa (amalanga ndi chilango choopsa omwe amunyoza); Wachisoni (kwa omkhulupirira ndi kumumvera).
Faccirooji aarabeeji:
وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ إِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo awerengere (osakhulupirira) nkhani ya (M’neneri) Ibrahim.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَا تَعۡبُدُونَ
Pamene adafunsa bambo wake ndi anthu ake (kuti); “Kodi mukupembedza chiyani?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ نَعۡبُدُ أَصۡنَامٗا فَنَظَلُّ لَهَا عَٰكِفِينَ
Adati: “Tikupembedza mafano; ndipo tipitiriza kuwapembedza.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ هَلۡ يَسۡمَعُونَكُمۡ إِذۡ تَدۡعُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi amakumvani mukawaitana?”
Faccirooji aarabeeji:
أَوۡ يَنفَعُونَكُمۡ أَوۡ يَضُرُّونَ
“Kapena amakuthandizani (mukawapembedza) kapena amapereka masautso kwa inu (mukasiya kuwapembedza)?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ بَلۡ وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا كَذَٰلِكَ يَفۡعَلُونَ
(Iwo) adati: “Koma tidapeza makolo athu akuchita zimenezi.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ أَفَرَءَيۡتُم مَّا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi mukuwaona awa amene mwakhala mukuwapembedza,”
Faccirooji aarabeeji:
أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُمُ ٱلۡأَقۡدَمُونَ
“Inu ndi makolo anu amene adatsogola?”
Faccirooji aarabeeji:
فَإِنَّهُمۡ عَدُوّٞ لِّيٓ إِلَّا رَبَّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndithu iwo ndiadani anga, kupatula Mbuye wa zolengedwa zonse;”
Faccirooji aarabeeji:
ٱلَّذِي خَلَقَنِي فَهُوَ يَهۡدِينِ
“Yemwe adandilenga, ndiponso Yemwe akundiongolera (kunjira yolungama);”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱلَّذِي هُوَ يُطۡعِمُنِي وَيَسۡقِينِ
“Ndiyemwe akundidyetsa ndi kundimwetsa.”
Faccirooji aarabeeji:
وَإِذَا مَرِضۡتُ فَهُوَ يَشۡفِينِ
“Ndipo ndikadwala ndiyemwe amandichiritsa.”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱلَّذِي يُمِيتُنِي ثُمَّ يُحۡيِينِ
“Ndi Amene adzandipatsa imfa, ndipo (tsiku la Qiyâma) adzandidzutsa;”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱلَّذِيٓ أَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لِي خَطِيٓـَٔتِي يَوۡمَ ٱلدِّينِ
“Ndi Yemwe ndikuyembekezera kuti adzandikhululukira zolakwa zanga tsiku la malipiro.”
Faccirooji aarabeeji:
رَبِّ هَبۡ لِي حُكۡمٗا وَأَلۡحِقۡنِي بِٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni nzeru zoweruzira (zinthu), ndikundilumikiza ndi anthu abwino;”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱجۡعَل لِّي لِسَانَ صِدۡقٖ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
“Ndipatseni kutchulidwa kwabwino kwa anthu ena odza pambuyo;”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱجۡعَلۡنِي مِن وَرَثَةِ جَنَّةِ ٱلنَّعِيمِ
“Ndichiteni kukhala mmodzi mwa olandira Munda wamtendere;”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱغۡفِرۡ لِأَبِيٓ إِنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
“Ndipo khululukirani bambo wanga; ndithu iye adali mmodzi wa osokera;”
Faccirooji aarabeeji:
وَلَا تُخۡزِنِي يَوۡمَ يُبۡعَثُونَ
“Ndipo musadzandiyalutse pa tsiku loukitsidwa anthu (ku imfa);”
Faccirooji aarabeeji:
يَوۡمَ لَا يَنفَعُ مَالٞ وَلَا بَنُونَ
“Tsiku lomwe chuma ndi ana sizidzathandiza (aliyense).”
Faccirooji aarabeeji:
إِلَّا مَنۡ أَتَى ٱللَّهَ بِقَلۡبٖ سَلِيمٖ
“Kupatula yemwe adzadza kwa Allah ndi mtima woyera (iye ndiamene adzathandizidwa patsikulo).”
Faccirooji aarabeeji:
وَأُزۡلِفَتِ ٱلۡجَنَّةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Ndipo Munda wamtendere udzayandikitsidwa kwa oopa (Allah),
Faccirooji aarabeeji:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِلۡغَاوِينَ
Ndipo Jahannam idzaonetsedwa kwa opotoka;
Faccirooji aarabeeji:
وَقِيلَ لَهُمۡ أَيۡنَ مَا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
Ndipo kudzanenedwa kwa iwo: “Ali kuti amene mudali kuwapembedza aja,
Faccirooji aarabeeji:
مِن دُونِ ٱللَّهِ هَلۡ يَنصُرُونَكُمۡ أَوۡ يَنتَصِرُونَ
M’malo mwa Allah? Kodi angathe kukuthandizani kapena kudzithandiza okha?”
Faccirooji aarabeeji:
فَكُبۡكِبُواْ فِيهَا هُمۡ وَٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo iwo ndi opotoka ena adzaponyedwa ndi nkhope zawo m’menemo (mu Jahannam).
Faccirooji aarabeeji:
وَجُنُودُ إِبۡلِيسَ أَجۡمَعُونَ
Ndi magulu onse ankhondo a Iblis (omwe adali kukometsa kwa anthu zoipa ndi machimo).
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ وَهُمۡ فِيهَا يَخۡتَصِمُونَ
Adzanena (movomereza kulakwa kwawo) uku naonso ali m’menemo, akukangana (ndi anzawo omwe adawasokeretsa):
Faccirooji aarabeeji:
تَٱللَّهِ إِن كُنَّا لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٍ
“Ndikulumbira Allah, ndithu tidali m’kusokera kowonekera.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ نُسَوِّيكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Pamene timakufananitsani ndi Mbuye wa zolengedwa.
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَضَلَّنَآ إِلَّا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
Ndipo sadatisokeretse, koma oipa okha basi.
Faccirooji aarabeeji:
فَمَا لَنَا مِن شَٰفِعِينَ
Choncho ife tilibe aomboli (otiombola),
Faccirooji aarabeeji:
وَلَا صَدِيقٍ حَمِيمٖ
Ngakhalenso bwenzi wapamtima (woti angatipulumutse kumasautsowa).
Faccirooji aarabeeji:
فَلَوۡ أَنَّ لَنَا كَرَّةٗ فَنَكُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Tikadapeza mwayi wobwerera (ku moyo wa padziko), tikadakhala mwa okhulupirira.”
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi, muli malingaliro akulu, koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, ndiye Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ نُوحٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Nuh adatsutsa atumiki.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ نُوحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene adawauza Nuh m’bale wawo kuti: “Kodi simukuopa (Allah ngakhale nditakuuzani zoopsa zimene zikukudikirani)?”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine kwa inu ndine Mtumiki wokhulupirika;”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
۞ قَالُوٓاْ أَنُؤۡمِنُ لَكَ وَٱتَّبَعَكَ ٱلۡأَرۡذَلُونَ
(Iwo) adati: “Nchotani kuti tikukhulupirire iwe chikhalirecho anthu wamba ndi amene akukutsatira?”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ وَمَا عِلۡمِي بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
(Nuh) adati: “Sindikudziwa zimene adali kuchita (zomwe zachititsa kuti Allah awaongolere kunjira yoongoka).”
Faccirooji aarabeeji:
إِنۡ حِسَابُهُمۡ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّيۖ لَوۡ تَشۡعُرُونَ
“Chiwerengero chawo sichili kwina koma kwa Mbuye wanga, mukadakhala mukuzindikira.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَنَا۠ بِطَارِدِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndipo sindine wopirikitsa okhulupirira (ku chipembedzo cha Allah kuti inu olemekezeka muchikhulupirire).”
Faccirooji aarabeeji:
إِنۡ أَنَا۠ إِلَّا نَذِيرٞ مُّبِينٞ
“Ine sikanthu , koma ndine mchenjezi woonekera.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰنُوحُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمَرۡجُومِينَ
(Iwo) adati: “Ngati susiya, iwe Nuh, (zonena zakozi) ndithu ukhala mmodzi mwa ogendedwa (miyala mpaka ufe).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبِّ إِنَّ قَوۡمِي كَذَّبُونِ
(Nuh) adati (kwa Allah): “Mbuye wanga! Ndithu anthu anga anditsutsa.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱفۡتَحۡ بَيۡنِي وَبَيۡنَهُمۡ فَتۡحٗا وَنَجِّنِي وَمَن مَّعِيَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Choncho weruzani pakati panga ndi pakati pa iwo (chiweruzo chabwino), ndipo ndipulumutseni pamodzi ndi amene alinane mwa okhulupirira.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَمَن مَّعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
Choncho, tidampulumutsa pamodzi ndi omwe adali naye m’chombo chodzadza (ndi chilichonse chamoyo chomwe chidalipo m’dziko, chachimuna ndi chachikazi chidaikidwa m’menemo).
Faccirooji aarabeeji:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا بَعۡدُ ٱلۡبَاقِينَ
Pambuyo pake tidawamiza otsalawo.
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; Ngwachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَّبَتۡ عَادٌ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Naonso Âdi adatsutsa atumiki.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ هُودٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo (Mneneri) Hûd adawafunsa kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu;”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho, muopeni Allah ndipo mverani ine.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo pazimenezi sindikukupemphani malipiro; ndithu malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
أَتَبۡنُونَ بِكُلِّ رِيعٍ ءَايَةٗ تَعۡبَثُونَ
“Kodi mukudzimangira nyumba pamalo paliponse pachitunda pokongola, moseweretsa?”
Faccirooji aarabeeji:
وَتَتَّخِذُونَ مَصَانِعَ لَعَلَّكُمۡ تَخۡلُدُونَ
“Ndipo mukudzimangira (nyumba zonga) linga ngati kuti mukuona kuti mudzakhala muyaya?”
Faccirooji aarabeeji:
وَإِذَا بَطَشۡتُم بَطَشۡتُمۡ جَبَّارِينَ
“Ndipo mukamamenya nkhondo mumamenya modzitukumula.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِيٓ أَمَدَّكُم بِمَا تَعۡلَمُونَ
“Ndipo muopeni Yemwe adakupatsani zimene mukuzidziwa.”
Faccirooji aarabeeji:
أَمَدَّكُم بِأَنۡعَٰمٖ وَبَنِينَ
“Adakupatsani ziweto ndi ana.”
Faccirooji aarabeeji:
وَجَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
“Ndi minda ndi akasupe.”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ سَوَآءٌ عَلَيۡنَآ أَوَعَظۡتَ أَمۡ لَمۡ تَكُن مِّنَ ٱلۡوَٰعِظِينَ
Iwo adati: “Kwa ife nchimodzimodzi, utichenjeze kapena iwe usakhale mmodzi mwa ochenjeza.”
Faccirooji aarabeeji:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا خُلُقُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndithu kutero (anthu ena kudzitcha atumiki a Allah), sikanthu koma ndi machitidwe a anthu akale.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
“Ndipo ife sitidzalangidwa (monga momwe ukunenera).”
Faccirooji aarabeeji:
فَكَذَّبُوهُ فَأَهۡلَكۡنَٰهُمۡۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho adamtsutsa, ndipo tidawaononga. Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako ndiye Wamphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
A Samudu (naonso) adatsutsa atumiki.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ صَٰلِحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Swalih adawauza kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndimtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo mverani ine.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi. Palibe kumene kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wa zolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
أَتُتۡرَكُونَ فِي مَا هَٰهُنَآ ءَامِنِينَ
“Kodi (mukuganizira kuti) mudzasiidwa mwamtendere pa izi zili pano (popanda imfa kukudzerani?)”
Faccirooji aarabeeji:
فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
“M’minda ndi mu akasupe?”
Faccirooji aarabeeji:
وَزُرُوعٖ وَنَخۡلٖ طَلۡعُهَا هَضِيمٞ
“Ndi (m’minda) yammera ndi mitengo yakanjedza yamikoko yakupsa yofewa?”
Faccirooji aarabeeji:
وَتَنۡحِتُونَ مِنَ ٱلۡجِبَالِ بُيُوتٗا فَٰرِهِينَ
“Ndipo mukugoba nyumba m’mapiri mwaluso.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
وَلَا تُطِيعُوٓاْ أَمۡرَ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
“Ndipo musamvere za awo opyola malire.”
Faccirooji aarabeeji:
ٱلَّذِينَ يُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا يُصۡلِحُونَ
“Amene akuononga pa dziko, ndipo sakonza.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
مَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا فَأۡتِ بِـَٔايَةٍ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Iwe suli kanthu, koma munthu ngati ife; tabwera ndi chozizwitsa, ngati ndiwedi mmodzi wa onena zoona!”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ هَٰذِهِۦ نَاقَةٞ لَّهَا شِرۡبٞ وَلَكُمۡ شِرۡبُ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Iye adati: “(Ndakubweretserani) ngamira iyi yaikazi; (koma) ili ndi gawo lake lakumwa, ndipo inu muli ndi gawo lanu lakutunga (madzi) patsiku lodziwika. (Tsiku lina lotunga rnadzi anthu).”
Faccirooji aarabeeji:
وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابُ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndipo musaikhudze ndi choipa chilichonse kuopera kuti chingakupezeni chilango cha tsiku lalikulu.”
Faccirooji aarabeeji:
فَعَقَرُوهَا فَأَصۡبَحُواْ نَٰدِمِينَ
Koma iwo adaipha; ndipo adali odzinena (pamene chidadza chilango cha Allah).
Faccirooji aarabeeji:
فَأَخَذَهُمُ ٱلۡعَذَابُۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho chilango (cha Allah) chidawaononga, ndithu pa zimenezi pali phunziro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; wachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ لُوطٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Luti adatsutsa atumiki.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ لُوطٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Luti adanena kwa iwo (kuti): “Kodi simuopa (Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; palibe komwe kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wazolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
أَتَأۡتُونَ ٱلذُّكۡرَانَ مِنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi mukugonana ndi amuna (anzanu) muzolengedwa (za Allah),
Faccirooji aarabeeji:
وَتَذَرُونَ مَا خَلَقَ لَكُمۡ رَبُّكُم مِّنۡ أَزۡوَٰجِكُمۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٌ عَادُونَ
“Ndikusiya amene Mbuye wanu adakulengerani kuti akhale akazi anu? Ndithu inu ndinu anthu olumpha malire.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰلُوطُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُخۡرَجِينَ
Iwo adati: “Ngati susiya (izi), E iwe Luti! ndithu ukhala mmodzi wa opirikitsidwa.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ إِنِّي لِعَمَلِكُم مِّنَ ٱلۡقَالِينَ
Iye adati: “Ndithu ine ndine m’modzi wakuzida izi zochita zanu (choncho Sindisiya kuzidzudzula).”
Faccirooji aarabeeji:
رَبِّ نَجِّنِي وَأَهۡلِي مِمَّا يَعۡمَلُونَ
“E Mbuye wanga! Ndipulumutseni ine ndi banja langa ku (matsoka a) zimene akuchita.”
Faccirooji aarabeeji:
فَنَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidampulumutsa iye ndi onse a pa banja lake,
Faccirooji aarabeeji:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yaikazi idali mwa otsalira m’mbuyo.
Faccirooji aarabeeji:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Titatero tidawaononga enawo.
Faccirooji aarabeeji:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji, mvula ya ochenjezedwa!
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pazimenezi pali malingaliro. Koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَّبَ أَصۡحَٰبُ لۡـَٔيۡكَةِ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a m’dziko lamitengo yambiri (Madiana) adatsutsa atumiki.
Faccirooji aarabeeji:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ شُعَيۡبٌ أَلَا تَتَّقُونَ
(Akumbutse) pamene (Mneneri) Shuaib adati kwa iwo: “Kodi simuopa (Allah)?”
Faccirooji aarabeeji:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Faccirooji aarabeeji:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; kulibe malipiro anga koma kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
۞ أَوۡفُواْ ٱلۡكَيۡلَ وَلَا تَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُخۡسِرِينَ
“Kwaniritsani mulingo (pamalonda pamene mukupima), ndipo musakhale mwaopungula (mulingo).”
Faccirooji aarabeeji:
وَزِنُواْ بِٱلۡقِسۡطَاسِ ٱلۡمُسۡتَقِيمِ
“Ndipo yesani ndi sikelo yolungama (yolondola).”
Faccirooji aarabeeji:
وَلَا تَبۡخَسُواْ ٱلنَّاسَ أَشۡيَآءَهُمۡ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo musawachepetsere anthu zinthu zawo, ndiponso musayende padziko uku mukuononga.”
Faccirooji aarabeeji:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ وَٱلۡجِبِلَّةَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndipo muopeni amene adalenga inu ndiponso zolengedwa zoyamba (zimene zidanka kale).”
Faccirooji aarabeeji:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا وَإِن نَّظُنُّكَ لَمِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
“Ndipo iwe suli kanthu koma munthu ngati ife, ndipo ndithu tikukutsimikizira kuti ndiwe mmodzi wa abodza.”
Faccirooji aarabeeji:
فَأَسۡقِطۡ عَلَيۡنَا كِسَفٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Choncho tigwetsere zidutswa za thambo (kuti zitiononge) ngati uli mmodzi wa onena zoona.”
Faccirooji aarabeeji:
قَالَ رَبِّيٓ أَعۡلَمُ بِمَا تَعۡمَلُونَ
(Shuaib) adati: “Mbuye wanga Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita. (Akadzaona kuti inu ngoyenera kulangidwa ndizidutswa za thambo, adzakulangani).”
Faccirooji aarabeeji:
فَكَذَّبُوهُ فَأَخَذَهُمۡ عَذَابُ يَوۡمِ ٱلظُّلَّةِۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٍ
Koma adamutsutsa. Ndipo chidawagwera chilango chatsiku la mthunzi; ndithu chimenecho chidali chilango cha tsiku lalikulu.
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّهُۥ لَتَنزِيلُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo, ndithu iyi (Qur’an) ndiyo chivumbulutso cha Mbuye wazolengedwa zonse.
Faccirooji aarabeeji:
نَزَلَ بِهِ ٱلرُّوحُ ٱلۡأَمِينُ
Mzimu Wokhulupirika (Jiburil) udaivumbulutsa.
Faccirooji aarabeeji:
عَلَىٰ قَلۡبِكَ لِتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُنذِرِينَ
Pa mtima wako kuti ukhale mmodzi wa achenjezi,
Faccirooji aarabeeji:
بِلِسَانٍ عَرَبِيّٖ مُّبِينٖ
M’chiyankhulo cha Chiarabu chomveka bwino.
Faccirooji aarabeeji:
وَإِنَّهُۥ لَفِي زُبُرِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo ndithu izi (zomwe zili m’Qur’an) zilipo m’mabuku akale.
Faccirooji aarabeeji:
أَوَلَمۡ يَكُن لَّهُمۡ ءَايَةً أَن يَعۡلَمَهُۥ عُلَمَٰٓؤُاْ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Kodi sipadapezeke chisonyezo kwa iwo kuti akuidziwa (Qur’an) odziwa mwa ana a Israyeli (kotero kuti ena alowa m’Chisilamu)?
Faccirooji aarabeeji:
وَلَوۡ نَزَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ بَعۡضِ ٱلۡأَعۡجَمِينَ
Ndipo tikadaivumbulutsa kwa wina amene sali Muarabu,
Faccirooji aarabeeji:
فَقَرَأَهُۥ عَلَيۡهِم مَّا كَانُواْ بِهِۦ مُؤۡمِنِينَ
Kotero kuti nkuwawerengera momveka bwino, sakadaikhulupirira.
Faccirooji aarabeeji:
كَذَٰلِكَ سَلَكۡنَٰهُ فِي قُلُوبِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Momwemo ndimo tidalowetsera kuitsutsa (Qur’an) m’mitima ya oipa.
Faccirooji aarabeeji:
لَا يُؤۡمِنُونَ بِهِۦ حَتَّىٰ يَرَوُاْ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَلِيمَ
Sangaikhulupirire kufikira ataona chilango chowawa.
Faccirooji aarabeeji:
فَيَأۡتِيَهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Choncho chidzawadzera mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira.
Faccirooji aarabeeji:
فَيَقُولُواْ هَلۡ نَحۡنُ مُنظَرُونَ
Tero adzayamba kunena: “Kodi ife tipatsidwa nthawi (yoti tilape)?”
Faccirooji aarabeeji:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi akuchifulumizitsa chilango Chathu?
Faccirooji aarabeeji:
أَفَرَءَيۡتَ إِن مَّتَّعۡنَٰهُمۡ سِنِينَ
Kodi ukuona bwanji, ngati titawasangalatsa zaka (zankhaninkhani).
Faccirooji aarabeeji:
ثُمَّ جَآءَهُم مَّا كَانُواْ يُوعَدُونَ
Kenako nkuwadzera (chilango) chomwe adalonjezedwa,
Faccirooji aarabeeji:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يُمَتَّعُونَ
Sizidawathandize zomwe adali kusangalatsidwa nazozo.
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَهۡلَكۡنَا مِن قَرۡيَةٍ إِلَّا لَهَا مُنذِرُونَ
Ndipo sitidauononge mudzi uliwonse koma udali ndi achenjezi.
Faccirooji aarabeeji:
ذِكۡرَىٰ وَمَا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Kuti akhale) chikumbutso. Ndipo sitidali osalungama (powaononga popanda kuwachenjeza).
Faccirooji aarabeeji:
وَمَا تَنَزَّلَتۡ بِهِ ٱلشَّيَٰطِينُ
Ndipo asatana sadaivumbulutse (iyi Qur’an monga osakhulupirira akunenera monyoza).
Faccirooji aarabeeji:
وَمَا يَنۢبَغِي لَهُمۡ وَمَا يَسۡتَطِيعُونَ
Ndipo sikoyenera kwa iwo (kuivumbulutsa Qur’an) ndiponso sangathe.
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّهُمۡ عَنِ ٱلسَّمۡعِ لَمَعۡزُولُونَ
Ndithu iwo ngotsekerezedwa kumvetsera (zimene angelo amalankhula kumwamba).
Faccirooji aarabeeji:
فَلَا تَدۡعُ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَ فَتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُعَذَّبِينَ
Choncho usapembedze mulungu wina pamodzi ndi Allah, kuti ungakhale mwa olangidwa.
Faccirooji aarabeeji:
وَأَنذِرۡ عَشِيرَتَكَ ٱلۡأَقۡرَبِينَ
Ndipo achenjeze abale ako a pafupi.
Faccirooji aarabeeji:
وَٱخۡفِضۡ جَنَاحَكَ لِمَنِ ٱتَّبَعَكَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndipo fungatira ndi phiko lako amene akutsata mwa okhulupirira. (Ukhale wachifundo kwa iwo).
Faccirooji aarabeeji:
فَإِنۡ عَصَوۡكَ فَقُلۡ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّمَّا تَعۡمَلُونَ
Ngati atakunyoza, nena: “Ine ndili kutali ndi zimene mukuchitazo.”
Faccirooji aarabeeji:
وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱلۡعَزِيزِ ٱلرَّحِيمِ
Ndipo tsamira kwa (Mbuye wako) Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Faccirooji aarabeeji:
ٱلَّذِي يَرَىٰكَ حِينَ تَقُومُ
Yemwe akukuona pamene ukuimilira (pamapemphero).
Faccirooji aarabeeji:
وَتَقَلُّبَكَ فِي ٱلسَّٰجِدِينَ
Ndikutembenukatembenuka kwako (pogwetsa mphumi yako pansi ndi kudzuka ndi kuimilira) pamodzi ndi ogwetsa mphumi pansi (polambira Allah).
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndithu Iye Ngwakumva; Ngodziwa chilichonse.
Faccirooji aarabeeji:
هَلۡ أُنَبِّئُكُمۡ عَلَىٰ مَن تَنَزَّلُ ٱلشَّيَٰطِينُ
Kodi ndikuuzeni amene asatana amawatsikira?
Faccirooji aarabeeji:
تَنَزَّلُ عَلَىٰ كُلِّ أَفَّاكٍ أَثِيمٖ
Amamtsikira yense wabodza lamkunkhuniza; wamachimo.
Faccirooji aarabeeji:
يُلۡقُونَ ٱلسَّمۡعَ وَأَكۡثَرُهُمۡ كَٰذِبُونَ
Amawaponyera (asatana anzawo a mu anthu) zimene azimva. Koma ambiri a iwo ngabodza.
Faccirooji aarabeeji:
وَٱلشُّعَرَآءُ يَتَّبِعُهُمُ ٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo alakatuli (olakatula zopanda phindu) amatsatidwa ndi (anthu) opotoka.
Faccirooji aarabeeji:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّهُمۡ فِي كُلِّ وَادٖ يَهِيمُونَ
Kodi suona kuti iwo akungoyumbayumba m’chigwa chilichonse (chamawu)?
Faccirooji aarabeeji:
وَأَنَّهُمۡ يَقُولُونَ مَا لَا يَفۡعَلُونَ
Ndithunso iwo akunena zomwe sachita.
Faccirooji aarabeeji:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَذَكَرُواْ ٱللَّهَ كَثِيرٗا وَٱنتَصَرُواْ مِنۢ بَعۡدِ مَا ظُلِمُواْۗ وَسَيَعۡلَمُ ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ أَيَّ مُنقَلَبٖ يَنقَلِبُونَ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, ndikumamtchula Allah mowirikiza, ndikuzipulumutsa okha pambuyo pochitiridwa zoipa. Ndipo posachedwa amene adzichitira okha zoipa adziwa kotembenukira komwe adzatembenukire.
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Simoore: Simoore yimooɓe
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo - Tippudi firooji ɗii

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo fayde e ɗemngal siisii, fari ɗum ko Kaaliid piitalaa. Tummbutere hitaande 2020

Uddude