《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 章: 莱仪拉   段:

莱仪拉

وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰ
Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse).
阿拉伯语经注:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ
Ndi usana pamene kukuyera.
阿拉伯语经注:
وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ
Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi.
阿拉伯语经注:
إِنَّ سَعۡيَكُمۡ لَشَتَّىٰ
Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446]
[446] Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi ndi kutumikira Allah. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.
阿拉伯语经注:
فَأَمَّا مَنۡ أَعۡطَىٰ وَٱتَّقَىٰ
Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447]
[447] Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m’njira ya Allah ndiponso kwa anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.
阿拉伯语经注:
وَصَدَّقَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448]
[448] Tanthauzo la “Kuvomereza zinthu zabwino” ndiko kugwirizana nazo zimene Allah walamula, chifukwa chakuti Iye amalamula zinthu zabwino zokhazokha ndikuletsa zoipa.
阿拉伯语经注:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡيُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449]
[449] Tanthauzo la Ayah imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza mtendere mu mtima mwake.
阿拉伯语经注:
وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana;
阿拉伯语经注:
وَكَذَّبَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndi kumatsutsa zinthu zabwino,
阿拉伯语经注:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡعُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku mavuto (a muyaya).
阿拉伯语经注:
وَمَا يُغۡنِي عَنۡهُ مَالُهُۥٓ إِذَا تَرَدَّىٰٓ
Ndipo chuma chake sichidzamthandiza (chilichonse) akadzagwera ku Moto.
阿拉伯语经注:
إِنَّ عَلَيۡنَا لَلۡهُدَىٰ
Ndithu Ife ndi amene timawalongosolera anthu njira yabwino ndi njira yoipa.
阿拉伯语经注:
وَإِنَّ لَنَا لَلۡأٓخِرَةَ وَٱلۡأُولَىٰ
Ndipo ndithu moyo womaliza ndi moyo woyamba uli m’manja mwathu.
阿拉伯语经注:
فَأَنذَرۡتُكُمۡ نَارٗا تَلَظَّىٰ
Basi, ndikukuchenjezani za Moto woyaka mwa mphamvu.
阿拉伯语经注:
لَا يَصۡلَىٰهَآ إِلَّا ٱلۡأَشۡقَى
Sakaulowa koma (kafiri) woipitsitsa kwambiri.
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِي كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
Yemwe amatsutsa (choona) ndi kunyoza (zisonyezo za Allah).
阿拉伯语经注:
وَسَيُجَنَّبُهَا ٱلۡأَتۡقَى
Koma yemwe akuopa Allah kwambiri akatalikitsidwa ndi Moto.
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِي يُؤۡتِي مَالَهُۥ يَتَزَكَّىٰ
Amene akupereka chuma chake ndi cholinga chodziyeretsa.
阿拉伯语经注:
وَمَا لِأَحَدٍ عِندَهُۥ مِن نِّعۡمَةٖ تُجۡزَىٰٓ
Ndipo palibe aliyense kwa iye, amene adamchitira za chifundo zomwe zikulipidwa.[450]
[450] (Ndime 19-20)Tanthauzo la ma Ayah awiriwa nkuti munthu uyu sakupereka chuma chake chifukwa chobwezera chifundo cha anthu, kapena kuti adzamubwezerenso iye chifundo, koma akupereka chifukwa chofuna chikondi cha Mbuye wake basi.
阿拉伯语经注:
إِلَّا ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Koma (akuchita zimenezi) kufuna chikondi cha Mbuye wake Wapamwambamwamba.
阿拉伯语经注:
وَلَسَوۡفَ يَرۡضَىٰ
Ndipo posachedwa adzasangalala.[451]
[451] Tanthauzo lake apa ndikuti Allah adzamukondweretsa ndi malipiro Ake abwino kufikira munthuyo adzakondwera. Ma Ayah, kuyambira 17 mpaka 21, adatsika chifukwa cha Sayyidina Abu Bakr (r.a) yemwe adali kupereka chuma chake powagula akapolo omwe adali kuzunzidwa ndi mabwana awo chifukwa cholowa Chisilamu, pambuyo pake amawapatsa ufulu. Ndipo m’modzi wa iwowa ndi Sayyidina Bilal (r.a) amene adali Muazzini wa Mneneri Muhammad (s.a.w). Chomwechonso Ayah zimenezi zikumkhudza aliyense amene akugwiritsa ntchito chuma chake mnjira yopulumutsira chipembedzo.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 莱仪拉
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭