ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: سوره حاقه   آیه:

سوره حاقه

ٱلۡحَآقَّةُ
Chakudza cha choonadi (chomwe ndi Qiyâma).
تفسیرهای عربی:
مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Kodi chakudza cha choonadi nchiyani?
تفسیرهای عربی:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Nanga nchiyani chikudziwitse za chakudza cha choonadicho?
تفسیرهای عربی:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ وَعَادُۢ بِٱلۡقَارِعَةِ
Asamudu ndi Âdi adatsutsa zakudza kwa Qiyâma (yomwe idzadzidzimutsa zolengedwa mwamphamvu ndi zoopsa zake).
تفسیرهای عربی:
فَأَمَّا ثَمُودُ فَأُهۡلِكُواْ بِٱلطَّاغِيَةِ
Tsono Asamudu adaonongedwa ndi phokoso lopyola muyeso, (lamphamvu kwambiri).
تفسیرهای عربی:
وَأَمَّا عَادٞ فَأُهۡلِكُواْ بِرِيحٖ صَرۡصَرٍ عَاتِيَةٖ
Ndipo Âdi adaonongedwa ndi chimphepo cha mkuntho, chozizira, champhamvu kwambiri.
تفسیرهای عربی:
سَخَّرَهَا عَلَيۡهِمۡ سَبۡعَ لَيَالٖ وَثَمَٰنِيَةَ أَيَّامٍ حُسُومٗاۖ فَتَرَى ٱلۡقَوۡمَ فِيهَا صَرۡعَىٰ كَأَنَّهُمۡ أَعۡجَازُ نَخۡلٍ خَاوِيَةٖ
Allah adachitumiza kwa iwo pa usiku usanu ndi uwiri ndi masana asanu ndi atatu mosadukiza; kotero ukadawaona ali lambalamba mmenemo ngati mathunthu a mitengo ya kanjedza yopanda kanthu m’kati mwake.
تفسیرهای عربی:
فَهَلۡ تَرَىٰ لَهُم مِّنۢ بَاقِيَةٖ
Kodi nanga ukumuona wotsala mwa iwo?
تفسیرهای عربی:
وَجَآءَ فِرۡعَوۡنُ وَمَن قَبۡلَهُۥ وَٱلۡمُؤۡتَفِكَٰتُ بِٱلۡخَاطِئَةِ
Ndipo Firiaun ndi amene adalipo iye asadabadwe, ndi khamu la anthu amidzi yotembenuzidwa (anthu a Luti) adadza ndi machimo (akulu).
تفسیرهای عربی:
فَعَصَوۡاْ رَسُولَ رَبِّهِمۡ فَأَخَذَهُمۡ أَخۡذَةٗ رَّابِيَةً
Ndipo (yense wa iwowa) adanyoza Mtumiki wa Mbuye wawo; choncho adawalanga chilango chopitilira muyeso.
تفسیرهای عربی:
إِنَّا لَمَّا طَغَا ٱلۡمَآءُ حَمَلۡنَٰكُمۡ فِي ٱلۡجَارِيَةِ
Ndithu pamene madzi adasefukira mopyola muyeso (mpaka kumeza mapiri nthawi ya chigumula cha Nowa) Ife tidakukwezani mchombo choyandama ndi kuyenda.
تفسیرهای عربی:
لِنَجۡعَلَهَا لَكُمۡ تَذۡكِرَةٗ وَتَعِيَهَآ أُذُنٞ وَٰعِيَةٞ
Kuti tichichite (chochitikacho chomwe okhulupirira adapulumuka nacho; osakhulupirira adaonongeka nacho) kukhala lingaliro ndi phunziro kwa inu, ndikuti lisunge (nkhaniyi) khutu losunga.
تفسیرهای عربی:
فَإِذَا نُفِخَ فِي ٱلصُّورِ نَفۡخَةٞ وَٰحِدَةٞ
Choncho likadzaimbidwa lipenga, kuimba kumodzi kokha (zamoyo zonse zidzafa).
تفسیرهای عربی:
وَحُمِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ وَٱلۡجِبَالُ فَدُكَّتَا دَكَّةٗ وَٰحِدَةٗ
Ndipo nthaka ndi mapiri nkuchotsedwa m’malo mwake ndi kuphwanyidwa kamodzi nkamodzi.
تفسیرهای عربی:
فَيَوۡمَئِذٖ وَقَعَتِ ٱلۡوَاقِعَةُ
Chomwecho tsiku limenelo, chochitika chidzachitika (imene ili Qiyâma).
تفسیرهای عربی:
وَٱنشَقَّتِ ٱلسَّمَآءُ فَهِيَ يَوۡمَئِذٖ وَاهِيَةٞ
Ndipo thambo lidzasweka choncho ilo tsiku limenelo lidzakhala lofooka (pamene lidali lolimba).
تفسیرهای عربی:
وَٱلۡمَلَكُ عَلَىٰٓ أَرۡجَآئِهَاۚ وَيَحۡمِلُ عَرۡشَ رَبِّكَ فَوۡقَهُمۡ يَوۡمَئِذٖ ثَمَٰنِيَةٞ
Ndipo angelo adzakhala m’mphepete mwake, ndipo pamwamba pawo tsiku limenero (angelo) asanu ndi atatu adzasenza Arsh (Mpando wachifumu) ya Mbuye wako.
تفسیرهای عربی:
يَوۡمَئِذٖ تُعۡرَضُونَ لَا تَخۡفَىٰ مِنكُمۡ خَافِيَةٞ
Tsiku limenelo mudzabweretsedwa ku chiweruzo; sichidzabisika chilichonse chobisika mwa inu.
تفسیرهای عربی:
فَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ فَيَقُولُ هَآؤُمُ ٱقۡرَءُواْ كِتَٰبِيَهۡ
Tsono amene adzapatsidwa kaundula wake chakudzanja lakumanja kwake adzanena (mokondwa kwa amene ali m’phepete mwake): “Tengani! Werengani kaundula wanga!”
تفسیرهای عربی:
إِنِّي ظَنَنتُ أَنِّي مُلَٰقٍ حِسَابِيَهۡ
“Ndithudi ine ndidatsimikiza (pa dziko lapansi) kuti ndidzakumana ndi chiwerengero changa.”
تفسیرهای عربی:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Choncho, iye adzakhala m’moyo wosangalatsa.
تفسیرهای عربی:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’munda wapamwamba.
تفسیرهای عربی:
قُطُوفُهَا دَانِيَةٞ
Zipatso zake zoyandikira pansi (zosavuta kuzithyola).
تفسیرهای عربی:
كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ هَنِيٓـَٔۢا بِمَآ أَسۡلَفۡتُمۡ فِي ٱلۡأَيَّامِ ٱلۡخَالِيَةِ
(Adzawauza kuti:) “Idyani, ndipo imwani mosangalala pa zimene mudatsogoza mmasiku aja adapita (a pa dziko lapansi).”
تفسیرهای عربی:
وَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِشِمَالِهِۦ فَيَقُولُ يَٰلَيۡتَنِي لَمۡ أُوتَ كِتَٰبِيَهۡ
Ndipo amene adzapatsidwe kaundula wake kudzanja lake lamanzere, adzanena (modandaula): “Kalanga ine! Ndiponi ndikadapanda kupatsidwa kaundula wangayu!”
تفسیرهای عربی:
وَلَمۡ أَدۡرِ مَا حِسَابِيَهۡ
“Nkusadziwa chiwerengero changa!”
تفسیرهای عربی:
يَٰلَيۡتَهَا كَانَتِ ٱلۡقَاضِيَةَ
“Ha! imfa ija ikadandimaliziratu (ndi kundilekanitsa ine ndi zimenezi).”
تفسیرهای عربی:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنِّي مَالِيَهۡۜ
“Chuma changa sichidandithandize!”
تفسیرهای عربی:
هَلَكَ عَنِّي سُلۡطَٰنِيَهۡ
“Mphamvu zanga (ndi moyo wanga wathanzi) zandichokera!”
تفسیرهای عربی:
خُذُوهُ فَغُلُّوهُ
(Kudzanenedwa kwa angelo oyang’anira Jahena): Mgwireni ndipo mnjateni (pomphatikiza manja ndi khosi)!
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ ٱلۡجَحِيمَ صَلُّوهُ
Kenako mponyeni ku Moto.
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ فِي سِلۡسِلَةٖ ذَرۡعُهَا سَبۡعُونَ ذِرَاعٗا فَٱسۡلُكُوهُ
Kenakonso mulowetseni mtcheni lotalika mikwamba makumi asanu ndi awiri!
تفسیرهای عربی:
إِنَّهُۥ كَانَ لَا يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndithudi, iye sadali kukhulupirira mwa Allah wamkulu.
تفسیرهای عربی:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Sadalinso kulimbikitsa zodyetsa osauka.
تفسیرهای عربی:
فَلَيۡسَ لَهُ ٱلۡيَوۡمَ هَٰهُنَا حَمِيمٞ
Basi, lero kuno alibe bwenzi (lomthandiza).
تفسیرهای عربی:
وَلَا طَعَامٌ إِلَّا مِنۡ غِسۡلِينٖ
Ngakhale chakudya kupatula mafinya (a anthu a ku Moto).
تفسیرهای عربی:
لَّا يَأۡكُلُهُۥٓ إِلَّا ٱلۡخَٰطِـُٔونَ
Zomwe palibe angazidye kupatula ochimwa (mwadala).
تفسیرهای عربی:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِمَا تُبۡصِرُونَ
Choncho ndikulumbilira zimene mukuziona.
تفسیرهای عربی:
وَمَا لَا تُبۡصِرُونَ
Ndi zimene simukuziona.
تفسیرهای عربی:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلُ رَسُولٖ كَرِيمٖ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndiliwu la mthenga wolemekezeka (Jibril).
تفسیرهای عربی:
وَمَا هُوَ بِقَوۡلِ شَاعِرٖۚ قَلِيلٗا مَّا تُؤۡمِنُونَ
Ndipo simawu a mlakatuli, ndi zochepa zimene mukuzikhulupirira.
تفسیرهای عربی:
وَلَا بِقَوۡلِ كَاهِنٖۚ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Ndiponso simawu a mlosi, ndizochepa zimene mmakumbukira!
تفسیرهای عربی:
تَنزِيلٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Ichi ndi) chivumbulutso chochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.
تفسیرهای عربی:
وَلَوۡ تَقَوَّلَ عَلَيۡنَا بَعۡضَ ٱلۡأَقَاوِيلِ
Ndipo (Mneneri) akadatipekera bodza linalake.
تفسیرهای عربی:
لَأَخَذۡنَا مِنۡهُ بِٱلۡيَمِينِ
Tikadamgwira (mwamphamvu) ndimkono wamanja.
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ لَقَطَعۡنَا مِنۡهُ ٱلۡوَتِينَ
Ndipo tikadadula mwa iye mtsempha wa moyo (kotero kuti ndikuferatu nthawi yomweyo).
تفسیرهای عربی:
فَمَا مِنكُم مِّنۡ أَحَدٍ عَنۡهُ حَٰجِزِينَ
Sipakadapezeka aliyense mwa inu womteteza (kuchilango Chathu).
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّهُۥ لَتَذۡكِرَةٞ لِّلۡمُتَّقِينَ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi phunziro labwino kwa owopa (Allah.)
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّا لَنَعۡلَمُ أَنَّ مِنكُم مُّكَذِّبِينَ
Ndithu Ife, tikudziwa kuti ena mwa inu ndiotsutsa (Qur’an).
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّهُۥ لَحَسۡرَةٌ عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo ndithu iyi (Qur’an) idzakhala chowadandaulitsa (chachikulu) osakhulupirira (pamene adzaona chilango chawo ndi mtendere wa okhulupirira).
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّهُۥ لَحَقُّ ٱلۡيَقِينِ
Ndithu iyoyi ndichoonadi Chotsimikizika; (mulibe chikaiko),
تفسیرهای عربی:
فَسَبِّحۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلۡعَظِيمِ
Basi, lemekeza dzina la Mbuye wako Wamkulu (pitiriza kutamanda dzina Lake).
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: سوره حاقه
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن