Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Esh Sherh   Ajeti:

Suretu Esh Sherh

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu Esh Sherh
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll