அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அத்தகாஸுர்   வசனம்:

ஸூரா அத்தகாஸுர்

أَلۡهَىٰكُمُ ٱلتَّكَاثُرُ
Kwakutangwanitsani kusonkhanitsa (chuma chambiri ndi ana).[477]
[477] (Ndime 1-2) Ndi chizolowezi cha anthu kupikisana pa chuma ndi pa ana. Choncho, mma Ayah awa: 1-2 Allah akuwauza: Kupikisana kwawo kochuluka, kukonda za m’dziko kwambiri, kwaiwalitsa kutumikira Allah mpaka imfa kuwapeza.
அரபு விரிவுரைகள்:
حَتَّىٰ زُرۡتُمُ ٱلۡمَقَابِرَ
Mpakana mwapita kumanda (mwamwalira ndikukalowa m’manda).
அரபு விரிவுரைகள்:
كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Sichoncho! Mudziwa posachedwapa.[478]
[478] Tanthauzo lake ndilakuti, pamene idzakufikirani imfa mudzadziwa kuti mudali kutaya nthawi ndi zinthu zopanda pake.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Ndiponso sichoncho! Mudziwa posachedwapa.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَلَّا لَوۡ تَعۡلَمُونَ عِلۡمَ ٱلۡيَقِينِ
Sichoncho! mukadakhala mukudziwa, kudziwa kwachitsimikizo (sibwenzi mukutangwanika ndi za mdziko).
அரபு விரிவுரைகள்:
لَتَرَوُنَّ ٱلۡجَحِيمَ
Ndithudi mudzauona Moto.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ لَتَرَوُنَّهَا عَيۡنَ ٱلۡيَقِينِ
Kenako mudzauona ndithu ndi diso lachitsimikizo.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ لَتُسۡـَٔلُنَّ يَوۡمَئِذٍ عَنِ ٱلنَّعِيمِ
Tsono patsikulo ndithudi mudzafunsidwa za mtendere (omwe munapatsidwa).[479]
[479] Munthu aliyense ndi chilichonse chimene ali nacho ndi mphatso yochokera kwa Allah. Choncho, pa tsiku lachimaliziro adzafunsidwa za momwe adagwiritsira ntchito mphatso zimenezi, kaya m’njira yoipa kapena yabwino.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அத்தகாஸுர்
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக