Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: Sura el-Lejl   Ajet:

Sura el-Lejl

وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰ
Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ
Ndi usana pamene kukuyera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ
Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ سَعۡيَكُمۡ لَشَتَّىٰ
Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446]
[446] Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi ndi kutumikira Allah. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَأَمَّا مَنۡ أَعۡطَىٰ وَٱتَّقَىٰ
Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447]
[447] Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m’njira ya Allah ndiponso kwa anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَصَدَّقَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448]
[448] Tanthauzo la “Kuvomereza zinthu zabwino” ndiko kugwirizana nazo zimene Allah walamula, chifukwa chakuti Iye amalamula zinthu zabwino zokhazokha ndikuletsa zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡيُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449]
[449] Tanthauzo la Ayah imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza mtendere mu mtima mwake.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana;
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَكَذَّبَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndi kumatsutsa zinthu zabwino,
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡعُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku mavuto (a muyaya).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَا يُغۡنِي عَنۡهُ مَالُهُۥٓ إِذَا تَرَدَّىٰٓ
Ndipo chuma chake sichidzamthandiza (chilichonse) akadzagwera ku Moto.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ عَلَيۡنَا لَلۡهُدَىٰ
Ndithu Ife ndi amene timawalongosolera anthu njira yabwino ndi njira yoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِنَّ لَنَا لَلۡأٓخِرَةَ وَٱلۡأُولَىٰ
Ndipo ndithu moyo womaliza ndi moyo woyamba uli m’manja mwathu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَأَنذَرۡتُكُمۡ نَارٗا تَلَظَّىٰ
Basi, ndikukuchenjezani za Moto woyaka mwa mphamvu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَا يَصۡلَىٰهَآ إِلَّا ٱلۡأَشۡقَى
Sakaulowa koma (kafiri) woipitsitsa kwambiri.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِي كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
Yemwe amatsutsa (choona) ndi kunyoza (zisonyezo za Allah).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَسَيُجَنَّبُهَا ٱلۡأَتۡقَى
Koma yemwe akuopa Allah kwambiri akatalikitsidwa ndi Moto.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِي يُؤۡتِي مَالَهُۥ يَتَزَكَّىٰ
Amene akupereka chuma chake ndi cholinga chodziyeretsa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَا لِأَحَدٍ عِندَهُۥ مِن نِّعۡمَةٖ تُجۡزَىٰٓ
Ndipo palibe aliyense kwa iye, amene adamchitira za chifundo zomwe zikulipidwa.[450]
[450] (Ndime 19-20)Tanthauzo la ma Ayah awiriwa nkuti munthu uyu sakupereka chuma chake chifukwa chobwezera chifundo cha anthu, kapena kuti adzamubwezerenso iye chifundo, koma akupereka chifukwa chofuna chikondi cha Mbuye wake basi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِلَّا ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Koma (akuchita zimenezi) kufuna chikondi cha Mbuye wake Wapamwambamwamba.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَسَوۡفَ يَرۡضَىٰ
Ndipo posachedwa adzasangalala.[451]
[451] Tanthauzo lake apa ndikuti Allah adzamukondweretsa ndi malipiro Ake abwino kufikira munthuyo adzakondwera. Ma Ayah, kuyambira 17 mpaka 21, adatsika chifukwa cha Sayyidina Abu Bakr (r.a) yemwe adali kupereka chuma chake powagula akapolo omwe adali kuzunzidwa ndi mabwana awo chifukwa cholowa Chisilamu, pambuyo pake amawapatsa ufulu. Ndipo m’modzi wa iwowa ndi Sayyidina Bilal (r.a) amene adali Muazzini wa Mneneri Muhammad (s.a.w). Chomwechonso Ayah zimenezi zikumkhudza aliyense amene akugwiritsa ntchito chuma chake mnjira yopulumutsira chipembedzo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: Sura el-Lejl
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje