কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ * - অনুবাদসমূহের সূচী


অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আল-কারিআহ   আয়াত:

সূরা আল-কারিআহ

ٱلۡقَارِعَةُ
Kugunda kwa phokoso (la Qiyâma)!
আরবি তাফসীরসমূহ:
مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Kodi kugunda kwa phokosolo ndi chiyani?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Ndichiyani chingakudziwitse za kugunda kwa phokoso (la Qiyâma komwe kudzawakomole anthu)?
আরবি তাফসীরসমূহ:
يَوۡمَ يَكُونُ ٱلنَّاسُ كَٱلۡفَرَاشِ ٱلۡمَبۡثُوثِ
Limenelo ndi tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika.[475]
[475] Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi yotuluka m’manda.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ ٱلۡمَنفُوشِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya womwazidwa (wongouluka uku ndi uku mumlengalenga).
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَأَمَّا مَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Tsono amene muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzalemere (ndikupepuka zoipa).[476]
[476] Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso wa Allah, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani udzayesa zonse zazikulu ndi zazing’ono zomwe mpaka za mumtima.
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Ndiye kuti iye adzakhala mu umoyo wosangalatsa (patsiku la chiweruziro).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَأَمَّا مَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Ndipo yemwe muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzapepuka (ndi kulemera zoipa),
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَأُمُّهُۥ هَاوِيَةٞ
Ndiye kuti mbuto yake ndi ku Hawiya.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا هِيَهۡ
Kodi ndi chiyani chingakudziwitse za Hawiya?
আরবি তাফসীরসমূহ:
نَارٌ حَامِيَةُۢ
Umenewo ndi Moto woyaka mwa ukali!
আরবি তাফসীরসমূহ:
 
অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আল-কারিআহ
সূরাসমূহের সূচী পৃষ্ঠার নাম্বার
 
কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ - অনুবাদসমূহের সূচী

চেওয়া ভাষা আল-কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ-খালিদ ইবরাহীম বীতালা, সংস্করণ ২০২০ খ্রি.

বন্ধ