Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Ma'aaridj (De Manieren van Ascentie)   Vers:

Soerat Al-Ma'aaridj (De Manieren van Ascentie)

سَأَلَ سَآئِلُۢ بِعَذَابٖ وَاقِعٖ
Wopempha adapempha kuti chiwadzere msanga chilango chopezekacho, (m’kupempha kwa chipongwe ndi kotsutsa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِّلۡكَٰفِرِينَ لَيۡسَ لَهُۥ دَافِعٞ
Kwa okanira palibe angachitsekereze.
Arabische uitleg van de Qur'an:
مِّنَ ٱللَّهِ ذِي ٱلۡمَعَارِجِ
Chochokera kwa Allah Mwini makwelero.
Arabische uitleg van de Qur'an:
تَعۡرُجُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَٱلرُّوحُ إِلَيۡهِ فِي يَوۡمٖ كَانَ مِقۡدَارُهُۥ خَمۡسِينَ أَلۡفَ سَنَةٖ
Angelo ndi Jiburil amakwera kwa Iye (Allah) m’tsiku lomwe kutalika kwake kuli ngati zaka zikwi makumi asanu (50 000).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَٱصۡبِرۡ صَبۡرٗا جَمِيلًا
Choncho, pirira (iwe Mtumiki (s.a.w) kupirira kwabwino,
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّهُمۡ يَرَوۡنَهُۥ بَعِيدٗا
Ndithu iwo akuliona (tsiku la Qiyâma) kuti lili kutali (silingachitike).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَنَرَىٰهُ قَرِيبٗا
Koma Ife tikuliona kuti lilipafupi (ndilochitika).
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَوۡمَ تَكُونُ ٱلسَّمَآءُ كَٱلۡمُهۡلِ
Tsiku limene thambo lidzakhala ngati mtovu wosungunuka.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya (wongouluka wokha).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَا يَسۡـَٔلُ حَمِيمٌ حَمِيمٗا
Ndipo m’bale sadzafunsa za m’bale wake.
Arabische uitleg van de Qur'an:
يُبَصَّرُونَهُمۡۚ يَوَدُّ ٱلۡمُجۡرِمُ لَوۡ يَفۡتَدِي مِنۡ عَذَابِ يَوۡمِئِذِۭ بِبَنِيهِ
Ngakhale adzawalole kuti aonane ndi kudziwana pakati pawo (sadzafunsana). Wochimwa adzalakalaka kuti akadaziwombola ku chilango cha tsiku limenelo ndi ana ake.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَأَخِيهِ
Ndi mkazi wake, ndi m’bale wake.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَفَصِيلَتِهِ ٱلَّتِي تُـٔۡوِيهِ
Ndi akumtundu wake amene amamsunga.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا ثُمَّ يُنجِيهِ
Ndi (kulipira) zonse za m’dziko, kuti zimpulumutse.
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّآۖ إِنَّهَا لَظَىٰ
Iyayi, (siya iwe wamachimo zimene ukulakalakazo)! Ndithu umenewu ndi Moto wa malawi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
نَزَّاعَةٗ لِّلشَّوَىٰ
Wosupula mwamphamvu khungu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
تَدۡعُواْ مَنۡ أَدۡبَرَ وَتَوَلَّىٰ
Udzaitana (potchula dzina la aliyense) amene adachitembenuzira msana choona ndi kunyoza.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَجَمَعَ فَأَوۡعَىٰٓ
Adasonkhanitsa (chuma) ndi kusunga (m’nkhokwe zake popanda kuperekera chopereka cha Allah).
Arabische uitleg van de Qur'an:
۞ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ خُلِقَ هَلُوعًا
Ndithu munthu walengedwa kukhala wosapirira.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِذَا مَسَّهُ ٱلشَّرُّ جَزُوعٗا
Mavuto akamkhudza amada nkhawa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِذَا مَسَّهُ ٱلۡخَيۡرُ مَنُوعًا
Koma zabwino zikamkhudza amamana (ena ndi kuiwala mavuto amene adali nawo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِلَّا ٱلۡمُصَلِّينَ
Kupatula opemphera Swala, (iwo alibe mbiri zoipazi).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ دَآئِمُونَ
Iwo amene sadukiza mapemphero awo a swala; (sakuwaleka ngakhale zivute chotani).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ فِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ مَّعۡلُومٞ
Ndi amene mchuma chawo muli gawo lodziwika (Zakaat),
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
La wopempha ndi wosapempha.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ يُصَدِّقُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndi amene akuvomereza za tsiku la malipiro (ndi kumalikonzekera.)
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هُم مِّنۡ عَذَابِ رَبِّهِم مُّشۡفِقُونَ
Ndi iwo amene akuopa chilango chochokera kwa Mbuye wawo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّ عَذَابَ رَبِّهِمۡ غَيۡرُ مَأۡمُونٖ
Ndithu chilango cha Mbuye wawo nchosapulumuka nacho (munthu woipa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِفُرُوجِهِمۡ حَٰفِظُونَ
Ndiponso iwo amene akusunga umaliseche wawo (posachita chiwerewere),
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِلَّا عَلَىٰٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ أَوۡ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ فَإِنَّهُمۡ غَيۡرُ مَلُومِينَ
Kupatula kwa akazi awo ndi amene manja awo akumanja apeza; ndithu pazimenezo iwo sangadzudzulidwe.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَمَنِ ٱبۡتَغَىٰ وَرَآءَ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡعَادُونَ
Koma amene angafune (zina) kusiya zimenezi iwowo ndiwo olumpha malire.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِأَمَٰنَٰتِهِمۡ وَعَهۡدِهِمۡ رَٰعُونَ
Ndi iwo amene amasunga mwaubwino zimene amasungitsidwa ndi zimene alonjeza.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هُم بِشَهَٰدَٰتِهِمۡ قَآئِمُونَ
Ndi iwo amene amaima molungama popereka umboni wawo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ يُحَافِظُونَ
Ndiponso iwo amene amasunga (mwaubwino) mapemphero awo a swala.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أُوْلَٰٓئِكَ فِي جَنَّٰتٖ مُّكۡرَمُونَ
Amene ali ndi mbiri zimenezi adzakhala m’Minda (yamtendere) ali olemekezedwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَمَالِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ قِبَلَكَ مُهۡطِعِينَ
Kodi kuli chiyani kwa amene akana (chikhulupiliro) akuthamangira kwa iwe (maso ali pamtunda)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَنِ ٱلۡيَمِينِ وَعَنِ ٱلشِّمَالِ عِزِينَ
Atakuzungulira ena chakumanja ena chakumanzere.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَيَطۡمَعُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُدۡخَلَ جَنَّةَ نَعِيمٖ
Kodi akulakalaka aliyense mwa iwo kuti akalowetsedwe ku Munda wamtendere?
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّآۖ إِنَّا خَلَقۡنَٰهُم مِّمَّا يَعۡلَمُونَ
Asiye (kukhumba kwawo kokalowa ku Munda wamtendere)! Ndithu Ife tidawalenga kuchokera m’zimene akudziwa (madzi opanda pake).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِرَبِّ ٱلۡمَشَٰرِقِ وَٱلۡمَغَٰرِبِ إِنَّا لَقَٰدِرُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kuvuma ndi kuzambwe konse ndithu Ndife Wokhoza.
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَلَىٰٓ أَن نُّبَدِّلَ خَيۡرٗا مِّنۡهُمۡ وَمَا نَحۡنُ بِمَسۡبُوقِينَ
Kuwasintha ndi kudzetsa abwino kuposa iwo; Ife palibe (chilichonse) chotipambana.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَذَرۡهُمۡ يَخُوضُواْ وَيَلۡعَبُواْ حَتَّىٰ يُلَٰقُواْ يَوۡمَهُمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Asiye azingolankhula zopanda pake ndi kumangosewera mpaka adzakumane ndi tsiku lawo limene akulonjezedwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَوۡمَ يَخۡرُجُونَ مِنَ ٱلۡأَجۡدَاثِ سِرَاعٗا كَأَنَّهُمۡ إِلَىٰ نُصُبٖ يُوفِضُونَ
Tsiku limene adzatuluke m’manda uku akuthamanga (kudza kwa woitana) ngati kuti akuthamangira kumafano awo (amene adali kuwapembedza).
Arabische uitleg van de Qur'an:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۚ ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلَّذِي كَانُواْ يُوعَدُونَ
Maso awo ali zyoli, (osatha kuwakweza); kuyaluka kutawaphimba! Limenelo ndilo tsiku lomwe adali kulonjezedwa (pomwe adali padziko lapansi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Ma'aaridj (De Manieren van Ascentie)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit