د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: الشرح   آیت:

الشرح

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
عربي تفسیرونه:
وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
عربي تفسیرونه:
ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
عربي تفسیرونه:
وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.
عربي تفسیرونه:
فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
عربي تفسیرونه:
إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
عربي تفسیرونه:
فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
عربي تفسیرونه:
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: الشرح
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول