Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Takāthur   Ayah:

At-Takāthur

أَلۡهَىٰكُمُ ٱلتَّكَاثُرُ
Kwakutangwanitsani kusonkhanitsa (chuma chambiri ndi ana).[477]
[477] (Ndime 1-2) Ndi chizolowezi cha anthu kupikisana pa chuma ndi pa ana. Choncho, mma Ayah awa: 1-2 Allah akuwauza: Kupikisana kwawo kochuluka, kukonda za m’dziko kwambiri, kwaiwalitsa kutumikira Allah mpaka imfa kuwapeza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
حَتَّىٰ زُرۡتُمُ ٱلۡمَقَابِرَ
Mpakana mwapita kumanda (mwamwalira ndikukalowa m’manda).
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Sichoncho! Mudziwa posachedwapa.[478]
[478] Tanthauzo lake ndilakuti, pamene idzakufikirani imfa mudzadziwa kuti mudali kutaya nthawi ndi zinthu zopanda pake.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Ndiponso sichoncho! Mudziwa posachedwapa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّا لَوۡ تَعۡلَمُونَ عِلۡمَ ٱلۡيَقِينِ
Sichoncho! mukadakhala mukudziwa, kudziwa kwachitsimikizo (sibwenzi mukutangwanika ndi za mdziko).
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَتَرَوُنَّ ٱلۡجَحِيمَ
Ndithudi mudzauona Moto.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ لَتَرَوُنَّهَا عَيۡنَ ٱلۡيَقِينِ
Kenako mudzauona ndithu ndi diso lachitsimikizo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ لَتُسۡـَٔلُنَّ يَوۡمَئِذٍ عَنِ ٱلنَّعِيمِ
Tsono patsikulo ndithudi mudzafunsidwa za mtendere (omwe munapatsidwa).[479]
[479] Munthu aliyense ndi chilichonse chimene ali nacho ndi mphatso yochokera kwa Allah. Choncho, pa tsiku lachimaliziro adzafunsidwa za momwe adagwiritsira ntchito mphatso zimenezi, kaya m’njira yoipa kapena yabwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Takāthur
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara