ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: سوره ضحى   آیه:

سوره ضحى

وَٱلضُّحَىٰ
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
تفسیرهای عربی:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا سَجَىٰ
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
تفسیرهای عربی:
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
[452] M’masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo Mtumiki (s.a.w) osamutsikira chivumbulutso. Iye poona izi adali kukaika ndi kudandaula kwakukulu, nao okanira a pa Makka adali kumchita chipongwe. Adali kumunena kuti: “Kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?’’ Basi apa Allah akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha okanira aja kuti: “Sadamusiye ndipo sadakwiye naye.”
تفسیرهای عربی:
وَلَلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لَّكَ مِنَ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
تفسیرهای عربی:
وَلَسَوۡفَ يُعۡطِيكَ رَبُّكَ فَتَرۡضَىٰٓ
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
[453] Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Allah, ndi zapadziko mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Allah adamchitira mnyengo yochepa modabwitsa.
تفسیرهای عربی:
أَلَمۡ يَجِدۡكَ يَتِيمٗا فَـَٔاوَىٰ
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
تفسیرهای عربی:
وَوَجَدَكَ ضَآلّٗا فَهَدَىٰ
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
[454] Mneneri Muhammad (s.a.w) asanapatsidwe uneneri wake ndi Allah anali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira yachiongoko.
تفسیرهای عربی:
وَوَجَدَكَ عَآئِلٗا فَأَغۡنَىٰ
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
تفسیرهای عربی:
فَأَمَّا ٱلۡيَتِيمَ فَلَا تَقۡهَرۡ
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
تفسیرهای عربی:
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنۡهَرۡ
Ndiponso wopempha usamukalipire.
تفسیرهای عربی:
وَأَمَّا بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثۡ
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: سوره ضحى
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن