Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-‘Asr   Ayah:

Al-‘Asr

وَٱلۡعَصۡرِ
Ndikuilumbilira nthawi.[480]
[480] Chinthu cha mtengo wapatali kwa munthu pa dziko lino ndi moyo wake. Choncho mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito pa zinthu zabwino ndiyo imene idzamuthandiza. Ndipo mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito mu zinthu zoipa kapena zopanda pake, kumeneko ndiko kutaika kwake; (kuluza).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَفِي خُسۡرٍ
Ndithu munthu aliyense ndi wotaika (chifukwa chakugonjetsedwa ndi zilakolako zake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡحَقِّ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ
Kupatula amene akhulupirira (mwa Allah) ndi kumachita zabwino, ndikumalangizana kutsatira choona ndiponso ndi kumalangizana za kupirira (potsatira malamulo a Allah ndi zina za mdziko).[481]
[481] Mgulu la otaika mwapatulidwa anthu olungama amene zochita zawo zili zolungama, omwe amalamulira kutsatira njira yolungama ndi kupilira. Anthu otere saataika, chifukwa chakuti nthawi yawo amaigwiritsira ntchito pa zinthu zabwino, zowathandiza padziko ndi pambuyo pa imfa. Kupilira kulipo mitundu inayi:-
(a) Kupilira pochita zinthu zabwino zomwe zili zovuta kwa munthu kuzipitiriza, monga kupemphera Swala zisanu.
(b) Kupilira posiya kuchita zoipa zimene zili zovuta kwa munthu kuti azileke.
(c) Kuwapilira anthu anzako; kupilira ndi zoipa zawo posawabwezera choipa chilichonse.
(d) Kupilira ndi mazunzo a padziko, monga njala, matenda, kusauka ndi zina zotero.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-‘Asr
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara