クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 章: 大打撃章   節:

大打撃章

ٱلۡقَارِعَةُ
Kugunda kwa phokoso (la Qiyâma)!
アラビア語 クルアーン注釈:
مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Kodi kugunda kwa phokosolo ndi chiyani?
アラビア語 クルアーン注釈:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Ndichiyani chingakudziwitse za kugunda kwa phokoso (la Qiyâma komwe kudzawakomole anthu)?
アラビア語 クルアーン注釈:
يَوۡمَ يَكُونُ ٱلنَّاسُ كَٱلۡفَرَاشِ ٱلۡمَبۡثُوثِ
Limenelo ndi tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika.[475]
[475] Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi yotuluka m’manda.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ ٱلۡمَنفُوشِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya womwazidwa (wongouluka uku ndi uku mumlengalenga).
アラビア語 クルアーン注釈:
فَأَمَّا مَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Tsono amene muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzalemere (ndikupepuka zoipa).[476]
[476] Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso wa Allah, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani udzayesa zonse zazikulu ndi zazing’ono zomwe mpaka za mumtima.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Ndiye kuti iye adzakhala mu umoyo wosangalatsa (patsiku la chiweruziro).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَأَمَّا مَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Ndipo yemwe muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzapepuka (ndi kulemera zoipa),
アラビア語 クルアーン注釈:
فَأُمُّهُۥ هَاوِيَةٞ
Ndiye kuti mbuto yake ndi ku Hawiya.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا هِيَهۡ
Kodi ndi chiyani chingakudziwitse za Hawiya?
アラビア語 クルアーン注釈:
نَارٌ حَامِيَةُۢ
Umenewo ndi Moto woyaka mwa ukali!
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 章: 大打撃章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる