Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Ghaasjijah (Het Overweldigende Evenement)   Vers:

Soerat Al-Ghaasjijah (Het Overweldigende Evenement)

هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡغَٰشِيَةِ
Kodi yakudzera, (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Qiyâma (imene idzaphimba anthu ndi zoopsa zake)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ خَٰشِعَةٌ
Nkhope zina tsiku limenelo, zidzakhala zonyozeka,[425]
[425] Tanthauzo la nkhope apa ndi eni nkhopezo. Amene akunenedwa pamenepa ndi anthu oipa. Allah watchula nkhope chifukwa ndi chiwalo cholemekezeka pa chilengedwe cha munthu ndipo ndi pamene pali chithunzi chake.
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَامِلَةٞ نَّاصِبَةٞ
Zogwira ntchito yotopetsa kwambiri.
Arabische uitleg van de Qur'an:
تَصۡلَىٰ نَارًا حَامِيَةٗ
Zikalowa ku Moto wotentha kwambiri.
Arabische uitleg van de Qur'an:
تُسۡقَىٰ مِنۡ عَيۡنٍ ءَانِيَةٖ
Zikamwetsedwa mu kasupe wotentha kwabasi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَّيۡسَ لَهُمۡ طَعَامٌ إِلَّا مِن ضَرِيعٖ
Sadzakhala ndichakudya koma minga.
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَّا يُسۡمِنُ وَلَا يُغۡنِي مِن جُوعٖ
Yosanenepetsa (thupi) ndiponso yosathetsa njala.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ نَّاعِمَةٞ
Nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zosangalala.
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِّسَعۡيِهَا رَاضِيَةٞ
Zidzakondwera ndi malipiro a zochita zake (za pa dziko lapansi).[426]
[426] Tanthauzo la “kukondweretsedwa ndi zochita zawo’’ ndikuti anthu abwino adzakondwera ndi ntchito zawo zabwino zomwe adazichita pa dziko lapansi akadzakhala ndi malipiro abwino pa tsiku lachimaliziro.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’minda ya pamwamba (Jannah).
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَّا تَسۡمَعُ فِيهَا لَٰغِيَةٗ
Sizikamva m’menemo mawu oipa, (otukwana ndi kulaula).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فِيهَا عَيۡنٞ جَارِيَةٞ
Mmenemo muli kasupe woyenda (mokongola).[427]
[427] (Ndime 12-16) Zosangalatsa zenizeni za tsiku lachimaliziro monga momwe adatiuzira Mneneri (s.a.w) kuti ku Jannah kuli zinthu zimene diso silidapenyepo ngakhale khutu silidamvepo ndipo sizidapitepo m’maganizo a munthu. Choncho zokondweretsa izi zimene Allah watiuza apa akungofanizira ndi zinthu zomwe tikuzidziwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فِيهَا سُرُرٞ مَّرۡفُوعَةٞ
Mmenemo muli makama a pamwamba,
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأَكۡوَابٞ مَّوۡضُوعَةٞ
Ndi zikho zoikidwa bwino (pamaso pawo),
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَنَمَارِقُ مَصۡفُوفَةٞ
Ndi misamiro yoikidwa bwino m’mizeremizere
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَزَرَابِيُّ مَبۡثُوثَةٌ
Ndi mphasa (zamtengo wapatali, carpet) zoyalidwa ponseponse.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَفَلَا يَنظُرُونَ إِلَى ٱلۡإِبِلِ كَيۡفَ خُلِقَتۡ
Kodi (akunyozera kulingalira zisonyezo za Allah), sakulingalira kungamira idalengedwa motani?[428]
[428] (Ndime 17-20) Allah akuwauza kuti ayang’ane chilengedwe cha ngamira, thambo, mapiri ndi nthaka. Pambuyo pake alingalire, aone kuti amene adalenga zimenezo ngotha kuchita chilichonse monga kuukitsa anthu m’manda. Cholinga cha Allah potchula zinthu zimenezi, ngakhale kuti malangizowa nga munthu aliyense, koma adali kuwauza akafiri a pa Makka amene zinthu zimenezi maso awo ankaziona nthawi ndi nthawi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِلَى ٱلسَّمَآءِ كَيۡفَ رُفِعَتۡ
Ndi thambo (limene akuliona nthawi zonse) m’mene lidatukulidwira (kutali popanda mzati)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِلَى ٱلۡجِبَالِ كَيۡفَ نُصِبَتۡ
Ndi mapiri momwe adakhazikitsidwira (molimba)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَيۡفَ سُطِحَتۡ
Ndi nthaka momwe idayalidwira.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَذَكِّرۡ إِنَّمَآ أَنتَ مُذَكِّرٞ
Basi, kumbutsa (anthu) ndithu iwe, ndiwe mkumbutsi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَّسۡتَ عَلَيۡهِم بِمُصَيۡطِرٍ
Sindiwe wokakamiza anthu (kuti akhulupirire).[429]
[429] Ayah iyi ikukwana kuwatsutsa adani a Chisilamu amene akunena kuti, “chipembedzo cha Chisilamu chidafala ndi lupanga.” Kutanthauza kuti ankawakakamiza anthu kuti achivomere chipembedzochi. Sichodabwitsa kuona adani a Chisilamu akuchinyoza chipembedzochi, koma chodabwitsa nchakuti mawu onamawa nkumatulukanso mkamwa mwa anthu omwe amadzitcha kuti ndi Asilamu. Nzoona alipo ena mwa anthu odziwa za chipembedzo (ma Ulama) amene adanena kuti chipembedzo cha Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga. Koma simonga momwe akutanthauzilira adani amene sadziwa za Chisilamu nkumangotsatira mabodza a akuluakulu awo. Cholinga cha ma Ulama ponena kuti “Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga” kumeneko ndi kudziteteza kwa adani omwe adafuna kuchithetsa, osati kuwakakamiza anthu kulowa mchipembedzo. Kukakamiza anthu kulowa mChisilamu nkosaloledwa. Amene akudziwa mbiri ya Chisilamu, akudziwa kuti Asilamu sadalamulidwe kuchita Jihâd mpaka pamene akafiri adali kuwazunza. Pali nkhani zambiri za Maswahaba (otsatira Mneneri) (s.a.w) ku Madina pamene adafuna kuwakakamiza ana awo kulowa m’Chisilamu, koma Mneneri adawakaniza kutero. Basi, munthu amene akunena zoterezo mwina akutero pa chifukwa chosadziwa za chipembedzo cha Chisilamu, mwinanso nkukhala misala basi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِلَّا مَن تَوَلَّىٰ وَكَفَرَ
Koma amene anyoza ndi kukanira (ulaliki wako),
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَيُعَذِّبُهُ ٱللَّهُ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَكۡبَرَ
Allah amulanga chilango chachikulu zedi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّ إِلَيۡنَآ إِيَابَهُمۡ
Ndithu kobwerera kwawo ndi kwa Ife basi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ إِنَّ عَلَيۡنَا حِسَابَهُم
Ndipo ndithu kuwerengedwa kwawo kuli kwa Ife.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Ghaasjijah (Het Overweldigende Evenement)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit