《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 章: 嘎勒尔   段:

嘎勒尔

ٱلۡقَارِعَةُ
Kugunda kwa phokoso (la Qiyâma)!
阿拉伯语经注:
مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Kodi kugunda kwa phokosolo ndi chiyani?
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Ndichiyani chingakudziwitse za kugunda kwa phokoso (la Qiyâma komwe kudzawakomole anthu)?
阿拉伯语经注:
يَوۡمَ يَكُونُ ٱلنَّاسُ كَٱلۡفَرَاشِ ٱلۡمَبۡثُوثِ
Limenelo ndi tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika.[475]
[475] Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi yotuluka m’manda.
阿拉伯语经注:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ ٱلۡمَنفُوشِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya womwazidwa (wongouluka uku ndi uku mumlengalenga).
阿拉伯语经注:
فَأَمَّا مَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Tsono amene muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzalemere (ndikupepuka zoipa).[476]
[476] Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso wa Allah, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani udzayesa zonse zazikulu ndi zazing’ono zomwe mpaka za mumtima.
阿拉伯语经注:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Ndiye kuti iye adzakhala mu umoyo wosangalatsa (patsiku la chiweruziro).
阿拉伯语经注:
وَأَمَّا مَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Ndipo yemwe muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzapepuka (ndi kulemera zoipa),
阿拉伯语经注:
فَأُمُّهُۥ هَاوِيَةٞ
Ndiye kuti mbuto yake ndi ku Hawiya.
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا هِيَهۡ
Kodi ndi chiyani chingakudziwitse za Hawiya?
阿拉伯语经注:
نَارٌ حَامِيَةُۢ
Umenewo ndi Moto woyaka mwa ukali!
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 嘎勒尔
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭