Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: At-Takâthur   Versetto:

At-Takâthur

أَلۡهَىٰكُمُ ٱلتَّكَاثُرُ
Kwakutangwanitsani kusonkhanitsa (chuma chambiri ndi ana).[477]
[477] (Ndime 1-2) Ndi chizolowezi cha anthu kupikisana pa chuma ndi pa ana. Choncho, mma Ayah awa: 1-2 Allah akuwauza: Kupikisana kwawo kochuluka, kukonda za m’dziko kwambiri, kwaiwalitsa kutumikira Allah mpaka imfa kuwapeza.
Esegesi in lingua araba:
حَتَّىٰ زُرۡتُمُ ٱلۡمَقَابِرَ
Mpakana mwapita kumanda (mwamwalira ndikukalowa m’manda).
Esegesi in lingua araba:
كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Sichoncho! Mudziwa posachedwapa.[478]
[478] Tanthauzo lake ndilakuti, pamene idzakufikirani imfa mudzadziwa kuti mudali kutaya nthawi ndi zinthu zopanda pake.
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Ndiponso sichoncho! Mudziwa posachedwapa.
Esegesi in lingua araba:
كَلَّا لَوۡ تَعۡلَمُونَ عِلۡمَ ٱلۡيَقِينِ
Sichoncho! mukadakhala mukudziwa, kudziwa kwachitsimikizo (sibwenzi mukutangwanika ndi za mdziko).
Esegesi in lingua araba:
لَتَرَوُنَّ ٱلۡجَحِيمَ
Ndithudi mudzauona Moto.
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ لَتَرَوُنَّهَا عَيۡنَ ٱلۡيَقِينِ
Kenako mudzauona ndithu ndi diso lachitsimikizo.
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ لَتُسۡـَٔلُنَّ يَوۡمَئِذٍ عَنِ ٱلنَّعِيمِ
Tsono patsikulo ndithudi mudzafunsidwa za mtendere (omwe munapatsidwa).[479]
[479] Munthu aliyense ndi chilichonse chimene ali nacho ndi mphatso yochokera kwa Allah. Choncho, pa tsiku lachimaliziro adzafunsidwa za momwe adagwiritsira ntchito mphatso zimenezi, kaya m’njira yoipa kapena yabwino.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: At-Takâthur
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi