Check out the new design

قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: شرح   آیت:

Ash-Sharh

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
عربی تفاسیر:
وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
عربی تفاسیر:
ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
عربی تفاسیر:
وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.
عربی تفاسیر:
فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
عربی تفاسیر:
إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
عربی تفاسیر:
فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
عربی تفاسیر:
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: شرح
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا - ترجمے کی لسٹ

خالد ابراہیم پیٹالا نے ترجمہ کیا۔

بند کریں