የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አሽ ሸርህ   አንቀጽ:

ሱረቱ አሽ ሸርህ

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አሽ ሸርህ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት