Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Сура: Қалам сураси   Оят:

Қалам сураси

نٓۚ وَٱلۡقَلَمِ وَمَا يَسۡطُرُونَ
Nûn. Ndikulumbilira cholembera (chimene akulembera angelo), ndi zimene amalemba.
Арабча тафсирлар:
مَآ أَنتَ بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ بِمَجۡنُونٖ
Pa chisomo cha Mbuye wako iwe sindiwe wamisala (pokupatsa uneneri).
Арабча тафсирлар:
وَإِنَّ لَكَ لَأَجۡرًا غَيۡرَ مَمۡنُونٖ
Ndipo ndithu udzakhala ndi malipiro akulu osaduka, (onkerankera mtsogolo chifukwa cha mavuto amene ukukumana nawo pofikitsa uthenga).
Арабча тафсирлар:
وَإِنَّكَ لَعَلَىٰ خُلُقٍ عَظِيمٖ
Ndipo ndithu uli nawo makhalidwe abwino kwambiri (omwe Allah adakulenga nawo).
Арабча тафсирлар:
فَسَتُبۡصِرُ وَيُبۡصِرُونَ
Basi, posachedwapa uona, iwonso aona.
Арабча тафсирлар:
بِأَييِّكُمُ ٱلۡمَفۡتُونُ
Kuti ndani mwa inu wamisala (iwe kapena iwo)?
Арабча тафсирлар:
إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu Mbuye wako akum’dziwa bwino amene wasokera panjira yake. Ndiponso akuwadziwa bwino amene ali oongoka.
Арабча тафсирлар:
فَلَا تُطِعِ ٱلۡمُكَذِّبِينَ
Choncho, usawamvere otsutsa; (usasiye zimene uli nazo ngakhale sakugwirizana nazo).
Арабча тафсирлар:
وَدُّواْ لَوۡ تُدۡهِنُ فَيُدۡهِنُونَ
Akufuna kuti ukadakhala wofewa kwa iwo (pa zinthu zina) nawo akadakhala ofewa (kwa iwe).
Арабча тафсирлар:
وَلَا تُطِعۡ كُلَّ حَلَّافٖ مَّهِينٍ
Ndipo usamumvere aliyense wochulukitsa kulumbira, woyaluka.
Арабча тафсирлар:
هَمَّازٖ مَّشَّآءِۭ بِنَمِيمٖ
Wojeda, woyenda ndi ukazitape (ndi cholinga choononga umodzi wawo).
Арабча тафсирлар:
مَّنَّاعٖ لِّلۡخَيۡرِ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Wotsekereza zabwino, wamtopola, wamachimo ambiri.
Арабча тафсирлар:
عُتُلِّۭ بَعۡدَ ذَٰلِكَ زَنِيمٍ
Wouma mtima; pamwamba pa izi ndi wodzipachika mu mtundu wa ena (pomwe iye sali m’menemo).
Арабча тафсирлар:
أَن كَانَ ذَا مَالٖ وَبَنِينَ
Chifukwa choti iye ndi mwini chuma ndi ana (ndi zimene ali kunyadira).
Арабча тафсирлар:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Zikawerengedwa kwa iye Ayah Zathu amanena: “Izi ndi nthano za akale (ndi zabodza zawo, zopeka).”
Арабча тафсирлар:
سَنَسِمُهُۥ عَلَى ٱلۡخُرۡطُومِ
Timuika pamphuno pake chizindikiro (chosasiyana nacho kuti ayaluke nacho pamaso pa anthu).
Арабча тафсирлар:
إِنَّا بَلَوۡنَٰهُمۡ كَمَا بَلَوۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡجَنَّةِ إِذۡ أَقۡسَمُواْ لَيَصۡرِمُنَّهَا مُصۡبِحِينَ
Ndithu ife tidawayesa (eni mzinda wa Makka ndi mtendere omwe udali pa iwo, koma adakana monga) momwe tidawayesera eni munda, pamene adalumbira kuti akathyola (zipatso za m’munda wawozo) mbandakucha (kuti osauka asawaone angawapemphe).
Арабча тафсирлар:
وَلَا يَسۡتَثۡنُونَ
Ndipo sadapatule (ngakhale wosauka ndi m’modzi yemwe ponena kuti uje timpatse, uje tisampatse, kapena sadanene kuti: “Ngati Allah afuna).”
Арабча тафсирлар:
فَطَافَ عَلَيۡهَا طَآئِفٞ مِّن رَّبِّكَ وَهُمۡ نَآئِمُونَ
Mliri woopsa wochokera kwa Mbuye wako udauzinga (mundawo nthawi yausiku) iwo ali mtulo.
Арабча тафсирлар:
فَأَصۡبَحَتۡ كَٱلصَّرِيمِ
Choncho udakhala ngati wokololedwa (chifukwa cha mliri uja).
Арабча тафсирлар:
فَتَنَادَوۡاْ مُصۡبِحِينَ
Tero adaitanizana nthawi ya mbandakucha.
Арабча тафсирлар:
أَنِ ٱغۡدُواْ عَلَىٰ حَرۡثِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰرِمِينَ
“Lawilirani kumunda wanu kuja ngati mukufuna kukolola (kuopera kuti angakuoneni osauka).”
Арабча тафсирлар:
فَٱنطَلَقُواْ وَهُمۡ يَتَخَٰفَتُونَ
Adanyamuka uku akunong’ onezana.
Арабча тафсирлар:
أَن لَّا يَدۡخُلَنَّهَا ٱلۡيَوۡمَ عَلَيۡكُم مِّسۡكِينٞ
(Akunena kuti): “Asakulowelereni wosauka lero mmenemo.”
Арабча тафсирлар:
وَغَدَوۡاْ عَلَىٰ حَرۡدٖ قَٰدِرِينَ
Ndipo adalawilira ali ndi chitsimikizo choti atha kuwamana (osauka).
Арабча тафсирлар:
فَلَمَّا رَأَوۡهَا قَالُوٓاْ إِنَّا لَضَآلُّونَ
Choncho pamene adauona, adanena (uku akunjenjemera): “Ndithu ife tasokera (sikuno ayi, munda wathu uja siuno).”
Арабча тафсирлар:
بَلۡ نَحۡنُ مَحۡرُومُونَ
“Iyayi, ndiwomwewu; koma tamanidwa zinthu zake.”
Арабча тафсирлар:
قَالَ أَوۡسَطُهُمۡ أَلَمۡ أَقُل لَّكُمۡ لَوۡلَا تُسَبِّحُونَ
Wolungama mwa iwo adanena: “Kodi sindinakuuzeni (pamene mudali kulangizana zomana osowa) kuti bwanji osamkumbukira Allah (ndi kusintha cholinga chanu)?”
Арабча тафсирлар:
قَالُواْ سُبۡحَٰنَ رَبِّنَآ إِنَّا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Iwo) adanena: “Alemekezeke Mbuye wathu ndithu ife tidali achinyengo (chifukwa cha kuipa kwa cholinga chathu).”
Арабча тафсирлар:
فَأَقۡبَلَ بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ يَتَلَٰوَمُونَ
Ndipo adatembenukirana ndikuyamba kudzudzulana.
Арабча тафсирлар:
قَالُواْ يَٰوَيۡلَنَآ إِنَّا كُنَّا طَٰغِينَ
Adati: “E chionongeko chathu! Ndithu Ife tidapyola malire (m’chinyengo chathu).”
Арабча тафсирлар:
عَسَىٰ رَبُّنَآ أَن يُبۡدِلَنَا خَيۡرٗا مِّنۡهَآ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا رَٰغِبُونَ
“Mwina Mbuye wathu angatipatse zabwino m’malo mwa munda wathuwu. Ndithu ife tikufunitsitsa kwa Mbuye wathu (chikhululuko Chake).”
Арабча тафсирлар:
كَذَٰلِكَ ٱلۡعَذَابُۖ وَلَعَذَابُ ٱلۡأٓخِرَةِ أَكۡبَرُۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Umo ndi mmene chimakhalira chilango (Changa chomwe ndimachitsitsa pa dziko lapansi kwa amene chamuyenera); koma chilango cha tsiku lachimaliziro nchachikulu zedi, akadakhala akudziwa.
Арабча тафсирлар:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ عِندَ رَبِّهِمۡ جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
Ndithu oopa Allah adzakhala ndi Minda ya mtendere kwa Mbuye wawo.
Арабча тафсирлар:
أَفَنَجۡعَلُ ٱلۡمُسۡلِمِينَ كَٱلۡمُجۡرِمِينَ
Kodi tiwachite Asilamu monga ochimwa.
Арабча тафсирлар:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani! Nanga mukuweruza bwanji (maweruzo opanda chilungamo)?
Арабча тафсирлар:
أَمۡ لَكُمۡ كِتَٰبٞ فِيهِ تَدۡرُسُونَ
Kapena muli ndi buku limene mukuwerenga.
Арабча тафсирлар:
إِنَّ لَكُمۡ فِيهِ لَمَا تَخَيَّرُونَ
Kuti ndithu mulinazo mmenemo zomwe mukudzisankhira.
Арабча тафсирлар:
أَمۡ لَكُمۡ أَيۡمَٰنٌ عَلَيۡنَا بَٰلِغَةٌ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ إِنَّ لَكُمۡ لَمَا تَحۡكُمُونَ
Kapena muli nawo mapangano ndi Ife okafika mpaka tsiku lachimaliziro akuti inu mudzapeza zimene mukudziweruzira?
Арабча тафсирлар:
سَلۡهُمۡ أَيُّهُم بِذَٰلِكَ زَعِيمٌ
Afunse (iwe Mtumiki) ndani mwa iwo amene ali mtsogoleri (pa malamulo amenewa)?
Арабча тафсирлар:
أَمۡ لَهُمۡ شُرَكَآءُ فَلۡيَأۡتُواْ بِشُرَكَآئِهِمۡ إِن كَانُواْ صَٰدِقِينَ
Kapena iwo ali nawo othandidzana nawo (pa mau awa)? Chomwecho atabweretsa othandizana nawo ngati akunena zowona!
Арабча тафсирлар:
يَوۡمَ يُكۡشَفُ عَن سَاقٖ وَيُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ فَلَا يَسۡتَطِيعُونَ
(Akumbukire) tsiku la mavuto okhwima, ndipo adzaitanidwa (akafiri) kuti achite sijida (polambira Allah) koma sadzatha.
Арабча тафсирлар:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۖ وَقَدۡ كَانُواْ يُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ وَهُمۡ سَٰلِمُونَ
Maso awo adzangoti pansi zyoli, manyazi ndi kunyozeka kudzawaphimba; chikhalirecho adali kuitanidwa (pa dziko lapansi) kuti agwetse nkhope pansi pomwe iwo adali ndi moyo wa ngwiro (koma ankakana).
Арабча тафсирлар:
فَذَرۡنِي وَمَن يُكَذِّبُ بِهَٰذَا ٱلۡحَدِيثِۖ سَنَسۡتَدۡرِجُهُم مِّنۡ حَيۡثُ لَا يَعۡلَمُونَ
Choncho ndisiye, (iwe Mtumiki), ndi amene akukanira nkhani iyi tiwakokera kuchilango pang’onopang’ono pamene iwo sakudziwa (mmene chiti chiwadzere chilangochi).
Арабча тафсирлар:
وَأُمۡلِي لَهُمۡۚ إِنَّ كَيۡدِي مَتِينٌ
Ndipo ndikuwalekelera (pochedwetsa chilango); ndithudi makonzedwe Anga ngokhwima, (palibe angapulumuke mmenemo).
Арабча тафсирлар:
أَمۡ تَسۡـَٔلُهُمۡ أَجۡرٗا فَهُم مِّن مَّغۡرَمٖ مُّثۡقَلُونَ
Kapena ukuwapempha malipiro (pofikitsa uthenga) kotero kuti iwo akulemedwa ndi kulipira?
Арабча тафсирлар:
أَمۡ عِندَهُمُ ٱلۡغَيۡبُ فَهُمۡ يَكۡتُبُونَ
Kapena ali nazo (nzeru) zobisika kotero kuti iwo akulemba (zimene akuweruzazo)!
Арабча тафсирлар:
فَٱصۡبِرۡ لِحُكۡمِ رَبِّكَ وَلَا تَكُن كَصَاحِبِ ٱلۡحُوتِ إِذۡ نَادَىٰ وَهُوَ مَكۡظُومٞ
Choncho pirira ndi lamulo la Mbuye wako (chifukwa chowalekelera ndi kuchedwetsa chipulumutso chako); ndipo usakhale ngati mwini nsomba (Yunusu pa changu ndi mkwiyo kwa anthu ake) pamene adaitana (Mbuye wake) uku ali wodzazidwa ndi mkwiyo (kupempha kuti chidze mwachangu chilango kwa anthu ake).
Арабча тафсирлар:
لَّوۡلَآ أَن تَدَٰرَكَهُۥ نِعۡمَةٞ مِّن رَّبِّهِۦ لَنُبِذَ بِٱلۡعَرَآءِ وَهُوَ مَذۡمُومٞ
Chikadapanda kumfikira chisomo chochokera kwa Mbuye wake (ndi kuvomera kulapa kwake), akadaponyedwa (kuchokera m’mimba mwa chinsomba chija) pagombe (popanda kanthu) ali wodzudzulidwa.
Арабча тафсирлар:
فَٱجۡتَبَٰهُ رَبُّهُۥ فَجَعَلَهُۥ مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Koma adamsankha Mbuye wake (povomera kulapa kwake) ndipo adamchita kukhala mmodzi wa anthu abwino.
Арабча тафсирлар:
وَإِن يَكَادُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَيُزۡلِقُونَكَ بِأَبۡصَٰرِهِمۡ لَمَّا سَمِعُواْ ٱلذِّكۡرَ وَيَقُولُونَ إِنَّهُۥ لَمَجۡنُونٞ
Ndithudi anthu amene sadakhulupirire adayandikira kukuteleretsa ndi kunyogodola kwa maso awo (chifukwa chachidani ndi mkwiyo) pamene adamva chikumbutso (Qur’an), ndipo akunena kuti iyeyo ngwamisala.
Арабча тафсирлар:
وَمَا هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo ichi sichina, koma (ndi phunziro, ndi nzeru) ndi chikumbutso kwa zolengedwa zonse.
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Сура: Қалам сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш