Check out the new design

ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمه‌ى چوایی - خالد ابراهیم بيتالا * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: شرح   آیه:

Ash-Sharh

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
تفسیرهای عربی:
وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
تفسیرهای عربی:
ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
تفسیرهای عربی:
وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.
تفسیرهای عربی:
فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
تفسیرهای عربی:
إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
تفسیرهای عربی:
فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
تفسیرهای عربی:
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: شرح
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمه‌ى چوایی - خالد ابراهیم بيتالا - لیست ترجمه ها

مترجم: خالد ابراهیم بیتالا.

بستن