Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: Al-Qâri‘ah   Versetto:

Al-Qâri‘ah

ٱلۡقَارِعَةُ
Kugunda kwa phokoso (la Qiyâma)!
Esegesi in lingua araba:
مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Kodi kugunda kwa phokosolo ndi chiyani?
Esegesi in lingua araba:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Ndichiyani chingakudziwitse za kugunda kwa phokoso (la Qiyâma komwe kudzawakomole anthu)?
Esegesi in lingua araba:
يَوۡمَ يَكُونُ ٱلنَّاسُ كَٱلۡفَرَاشِ ٱلۡمَبۡثُوثِ
Limenelo ndi tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika.[475]
[475] Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi yotuluka m’manda.
Esegesi in lingua araba:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ ٱلۡمَنفُوشِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya womwazidwa (wongouluka uku ndi uku mumlengalenga).
Esegesi in lingua araba:
فَأَمَّا مَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Tsono amene muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzalemere (ndikupepuka zoipa).[476]
[476] Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso wa Allah, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani udzayesa zonse zazikulu ndi zazing’ono zomwe mpaka za mumtima.
Esegesi in lingua araba:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Ndiye kuti iye adzakhala mu umoyo wosangalatsa (patsiku la chiweruziro).
Esegesi in lingua araba:
وَأَمَّا مَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Ndipo yemwe muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzapepuka (ndi kulemera zoipa),
Esegesi in lingua araba:
فَأُمُّهُۥ هَاوِيَةٞ
Ndiye kuti mbuto yake ndi ku Hawiya.
Esegesi in lingua araba:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا هِيَهۡ
Kodi ndi chiyani chingakudziwitse za Hawiya?
Esegesi in lingua araba:
نَارٌ حَامِيَةُۢ
Umenewo ndi Moto woyaka mwa ukali!
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: Al-Qâri‘ah
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi