Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Сура: Лайл сураси   Оят:

Лайл сураси

وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰ
Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse).
Арабча тафсирлар:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ
Ndi usana pamene kukuyera.
Арабча тафсирлар:
وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ
Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi.
Арабча тафсирлар:
إِنَّ سَعۡيَكُمۡ لَشَتَّىٰ
Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446]
[446] Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi ndi kutumikira Allah. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.
Арабча тафсирлар:
فَأَمَّا مَنۡ أَعۡطَىٰ وَٱتَّقَىٰ
Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447]
[447] Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m’njira ya Allah ndiponso kwa anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.
Арабча тафсирлар:
وَصَدَّقَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448]
[448] Tanthauzo la “Kuvomereza zinthu zabwino” ndiko kugwirizana nazo zimene Allah walamula, chifukwa chakuti Iye amalamula zinthu zabwino zokhazokha ndikuletsa zoipa.
Арабча тафсирлар:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡيُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449]
[449] Tanthauzo la Ayah imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza mtendere mu mtima mwake.
Арабча тафсирлар:
وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana;
Арабча тафсирлар:
وَكَذَّبَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndi kumatsutsa zinthu zabwino,
Арабча тафсирлар:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡعُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku mavuto (a muyaya).
Арабча тафсирлар:
وَمَا يُغۡنِي عَنۡهُ مَالُهُۥٓ إِذَا تَرَدَّىٰٓ
Ndipo chuma chake sichidzamthandiza (chilichonse) akadzagwera ku Moto.
Арабча тафсирлар:
إِنَّ عَلَيۡنَا لَلۡهُدَىٰ
Ndithu Ife ndi amene timawalongosolera anthu njira yabwino ndi njira yoipa.
Арабча тафсирлар:
وَإِنَّ لَنَا لَلۡأٓخِرَةَ وَٱلۡأُولَىٰ
Ndipo ndithu moyo womaliza ndi moyo woyamba uli m’manja mwathu.
Арабча тафсирлар:
فَأَنذَرۡتُكُمۡ نَارٗا تَلَظَّىٰ
Basi, ndikukuchenjezani za Moto woyaka mwa mphamvu.
Арабча тафсирлар:
لَا يَصۡلَىٰهَآ إِلَّا ٱلۡأَشۡقَى
Sakaulowa koma (kafiri) woipitsitsa kwambiri.
Арабча тафсирлар:
ٱلَّذِي كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
Yemwe amatsutsa (choona) ndi kunyoza (zisonyezo za Allah).
Арабча тафсирлар:
وَسَيُجَنَّبُهَا ٱلۡأَتۡقَى
Koma yemwe akuopa Allah kwambiri akatalikitsidwa ndi Moto.
Арабча тафсирлар:
ٱلَّذِي يُؤۡتِي مَالَهُۥ يَتَزَكَّىٰ
Amene akupereka chuma chake ndi cholinga chodziyeretsa.
Арабча тафсирлар:
وَمَا لِأَحَدٍ عِندَهُۥ مِن نِّعۡمَةٖ تُجۡزَىٰٓ
Ndipo palibe aliyense kwa iye, amene adamchitira za chifundo zomwe zikulipidwa.[450]
[450] (Ndime 19-20)Tanthauzo la ma Ayah awiriwa nkuti munthu uyu sakupereka chuma chake chifukwa chobwezera chifundo cha anthu, kapena kuti adzamubwezerenso iye chifundo, koma akupereka chifukwa chofuna chikondi cha Mbuye wake basi.
Арабча тафсирлар:
إِلَّا ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Koma (akuchita zimenezi) kufuna chikondi cha Mbuye wake Wapamwambamwamba.
Арабча тафсирлар:
وَلَسَوۡفَ يَرۡضَىٰ
Ndipo posachedwa adzasangalala.[451]
[451] Tanthauzo lake apa ndikuti Allah adzamukondweretsa ndi malipiro Ake abwino kufikira munthuyo adzakondwera. Ma Ayah, kuyambira 17 mpaka 21, adatsika chifukwa cha Sayyidina Abu Bakr (r.a) yemwe adali kupereka chuma chake powagula akapolo omwe adali kuzunzidwa ndi mabwana awo chifukwa cholowa Chisilamu, pambuyo pake amawapatsa ufulu. Ndipo m’modzi wa iwowa ndi Sayyidina Bilal (r.a) amene adali Muazzini wa Mneneri Muhammad (s.a.w). Chomwechonso Ayah zimenezi zikumkhudza aliyense amene akugwiritsa ntchito chuma chake mnjira yopulumutsira chipembedzo.
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Сура: Лайл сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш