Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 泰开苏尔   段:

At-Takâthur

أَلۡهَىٰكُمُ ٱلتَّكَاثُرُ
Kwakutangwanitsani kusonkhanitsa (chuma chambiri ndi ana).[477]
[477] (Ndime 1-2) Ndi chizolowezi cha anthu kupikisana pa chuma ndi pa ana. Choncho, mma Ayah awa: 1-2 Allah akuwauza: Kupikisana kwawo kochuluka, kukonda za m’dziko kwambiri, kwaiwalitsa kutumikira Allah mpaka imfa kuwapeza.
阿拉伯语经注:
حَتَّىٰ زُرۡتُمُ ٱلۡمَقَابِرَ
Mpakana mwapita kumanda (mwamwalira ndikukalowa m’manda).
阿拉伯语经注:
كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Sichoncho! Mudziwa posachedwapa.[478]
[478] Tanthauzo lake ndilakuti, pamene idzakufikirani imfa mudzadziwa kuti mudali kutaya nthawi ndi zinthu zopanda pake.
阿拉伯语经注:
ثُمَّ كَلَّا سَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Ndiponso sichoncho! Mudziwa posachedwapa.
阿拉伯语经注:
كَلَّا لَوۡ تَعۡلَمُونَ عِلۡمَ ٱلۡيَقِينِ
Sichoncho! mukadakhala mukudziwa, kudziwa kwachitsimikizo (sibwenzi mukutangwanika ndi za mdziko).
阿拉伯语经注:
لَتَرَوُنَّ ٱلۡجَحِيمَ
Ndithudi mudzauona Moto.
阿拉伯语经注:
ثُمَّ لَتَرَوُنَّهَا عَيۡنَ ٱلۡيَقِينِ
Kenako mudzauona ndithu ndi diso lachitsimikizo.
阿拉伯语经注:
ثُمَّ لَتُسۡـَٔلُنَّ يَوۡمَئِذٍ عَنِ ٱلنَّعِيمِ
Tsono patsikulo ndithudi mudzafunsidwa za mtendere (omwe munapatsidwa).[479]
[479] Munthu aliyense ndi chilichonse chimene ali nacho ndi mphatso yochokera kwa Allah. Choncho, pa tsiku lachimaliziro adzafunsidwa za momwe adagwiritsira ntchito mphatso zimenezi, kaya m’njira yoipa kapena yabwino.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 泰开苏尔
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭