Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Ad-Dhohaa (De Glorieuze Ochtend)   Vers:

Soerat Ad-Dhohaa (De Glorieuze Ochtend)

وَٱلضُّحَىٰ
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا سَجَىٰ
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
Arabische uitleg van de Qur'an:
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
[452] M’masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo Mtumiki (s.a.w) osamutsikira chivumbulutso. Iye poona izi adali kukaika ndi kudandaula kwakukulu, nao okanira a pa Makka adali kumchita chipongwe. Adali kumunena kuti: “Kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?’’ Basi apa Allah akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha okanira aja kuti: “Sadamusiye ndipo sadakwiye naye.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لَّكَ مِنَ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَسَوۡفَ يُعۡطِيكَ رَبُّكَ فَتَرۡضَىٰٓ
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
[453] Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Allah, ndi zapadziko mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Allah adamchitira mnyengo yochepa modabwitsa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَلَمۡ يَجِدۡكَ يَتِيمٗا فَـَٔاوَىٰ
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَوَجَدَكَ ضَآلّٗا فَهَدَىٰ
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
[454] Mneneri Muhammad (s.a.w) asanapatsidwe uneneri wake ndi Allah anali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira yachiongoko.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَوَجَدَكَ عَآئِلٗا فَأَغۡنَىٰ
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَأَمَّا ٱلۡيَتِيمَ فَلَا تَقۡهَرۡ
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنۡهَرۡ
Ndiponso wopempha usamukalipire.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأَمَّا بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثۡ
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Ad-Dhohaa (De Glorieuze Ochtend)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit