Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: Almaarij (Inzego)   Umurongo:

Almaarij (Inzego)

سَأَلَ سَآئِلُۢ بِعَذَابٖ وَاقِعٖ
Wopempha adapempha kuti chiwadzere msanga chilango chopezekacho, (m’kupempha kwa chipongwe ndi kotsutsa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
لِّلۡكَٰفِرِينَ لَيۡسَ لَهُۥ دَافِعٞ
Kwa okanira palibe angachitsekereze.
Ibisobanuro by'icyarabu:
مِّنَ ٱللَّهِ ذِي ٱلۡمَعَارِجِ
Chochokera kwa Allah Mwini makwelero.
Ibisobanuro by'icyarabu:
تَعۡرُجُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَٱلرُّوحُ إِلَيۡهِ فِي يَوۡمٖ كَانَ مِقۡدَارُهُۥ خَمۡسِينَ أَلۡفَ سَنَةٖ
Angelo ndi Jiburil amakwera kwa Iye (Allah) m’tsiku lomwe kutalika kwake kuli ngati zaka zikwi makumi asanu (50 000).
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَٱصۡبِرۡ صَبۡرٗا جَمِيلًا
Choncho, pirira (iwe Mtumiki (s.a.w) kupirira kwabwino,
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّهُمۡ يَرَوۡنَهُۥ بَعِيدٗا
Ndithu iwo akuliona (tsiku la Qiyâma) kuti lili kutali (silingachitike).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَنَرَىٰهُ قَرِيبٗا
Koma Ife tikuliona kuti lilipafupi (ndilochitika).
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَوۡمَ تَكُونُ ٱلسَّمَآءُ كَٱلۡمُهۡلِ
Tsiku limene thambo lidzakhala ngati mtovu wosungunuka.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya (wongouluka wokha).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَلَا يَسۡـَٔلُ حَمِيمٌ حَمِيمٗا
Ndipo m’bale sadzafunsa za m’bale wake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
يُبَصَّرُونَهُمۡۚ يَوَدُّ ٱلۡمُجۡرِمُ لَوۡ يَفۡتَدِي مِنۡ عَذَابِ يَوۡمِئِذِۭ بِبَنِيهِ
Ngakhale adzawalole kuti aonane ndi kudziwana pakati pawo (sadzafunsana). Wochimwa adzalakalaka kuti akadaziwombola ku chilango cha tsiku limenelo ndi ana ake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَأَخِيهِ
Ndi mkazi wake, ndi m’bale wake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَفَصِيلَتِهِ ٱلَّتِي تُـٔۡوِيهِ
Ndi akumtundu wake amene amamsunga.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا ثُمَّ يُنجِيهِ
Ndi (kulipira) zonse za m’dziko, kuti zimpulumutse.
Ibisobanuro by'icyarabu:
كَلَّآۖ إِنَّهَا لَظَىٰ
Iyayi, (siya iwe wamachimo zimene ukulakalakazo)! Ndithu umenewu ndi Moto wa malawi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
نَزَّاعَةٗ لِّلشَّوَىٰ
Wosupula mwamphamvu khungu.
Ibisobanuro by'icyarabu:
تَدۡعُواْ مَنۡ أَدۡبَرَ وَتَوَلَّىٰ
Udzaitana (potchula dzina la aliyense) amene adachitembenuzira msana choona ndi kunyoza.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَجَمَعَ فَأَوۡعَىٰٓ
Adasonkhanitsa (chuma) ndi kusunga (m’nkhokwe zake popanda kuperekera chopereka cha Allah).
Ibisobanuro by'icyarabu:
۞ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ خُلِقَ هَلُوعًا
Ndithu munthu walengedwa kukhala wosapirira.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِذَا مَسَّهُ ٱلشَّرُّ جَزُوعٗا
Mavuto akamkhudza amada nkhawa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَإِذَا مَسَّهُ ٱلۡخَيۡرُ مَنُوعًا
Koma zabwino zikamkhudza amamana (ena ndi kuiwala mavuto amene adali nawo).
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِلَّا ٱلۡمُصَلِّينَ
Kupatula opemphera Swala, (iwo alibe mbiri zoipazi).
Ibisobanuro by'icyarabu:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ دَآئِمُونَ
Iwo amene sadukiza mapemphero awo a swala; (sakuwaleka ngakhale zivute chotani).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ فِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ مَّعۡلُومٞ
Ndi amene mchuma chawo muli gawo lodziwika (Zakaat),
Ibisobanuro by'icyarabu:
لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
La wopempha ndi wosapempha.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ يُصَدِّقُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndi amene akuvomereza za tsiku la malipiro (ndi kumalikonzekera.)
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ هُم مِّنۡ عَذَابِ رَبِّهِم مُّشۡفِقُونَ
Ndi iwo amene akuopa chilango chochokera kwa Mbuye wawo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّ عَذَابَ رَبِّهِمۡ غَيۡرُ مَأۡمُونٖ
Ndithu chilango cha Mbuye wawo nchosapulumuka nacho (munthu woipa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِفُرُوجِهِمۡ حَٰفِظُونَ
Ndiponso iwo amene akusunga umaliseche wawo (posachita chiwerewere),
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِلَّا عَلَىٰٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ أَوۡ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ فَإِنَّهُمۡ غَيۡرُ مَلُومِينَ
Kupatula kwa akazi awo ndi amene manja awo akumanja apeza; ndithu pazimenezo iwo sangadzudzulidwe.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَمَنِ ٱبۡتَغَىٰ وَرَآءَ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡعَادُونَ
Koma amene angafune (zina) kusiya zimenezi iwowo ndiwo olumpha malire.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِأَمَٰنَٰتِهِمۡ وَعَهۡدِهِمۡ رَٰعُونَ
Ndi iwo amene amasunga mwaubwino zimene amasungitsidwa ndi zimene alonjeza.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ هُم بِشَهَٰدَٰتِهِمۡ قَآئِمُونَ
Ndi iwo amene amaima molungama popereka umboni wawo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ يُحَافِظُونَ
Ndiponso iwo amene amasunga (mwaubwino) mapemphero awo a swala.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أُوْلَٰٓئِكَ فِي جَنَّٰتٖ مُّكۡرَمُونَ
Amene ali ndi mbiri zimenezi adzakhala m’Minda (yamtendere) ali olemekezedwa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَمَالِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ قِبَلَكَ مُهۡطِعِينَ
Kodi kuli chiyani kwa amene akana (chikhulupiliro) akuthamangira kwa iwe (maso ali pamtunda)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
عَنِ ٱلۡيَمِينِ وَعَنِ ٱلشِّمَالِ عِزِينَ
Atakuzungulira ena chakumanja ena chakumanzere.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَيَطۡمَعُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُدۡخَلَ جَنَّةَ نَعِيمٖ
Kodi akulakalaka aliyense mwa iwo kuti akalowetsedwe ku Munda wamtendere?
Ibisobanuro by'icyarabu:
كَلَّآۖ إِنَّا خَلَقۡنَٰهُم مِّمَّا يَعۡلَمُونَ
Asiye (kukhumba kwawo kokalowa ku Munda wamtendere)! Ndithu Ife tidawalenga kuchokera m’zimene akudziwa (madzi opanda pake).
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِرَبِّ ٱلۡمَشَٰرِقِ وَٱلۡمَغَٰرِبِ إِنَّا لَقَٰدِرُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kuvuma ndi kuzambwe konse ndithu Ndife Wokhoza.
Ibisobanuro by'icyarabu:
عَلَىٰٓ أَن نُّبَدِّلَ خَيۡرٗا مِّنۡهُمۡ وَمَا نَحۡنُ بِمَسۡبُوقِينَ
Kuwasintha ndi kudzetsa abwino kuposa iwo; Ife palibe (chilichonse) chotipambana.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَذَرۡهُمۡ يَخُوضُواْ وَيَلۡعَبُواْ حَتَّىٰ يُلَٰقُواْ يَوۡمَهُمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Asiye azingolankhula zopanda pake ndi kumangosewera mpaka adzakumane ndi tsiku lawo limene akulonjezedwa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَوۡمَ يَخۡرُجُونَ مِنَ ٱلۡأَجۡدَاثِ سِرَاعٗا كَأَنَّهُمۡ إِلَىٰ نُصُبٖ يُوفِضُونَ
Tsiku limene adzatuluke m’manda uku akuthamanga (kudza kwa woitana) ngati kuti akuthamangira kumafano awo (amene adali kuwapembedza).
Ibisobanuro by'icyarabu:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۚ ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلَّذِي كَانُواْ يُوعَدُونَ
Maso awo ali zyoli, (osatha kuwakweza); kuyaluka kutawaphimba! Limenelo ndilo tsiku lomwe adali kulonjezedwa (pomwe adali padziko lapansi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: Almaarij (Inzego)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga